< Numeri 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
2 “Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
Parle à Aaron et tu lui diras: Lorsque tu auras placé les sept lampes, que le chandelier soit dressé à la partie australe. Ordonne donc que les lampes regardent contre le nord vis-à-vis de la table des pains de proposition; c’est contre cette partie que leurs le chandelier regarde, qu’elles devront luire.
3 Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
Et Aaron le fit, et il posa les lampes sur le chandelier, comme avait ordonné le Seigneur à Moïse.
4 Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
Or voici la façon du chandelier: il était d’or ductile, tant la tige du milieu, que tout ce qui sortait des deux côtés des branches: c’est selon le modèle que montra le Seigneur à Moïse, que Moïse fit le chandelier.
5 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
6 “Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
Prends les Lévites du milieu d’Israël, et tu les purifieras
7 Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
Selon ce rite: Qu’ils soient aspergés d’eau de purification, et qu’ils rasent tous les poils de leur chair. Et lorsqu’ils auront lavé leurs vêtements, et qu’ils seront purifiés,
8 Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
Ils prendront un bœuf des troupeaux, avec sa libation, de la fleur de farine arrosée d’huile: et toi, tu prendras un autre bœuf du troupeau pour le péché;
9 Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
Et tu feras approcher les Lévites devant le tabernacle d’alliance, toute la multitude des enfants d’Israël ayant été convoquée.
10 Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
Et lorsque les Lévites seront devant le Seigneur, les enfants d’Israël poseront leurs mains sur eux,
11 Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
Et Aaron offrira les Lévites en la présence du Seigneur, comme un don de la part des enfants d’Israël, afin qu’ils le servent dans son ministère.
12 “Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
Les Lévites aussi poseront leurs mains sur la tête des bœufs, dont tu sacrifieras l’un pour le péché, et l’autre pour l’holocauste du Seigneur, afin que tu pries pour eux.
13 Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
Tu présenteras ensuite les Lévites devant Aaron et ses fils, et tu les consacreras après les avoir offerts au Seigneur,
14 Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
Et tu les sépareras du milieu des enfants d’Israël, afin qu’ils soient à moi;
15 “Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
Et après cela ils entreront dans le tabernacle d’alliance, pour qu’ils me servent. Et c’est ainsi que tu les purifieras et les consacreras pour l’oblation du Seigneur, parce qu’ils m’ont été donnés en don par les enfants d’Israël.
16 Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
C’est en place des premiers-nés qui ouvrent un sein quelconque, que je les ai reçus.
17 Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
Car ils sont à moi, tous les premiers-nés des enfants d’Israël, tant des hommes que des bêtes. Depuis le jour que j’ai frappé tout premier-né dans la terre d’Egypte, je les ai consacrés pour moi;
18 Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
Et j’ai pris les Lévites au lieu de tous les premiers-nés des enfants d’Israël;
19 Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
Et j’en ai fait don à Aaron et à ses fils, les tirant du milieu du peuple, pour qu’ils me servent au lieu d’Israël dans le tabernacle d’alliance, et qu’ils prient pour eux, afin qu’il n’y ait pas de plaie sur le peuple, s’il osait approcher du sanctuaire.
20 Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
Or, Moïse et Aaron et toute la multitude des enfants d’Israël firent touchant les Lévites ce qu’avait ordonné le Seigneur à Moïse:
21 Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
Ils furent donc purifiés, et ils lavèrent leurs vêtements; et Aaron les éleva en la présence du Seigneur, et il pria pour eux,
22 Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
Afin que purifiés, ils entrassent dans le tabernacle d’alliance pour leurs fonctions devant Aaron et ses fils. Comme le Seigneur avait ordonné à Moïse touchant les Lévites, ainsi il fut lait.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
24 “Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
Voici la loi des Lévites: Depuis vingt-cinq ans et au-dessus, ils entreront pour servir dans le tabernacle d’alliance.
25 Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
Et lorsqu’ils auront accompli la cinquantième année d’âge, ils cesseront de servir,
26 Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”
Et ils seront les ministres de leurs frères dans le tabernacle d’alliance, pour garder ce qui leur aura été confié; mais les fonctions elles-mêmes, qu’ils ne les fassent point. Tu régleras ainsi pour les Lévites touchant leur garde.

< Numeri 8 >