< Numeri 9 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai pa mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, nati,
Yahvé parla à Moïse dans le désert de Sinaï, le premier mois de la deuxième année après leur sortie du pays d'Égypte, et dit:
2 “Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika.
« Que les enfants d'Israël célèbrent la Pâque au temps fixé.
3 Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.”
Le quatorzième jour de ce mois, au soir, vous la célébrerez au temps fixé. Vous la célébrerez selon toutes ses lois et selon toutes ses ordonnances. »
4 Choncho Mose anawuza Aisraeli kuti azichita Paska,
Moïse dit aux enfants d'Israël qu'ils devaient célébrer la Pâque.
5 ndipo anachitadi Paskayo mʼchipululu cha Sinai madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
Ils célébrèrent la Pâque au premier mois, le quatorzième jour du mois, au soir, dans le désert du Sinaï. Les enfants d'Israël firent tout ce que Yahvé avait ordonné à Moïse.
6 Koma ena a iwo sanathe kuchita nawo Paska pa tsiku limenelo chifukwa anali odetsedwa chifukwa chokhudza mtembo. Choncho anabwera kwa Mose ndi Aaroni tsiku lomwelo,
Il y avait des hommes qui étaient impurs à cause d'un cadavre d'homme, de sorte qu'ils ne pouvaient pas célébrer la Pâque ce jour-là, et ils se présentèrent devant Moïse et Aaron ce jour-là.
7 ndipo anawuza Moseyo kuti, “Ife tadetsedwa chifukwa cha mtembo wa munthu. Nʼchifukwa chiyani taletsedwa kupereka nsembe kwa Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena pa nthawi yake?”
Ces hommes lui dirent: « Nous sommes impurs à cause du cadavre d'un homme. Pourquoi sommes-nous retenus, afin de ne pas offrir l'offrande de Yahvé au temps fixé parmi les enfants d'Israël? »
8 Mose anawayankha kuti, “Dikirani mpaka nditamva zimene Yehova walamula zokhudza Inu.”
Moïse leur répondit: « Attendez, afin que j'entende ce que l'Éternel commandera à votre sujet. »
9 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
Yahvé parla à Moïse, et dit:
10 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene wina mwa inu kapena zidzukulu zanu adetsedwa chifukwa chokhudza mtembo wa munthu, kapena akakhala pa ulendo, akhoza kuchita nawo Paska ya Yehova.
Dis aux enfants d'Israël: « Si l'un d'entre vous ou l'un de vos descendants est impur à cause d'un cadavre, ou s'il est en voyage lointain, il célébrera quand même la Pâque en l'honneur de Yahvé.
11 Azichita chikondwererochi madzulo a pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Azidya mwana wankhosa wamwamuna pamodzi ndi buledi wopanda yisiti ndi ndiwo zowawa zamasamba.
Au deuxième mois, le quatorzième jour, au soir, ils la célébreront; ils la mangeront avec des pains sans levain et des herbes amères.
12 Iwo asasiye nyama ina iliyonse mpaka mmawa. Asaswe mafupa aliwonse. Pamene akuchita chikondwerero cha Paska, atsate malangizo onse.
Ils n'en laisseront rien jusqu'au matin, et ils n'en briseront pas un os. Ils observeront toutes les règles de la Pâque.
13 Koma ngati munthu wina ali woyeretsedwa ndipo sali pa ulendo koma alephera kuchita Paska, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake chifukwa sanabweretse chopereka cha Yehova pa nthawi yake. Munthu ameneyo adzalangidwa chifukwa cha tchimo lake.
Mais l'homme qui est pur, qui n'est pas en voyage, et qui ne célèbre pas la Pâque, cette personne sera retranchée de son peuple. Parce qu'il n'a pas offert l'offrande de Yahvé au temps fixé, cet homme portera son péché.
14 “‘Mlendo amene akukhala pakati panu, nafuna kuchita nawo Paska ya Yehova, achite nawo motsata malamulo ndi malangizo ake. Muzikhala ndi malangizo ofanana a Paska; mbadwa kapena mlendo.’”
"'Si un étranger habite parmi vous et désire célébrer la Pâque en l'honneur de Yahvé, il le fera selon le statut de la Pâque et selon son ordonnance. Vous aurez un seul statut, tant pour l'étranger que pour celui qui est né dans le pays. »"
15 Pa tsiku limene anayimika chihema, tenti ya umboni, mtambo unaphimba chihemacho. Kuyambira madzulo mpaka mmawa, mtambo umene unali pamwamba pa chihemacho unkaoneka ngati moto.
Le jour où le tabernacle fut élevé, la nuée couvrit le tabernacle, la Tente du Témoignage. Le soir, elle était au-dessus du tabernacle, comme une apparence de feu, jusqu'au matin.
16 Zinkachitika motere mosalekeza: mtambo unkakhala pamwamba pa chihema, ndipo usiku unkaoneka ngati moto.
Il en était ainsi continuellement. La nuée le couvrait, et l'aspect du feu pendant la nuit.
17 Nthawi ina iliyonse mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso, ndipo paliponse pamene mtambo wayima, Aisraeli ankamangapo misasa.
Chaque fois que la nuée s'éloignait de la Tente, les enfants d'Israël partaient; et les enfants d'Israël campaient à l'endroit où la nuée restait.
18 Aisraeli ankasamuka pamalopo Yehova akawalamula, ndipo ankamanganso misasa Iyeyo akawalamula. Nthawi yonse imene mtambowo wayima pa chihema, ankakhalabe mʼmisasa yawo.
Sur l'ordre de l'Éternel, les enfants d'Israël partirent, et ils campèrent sur l'ordre de l'Éternel. Tant que la nuée resta sur le tabernacle, ils restèrent campés.
19 Mtambowo ukakhala pa chihema nthawi yayitali, Aisraeli ankasungabe lamulo la Yehova ndipo iwo sankasamukanso.
Lorsque la nuée restait plusieurs jours sur le tabernacle, les enfants d'Israël respectaient l'ordre de l'Éternel et ne voyageaient pas.
20 Nthawi zina mtambowo unkakhala pa chihemapo masiku owerengeka. Aisraeli ankamanga misasa molamulidwa ndi Yehova ndipo ankasamukanso molamulidwa ndi Iyeyo.
Parfois, la nuée restait quelques jours sur la tente; alors, selon le commandement de l'Éternel, ils restaient campés, et selon le commandement de l'Éternel, ils voyageaient.
21 Nthawi zina mtambo unkakhala kuyambira madzulo mpaka mmawa ndipo unkachoka mmawa mwake, ankasamuka. Kaya ndi masana kapena usiku, pamene mtambo wachoka, ankasamuka.
Parfois la nuée était du soir jusqu'au matin; et quand la nuée se levait le matin, ils voyageaient; ou bien, de jour et de nuit, quand la nuée se levait, ils voyageaient.
22 Ngakhale mtambo ukhale pa chihema masiku awiri kapena mwezi kapena chaka, Aisraeli ankakhalabe pa msasa osachoka. Koma ukachoka, ankasamuka.
Que la nuée soit restée sur le tabernacle pendant deux jours, un mois ou un an, les enfants d'Israël restaient campés et ne voyageaient pas; mais quand elle était levée, ils voyageaient.
23 Molamulidwa ndi Yehova ankamanga misasa yawo ndipo ankasamukanso Yehova akawalamula. Ankamvera lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.
Sur l'ordre de Yahvé, ils campaient, et sur l'ordre de Yahvé, ils voyageaient. Ils ont observé l'ordre de Yahvé, sur l'ordre de Yahvé donné par Moïse.

< Numeri 9 >