< Numeri 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
И рече Господ Мојсију говорећи:
2 “Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
Кажи Арону и реци му: Кад запалиш жишке, седам жижака нека светли напред, на свећњаку.
3 Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
И учини Арон тако, и запали жишке да светле спреда, на свећњаку, као што Господ заповеди Мојсију.
4 Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
А свећњак беше скован од злата, и ступац му и цвеће сковано; по прилици коју показа Господ Мојсију тако беше начинио свећњак.
5 Yehova anawuza Mose kuti,
Још рече Господ Мојсију говорећи:
6 “Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
Узми Левите између синова Израиљевих, и очисти их.
7 Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
А учини им ово да их очистиш: покропи их водом очишћења, а они нека обрију све тело своје и оперу хаљине своје, и очистиће се.
8 Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
Потом нека узму теле с даром уз њега, белим брашном помешаним с уљем; и друго теле узми за грех.
9 Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
Па доведи Левите пред шатор од састанка, и сазови сав збор синова Израиљевих.
10 Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
И доведи Левите пред Господа, и нека метну синови Израиљеви руке своје на Левите.
11 Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
И Арон нека принесе Левите Господу за принос од синова Израиљевих да врше службу Господу.
12 “Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
А Левити нека метну руке своје на главе теоцима, па принеси једно теле за грех а друго на жртву паљеницу Господу да се очисте Левити.
13 Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
И постави Левите пред Ароном и синовима његовим, и принеси их за принос Господу.
14 Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
И одвој Левите између синова Израиљевих да буду моји Левити.
15 “Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
А после нека дођу Левити да служе у шатору од састанка, кад их очистиш и принесеш за принос.
16 Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
Јер су мени дани између синова Израиљевих; за све што отвара материцу, за све првенце између синова Израиљевих узех њих.
17 Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
Јер је мој сваки првенац између синова Израиљевих и од људи и од стоке; онај дан кад побих све првенце у земљи мисирској, посветио сам их себи.
18 Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
А Левите узех за све првенце синова Израиљевих.
19 Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
И дадох Левите на дар Арону и синовима његовим између синова Израиљевих, да служе место синова Израиљевих у шатору од састанка, и да буду откуп за синове Израиљеве, да не би долазио помор на синове Израиљеве, кад би приступали к светињи синови Израиљеви.
20 Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
И учини Мојсије и Арон и сав збор синова Израиљевих Левитима све што заповеди Господ Мојсију за Левите, тако им учинише синови Израиљеви.
21 Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
И очистише се Левити, и опраше хаљине своје, и принесе их Арон за принос пред Господом, и очисти их Арон да би били чисти.
22 Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
А онда тек приступише Левити да врше службу своју у шатору од састанка пред Ароном и пред синовима његовим; као што заповеди Господ Мојсију за Левите, тако им учинише.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
И опет рече Господ Мојсију говорећи:
24 “Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
И ово је за Левите: од двадесет и пет година и више нека ступају у службу да служе у шатору од састанка.
25 Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
А кад коме буде педесет година, нека излази из те службе и више нека не служи.
26 Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”
Али нека служи браћи својој у шатору од састанка радећи шта треба радити, а сам нека не врши службу. Тако учини Левитима за послове њихове.

< Numeri 8 >