< Numeri 7 >

1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
Și s-a întâmplat în ziua în care Moise a ridicat în întregime tabernacolul și l-a uns și l-a sfințit pe el și toate uneltele lui, deopotrivă altarul și toate vasele acestuia și le-a uns și le-a sfințit;
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
Că prinții lui Israel, căpeteniile caselor părinților lor, care erau prinții triburilor și erau peste cei care au fost numărați, au oferit,
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
Și au adus darul lor înaintea DOMNULUI, șase care acoperite și doisprezece boi; un car pentru doi dintre prinți și pentru fiecare dintre ei un bou și i-au adus înaintea tabernacolului.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
Și DOMNUL i-a vorbit lui Moise, spunând:
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
Ia-le de la ei, ca să poată fi făcut serviciul tabernacolului întâlnirii; și să le dai leviților, fiecărui bărbat conform serviciului său.
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
Și Moise a luat carele și boii și le-a dat leviților.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
Două care și patru boi le-a dat fiilor lui Gherșon, conform serviciului lor;
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
Și patru care și opt boi le-a dat fiilor lui Merari, conform serviciului lor, sub mâna lui Itamar, fiul lui Aaron, preotul.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
Dar fiilor lui Chehat nu le-a dat nimic, deoarece serviciul sanctuarului ce le aparținea era ca ei să care pe umerii lor.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
Și prinții au adus ofrande pentru dedicarea altarului în ziua în care a fost uns, prinții au adus darul lor înaintea altarului.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
Și DOMNUL i-a spus lui Moise: Să aducă darul lor, fiecare prinț în ziua lui, pentru dedicarea altarului.
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
Și cel ce a adus darul său în prima zi a fost Nahșon, fiul lui Aminadab, din tribul lui Iuda.
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
Și darul său a fost un platou de argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă erau pline de floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină cu tămâie;
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an, ca ofrandă arsă;
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Nahșon, fiul lui Aminadab.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
În a doua zi a oferit Nataneel, fiul lui Țuar, prințul lui Isahar.
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
A adus ca dar al său, un platou din argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Nataneel, fiul lui Țuar.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a treia a oferit Eliab, fiul lui Helon, prințul copiilor lui Zabulon.
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
Darul său a fost un platou din argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an, ca ofrandă arsă;
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Eliab, fiul lui Helon.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a patra a oferit Elițur, fiul lui Ședeur, prințul copiilor lui Ruben.
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
Darul său a fost un platou din argint în greutatea de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Elițur, fiul lui Ședeur.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a cincea a oferit Șelumiel, fiul lui Țurișadai, prințul copiilor lui Simeon.
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Darul său a fost un platou din argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Șelumiel, fiul lui Țurișadai.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a șasea a oferit Eliasaf, fiul lui Deuel, prințul copiilor lui Gad.
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Darul său a fost un platou din argint în greutatea de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Eliasaf, fiul lui Deuel.
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a șaptea a oferit Elișama, fiul lui Amihud, prințul copiilor lui Efraim.
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Darul său a fost un platou din argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Elișama, fiul lui Amihud.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a opta a oferit Gamaliel, fiul lui Pedahțur, prințul copiilor lui Manase.
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Darul său a fost un platou din argint, în greutatea de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
O lingură din aur de zece șekeli, plină de tămâie;
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Gamaliel, fiul lui Pedahțur.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a noua a oferit Abidan, fiul lui Ghideoni, prințul copiilor lui Beniamin.
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
Darul său a fost un platou din argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Abidan, fiul lui Ghideoni.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
În ziua a zecea a oferit Ahiezer, fiul lui Amișadai, prințul copiilor lui Dan.
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Darul său a fost un platou din argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Ahiezer, fiul lui Amișadai.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a unsprezecea a oferit Paghiel, fiul lui Ocran, prințul copiilor lui Așer.
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Darul său a fost un platou din argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Paghiel, fiul lui Ocran.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
În ziua a douăsprezecea a oferit Ahira, fiul lui Enan, prințul copiilor lui Neftali.
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Darul său a fost un platou din argint, greutatea lui era de o sută treizeci de șekeli, un bol de argint de șaptezeci de șekeli, după șekelul sanctuarului; amândouă pline cu floarea făinii amestecată cu untdelemn, ca dar de mâncare;
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
O lingură din aur, de zece șekeli, plină de tămâie;
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un taur tânăr, un berbec, un miel de un an ca ofrandă arsă;
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un ied dintre capre ca ofrandă pentru păcat;
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
Și ca sacrificiu al ofrandelor de pace, doi boi, cinci berbeci, cinci țapi, cinci miei de un an, acesta a fost darul lui Ahira, fiul lui Enan.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
Aceasta a fost dedicarea altarului, în ziua când a fost uns, de prinții lui Israel, douăsprezece platouri de argint, douăsprezece boluri de argint, douăsprezece linguri de aur;
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
Fiecare platou din argint cântărind o sută treizeci de șekeli, fiecare bol șaptezeci, toate vasele din argint cântăreau două mii patru sute de șekeli, după șekelul sanctuarului;
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
Lingurile din aur erau douăsprezece, pline cu tămâie, cântărind zece șekeli o bucată, după șekelul sanctuarului; tot aurul lingurilor era o sută douăzeci de șekeli.
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
Toate vitele pentru ofranda arsă erau, doisprezece tauri, doisprezece berbeci, doisprezece miei de un an, împreună cu darul lor de mâncare; și doisprezece iezi dintre capre pentru ofranda pentru păcat.
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
Și toate vitele pentru sacrificiul ofrandelor de pace erau, douăzeci și patru de tauri, șaizeci de berbeci, șaizeci de țapi, șaizeci de miei de un an. Aceasta a fost dedicarea altarului, după ce a fost uns.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
Și când a intrat Moise în tabernacolul întâlnirii, ca să îi vorbească, a auzit vocea unuia vorbind de pe șezământul milei care era pe chivotul mărturiei dintre cei doi heruvimi și vorbea cu el.

< Numeri 7 >