< Numeri 7 >

1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
Kwathi uMosi eseqedile ukumisa ithabanikeli, waligcoba njalo walibusisa kanye lempahla yalo yonke. Wabuye wagcoba njalo wabusisa i-alithari kanye lezitsha zalo zonke.
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
Kwasekusithi abakhokheli bako-Israyeli, inhloko zezimuli ezazingabakhokheli zensendo ziphethe labo ababebalwa, zanikela.
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
Zaletha izipho zazo kuThixo, izinqola eziyisithupha ezembesiweyo lenkabi ezilitshumi lambili, kuyikuthi umkhokheli munye anikele ngenkabi eyodwa kuthi ababili bahlanganyele inqola eyodwa. Lokhu bakuletha ethabanikeleni.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
UThixo wathi kuMosi,
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
“Yamukela izipho ezivela kubo ukuze zisetshenziswe ethenteni lokuhlangana. Yabela abaLevi kusiya ngomsebenzi wendoda yinye ngayinye.”
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
Ngakho uMosi wathatha izinqola kanye lenkabi wazinika abaLevi.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
Wanika abakoGeshoni izinqola ezimbili kanye lenkabi ezine, kusiya ngomsebenzi wabo,
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
abakoMerari bona wabapha izinqola ezine kanye lenkabi eziyisificaminwembili, kusiya ngomsebenzi wabo. Bonke babelawulwa ngu-Ithamari indodana ka-Aroni, umphristi.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
Kodwa uMosi kazange aphe lokukodwa kumaKhohathi, ngenxa yokuthi kwakungumlandu wabo wokuthwala ngamahlombe abo zonke izinto ezingcwele.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
Ekugcotshweni kwe-alithari, abakhokheli baletha phambi kwalo iminikelo yabo yokulahlukanisela.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
Ngoba uThixo wayethe kuMosi, “Umkhokheli oyedwa ngelanga uzaletha umnikelo wakhe wokwahlukaniselwa kwe-alithari.”
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
Owaletha umnikelo wakhe ngosuku lwakuqala nguNahashoni indodana ka-Aminadabi owesizwana sakoJuda.
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva isisindo sawo singamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu oyingubhe wokuchela wesiliva, isisindo sawo ungamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili kulinganiswa ngeshekeli lendlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo ixutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa lezinyane lemvu eliduna elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane amaduna ezimvu alomnyaka owodwa, ukuze kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwaba ngumnikelo kaNahashoni indodana ka-Aminadabi.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwesibili uNethaneli indodana kaZuwari umkhokheli wabendlu ka-Isakhari, waletha umnikelo wakhe.
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
Umnikelo awulethayo: kwakungumganu wesiliva isisindo sawo ungamashekeli alikhulu elilamatshumi amathathu, lomganu owodwa wesiliva oyingubhe owokuchela olesisindo samashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili kulinganiswa ngeshekeli lendlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo ixutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane lemvu eliduna elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amahlanu alomnyaka owodwa, kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwaba ngumnikelo kaNethaneli indodana kaZuwari.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwesithathu, u-Eliyabi indodana kaHeloni, umkhokheli wabantu bakaZebhuluni, waletha umnikelo wakhe.
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo, exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna alomnyaka owodwa, kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo ka-Eliyabi indodana kaHeloni.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwesine u-Elizuri indodana kaShedewuri, umkhokheli wabantu bakaRubheni, waletha umnikelo wakhe.
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo ka-Elizuri indodana kaShedewuri.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwesihlanu uShelumiyeli indodana kaZurishadayi, umkhokheli wabantu bakaSimiyoni waletha umnikelo wakhe.
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
kanye lenkabi ezimbili, lenqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo kaShelumiyeli indodana kaZurishadayi.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwesithupha u-Eliyasafi indodana kaDuweli, umkhokheli wabantu bakaGadi, waletha umnikelo wakhe.
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo ka-Eliyasafi indodana kaDuweli.
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwesikhombisa u-Elishama indodana ka-Amihudi, umkhokheli wabantu baka-Efrayimi, waletha umnikelo wakhe.
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi igcwele impepha;
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa ukuba kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo ka-Elishama indodana ka-Amihudi.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwesificaminwembili uGamaliyeli indodana kaPhedazuri, umkhokheli wabantu bakaManase, waletha umnikelo wakhe.
