< Numeri 7 >
1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
Lorsque Moïse eut achevé de dresser la Demeure, et qu'il l'eut ointe et consacrée avec tous ses ustensiles, lorsqu'il eut aussi oint et consacré l'autel et tous ses ustensiles,
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
Les principaux d'Israël, chefs des familles de leurs pères, c'est-à-dire les princes des tribus, ceux qui avaient présidé au dénombrement, firent leur offrande.
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
Ils amenèrent donc leur offrande devant l'Éternel: six chariots en forme de litières, et douze taureaux; un chariot pour deux princes, et un taureau pour chacun, et ils les offrirent devant la Demeure.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
Alors l'Éternel parla à Moïse, en disant:
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
Prends d'eux ces choses, et qu'elles soient employées au service du tabernacle d'assignation; et donne-les aux Lévites, à chacun selon son service.
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
Moïse prit donc les chariots et les taureaux, et les donna aux Lévites.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
Il donna aux enfants de Guershon deux chariots et quatre taureaux, selon leur service.
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
Et il donna aux enfants de Mérari quatre chariots et huit taureaux, selon leur service, sous la conduite d'Ithamar, fils d'Aaron, le sacrificateur.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
Mais il n'en donna point aux enfants de Kéhath parce qu'ils étaient chargés du service des choses saintes; ils les portaient sur leurs épaules.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
Et les princes firent une offrande pour la dédicace de l'autel, au jour qu'il fut oint; les princes apportèrent leur offrande devant l'autel.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
Et l'Éternel dit à Moïse: Qu'un prince apporte son offrande un jour, et un autre, un autre jour, pour la dédicace de l'autel.
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
Et celui qui offrit son offrande le premier jour fut Nahasshon, fils d'Amminadab, de la tribu de Juda.
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles pleine de parfum;
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande de Nahasshon, fils d'Amminadab.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
Le second jour, Nathanaël, fils de Tsuar, prince d'Issacar, fit son offrande;
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
Il offrit: un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande de Nathanaël, fils de Tsuar.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
Le troisième jour, ce fut le prince des enfants de Zabulon, Éliab, fils de Hélon.
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande d'Éliab, fils de Hélon.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
Le quatrième jour, ce fut le prince des enfants de Ruben, Elitsur, fils de Shedéur.
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande d'Elitsur, fils de Shedéur.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
Le cinquième jour, ce fut le prince des enfants de Siméon, Shelumiel, fils de Tsurishaddaï.
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande de Shelumiel, fils de Tsurishaddaï.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
Le sixième jour, ce fut le prince des enfants de Gad, Eliasaph, fils de Déhuël.
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande d'Eliasaph, fils de Déhuël.
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
Le septième jour, ce fut le prince des enfants d'Éphraïm, Elishama, fils d'Ammihud.
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande d'Elishama, fils d'Ammihud.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
Le huitième jour, ce fut le prince des enfants de Manassé, Gamaliel, fils de Pedahtsur.
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum,
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande de Gamaliel, fils de Pedahtsur.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
Le neuvième jour, ce fut le prince des enfants de Benjamin, Abidan, fils de Guideoni.
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année pour l'holocauste;
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande d'Abidan, fils de Guideoni.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
Le dixième jour, ce fut le prince des enfants de Dan, Ahiézer, fils d'Ammishaddaï.
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande d'Ahiézer, fils d'Ammishaddaï.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
Le onzième jour, ce fut le prince des enfants d'Asser, Paguiel, fils d'Ocran.
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande de Paguiel, fils d'Ocran.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
Le douzième jour, ce fut le prince des enfants de Nephthali, Ahira, fils d'Enan.
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Son offrande fut un plat d'argent, du poids de cent trente sicles, un bassin d'argent de soixante et dix sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fine farine pétrie à l'huile, pour l'oblation;
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Une coupe d'or de dix sicles, pleine de parfum;
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Un jeune taureau, un bélier, un agneau de l'année, pour l'holocauste;
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Un bouc pour le sacrifice pour le péché;
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
Et pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq jeunes boucs, cinq agneaux d'un an. Telle fut l'offrande d'Ahira, fils d'Enan.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
Voilà ce qu'on reçut des princes d'Israël pour la dédicace de l'autel, lorsqu'il fut oint: Douze plats d'argent, douze bassins d'argent, douze coupes d'or;
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
Chaque plat d'argent était de cent trente sicles, et chaque bassin de soixante et dix. Tout l'argent des vases fut de deux mille quatre cents sicles selon le sicle du sanctuaire.
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
Douze coupes d'or, pleines de parfum, chacune de dix sicles, selon le sicle du sanctuaire. Tout l'or des coupes fut de cent vingt sicles.
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
Tous les taureaux pour l'holocauste, furent douze jeunes taureaux, avec douze béliers, douze agneaux d'un an, avec leurs oblations, et douze boucs, pour le sacrifice pour le péché;
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
Tous les taureaux du sacrifice de prospérités furent vingt-quatre jeunes taureaux, avec soixante béliers, soixante jeunes boucs, soixante agneaux d'un an. Telle fut la dédicace de l'autel, après qu'il eut été oint.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
Or quand Moïse entrait au tabernacle d'assignation, pour parler avec Dieu, il entendait la voix lui parlant de dessus le propitiatoire, qui était sur l'arche du Témoignage, d'entre les deux chérubins; et il lui parlait.