< Numeri 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
Speak to Aaron, and thou shalt say to him, Whenever thou shalt set the lamps in order, the seven lamps shall give light opposite the candlestick.
3 Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
And Aaron did so: on one side opposite the candlestick he lighted its lamps, as the Lord appointed Moses.
4 Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
And this [is] the construction of the candlestick: [it is] solid, golden—its stem, and its lilies—all solid: according to the pattern which the Lord shewed Moses, so he made the candlestick.
5 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying,
6 “Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
Take the Levites out of the midst of the children of Israel, and thou shalt purify them.
7 Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
And thus shalt thou perform their purification: thou shalt sprinkle them with water of purification, and a razor shall come upon the whole of their body, and they shall wash their garments, and shall be clean.
8 Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
And they shall take one calf of the herd, and its meat-offering, fine flour mingled with oil: and thou shalt take a calf of a year old of the herd for a sin-offering.
9 Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
And thou shalt bring the Levites before the tabernacle of witness; and thou shalt assemble all the congregation of the sons of Israel.
10 Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
And thou shalt bring the Levites before the Lord; and the sons of Israel shall lay their hands upon the Levites.
11 Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
And Aaron shall separate the Levites for a gift before the Lord from the children of Israel: and they shall be prepared to perform the works of the Lord.
12 “Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
And the Levites shall lay their hands on the heads of the calves; and thou shalt offer one for a sin-offering, and the other for a whole-burnt-offering to the Lord, to make atonement for them.
13 Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
And thou shalt set the Levites before the Lord, and before Aaron, and before his sons; and thou shalt give them as a gift before the Lord.
14 Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
And thou shalt separate the Levites from the midst of the sons of Israel, and they shall be mine.
15 “Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
And afterwards the Levites shall go in to perform the works of the tabernacle of witness; and thou shalt purify them, and present them before the Lord.
16 Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
For these are given to me for a present out of the midst of the children of Israel: I have taken them to myself instead of all the first-born of the sons of Israel that open every womb.
17 Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
For every first-born among the children of Israel [is] mine, whether of man or beast: in the day in which I smote every first-born in the land of Egypt, I sanctified them to myself.
18 Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
And I took the Levites in the place of every first-born among the children of Israel.
19 Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
And I gave the Levites presented as a gift to Aaron and his sons out of the midst of the children of Israel, to do the service of the children of Israel in the tabernacle of witness, and to make atonement for the children of Israel: thus there shall be none among the sons of Israel to draw nigh to the holy things.
20 Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
And Moses and Aaron, and all the congregation of the children of Israel, did to the Levites as the Lord commanded Moses concerning the Levites, so the sons of Israel did to them.
21 Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
So the Levites purified themselves and washed their garments; and Aaron presented them as a gift before the Lord, and Aaron made atonement for them to purify them.
22 Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
And afterwards the Levites went in to minister in their service in the tabernacle of witness before Aaron, and before his sons; as the Lord appointed Moses concerning the Levites, so they did to them.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying,
24 “Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
This is the [ordinance] for the Levites; From five and twenty years old and upward, they shall go in to minister in the tabernacle of witness.
25 Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
And from fifty years old [the Levites] shall cease from the ministry, and shall not work any longer.
26 Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”
And his brother shall serve in the tabernacle of witness to keep charges, but he shall not do works: so shalt thou do to the Levites in their charges.

< Numeri 8 >