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo kaGamaliyeli indodana kaPhedazuri.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwesificamunwemunye u-Abhidani indodana kaGidiyoni, umkhokheli wabantu bakaBhenjamini, waletha umnikelo wakhe.
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa, kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo ka-Abhidani indodana kaGidiyoni.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwetshumi u-Ahiyezeri indodana ka-Amishadayi, umkhokheli wabantu bakaDani, waletha umnikelo wakhe.
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa, kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo ka-Ahiyezeri indodana ka-Amishadayi.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwetshumi lanye uPhagiyeli indodana ka-Okhirani, umkhokheli wabantu baka-Asheri, waletha umnikelo wakhe.
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa, kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo kaPhagiyeli indodana ka-Okhirani.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
Ngosuku lwetshumi lambili u-Ahira indodana ka-Enani, umkhokheli wabantu bakaNafithali, waletha umnikelo wakhe.
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Umnikelo wakhe: wawungumganu wesiliva olesisindo esingamashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, lomganu wesiliva oyingubhe wokuchela olesisindo esingamashekeli angamatshumi ayisikhombisa, yomibili ibe lesilinganiso samashekeli endlu engcwele, ngamunye ugcwele ifulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha njengomnikelo wamabele;
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
inditshi yegolide eyodwa elesisindo esingamashekeli alitshumi, igcwele impepha;
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
inkunzi eliguqa, inqama eyodwa kanye lezinyane eliduna lemvu elilomnyaka owodwa, kungumnikelo wokutshiswa;
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
impongo eyodwa kungumnikelo wesono;
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
kanye lenkabi ezimbili, inqama ezinhlanu, impongo ezinhlanu kanye lamazinyane ezimvu amaduna amahlanu alomnyaka owodwa, kube ngumhlatshelo womnikelo wobudlelwano. Lo kwakungumnikelo ka-Ahira indodana ka-Enani.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
Le yayiyiminikelo yabakhokheli bako-Israyeli yokwahlukaniselwa kwe-alithari mhla ligcotshwa: imiganu elitshumi lambili yesiliva, imiganu yokuchela yesiliva eyingubhe elitshumi lambili kanye lenkezo zegolide ezilitshumi lambili.
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
Umganu munye wesiliva ulesisindo samashekeli alikhulu lamatshumi amathathu, njalo umganu oyingubhe wokuchela ngamunye ulesisindo samashekeli angamatshumi ayisikhombisa. Sezihlangene, izitsha zesiliva zazilesisindo esingamashekeli azinkulungwane ezimbili lamakhulu amane, kulinganiswa ngesisindo seshekeli lendlu engcwele.
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
Izinditshi ezilitshumi lambili zegolide zigcwele impepha zilesisindo samashekeli alitshumi inye, kulinganiswa ngesisindo seshekeli lendlu engcwele. Sezindawonye, inkezo zegolide zilesisindo samashekeli alikhulu elilamatshumi amabili.
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
Inani lezinyamazana zonke ezomnikelo wokutshiswa zazibalisa itshumi lambili lenkunzi ezingamaguqa, itshumi lambili lenqama kanye letshumi lambili lamazinyane ezimvu amaduna alomnyaka owodwa, kanye lomnikelo wazo wamabele. Impongo ezilitshumi lambili zaba ngezomnikelo wesono.
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
Sezihlangene zonke izinyamazana zomhlatshelo womnikelo wobudlelwano kwaba zinkabi ezingamatshumi amabili lane, inqama ezingamatshumi ayisithupha, impongo ezingamatshumi ayisithupha kanye lamazinyane amaduna ezimvu alomnyaka owodwa angamatshumi ayisithupha. Le kwakuyiminikelo yokwahlukaniselwa kwe-alithari emva kokugcotshwa kwalo.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
Kwathi uMosi engena ethenteni lokuhlangana ukuba ayekhuluma loThixo, wezwa ilizwi likhuluma laye liphuma sengathi liphahlwe ngamakherubhi amabili ngaphezu kwesisibekelo sesihlalo somusa, phezu kwebhokisi lobuFakazi. Wasekhuluma laye.

< Numeri 7 >