< Numeri 7 >
1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
Da Moses var færdig med at rejse Boligen og havde salvet og helliget den med alt dens Tilbehør og ligeledes salvet og helliget Alteret med alt dets Tilbehør,
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
traadte Israels Øverster, Overhovederne for deres Fædrenehuse, Stammernes Øverster, der havde forestaaet Mønstringen, frem
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
og førte deres Offergave frem for HERRENS Aasyn, seks lukkede Vogne og tolv Stykker Hornkvæg, en Vogn for hver to Øverster og et Stykke Hornkvæg for hver een, og de bragte dem hen foran Boligen.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
Da sagde HERREN til Moses:
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
Modtag dette af dem, for at det kan bruges til Arbejdet ved Aabenbaringsteltet, og giv Leviterne det med Henblik paa hver enkeltes særlige Arbejde!
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
Saa modtog Moses Vognene og Hornkvæget og gav Leviterne dem.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
To Vogne og fire Stykker Hornkvæg gav han Gersoniterne med Henblik paa deres særlige Arbejde,
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
og fire Vogne og otte Stykker Hornkvæg gav han Merariterne med Henblik paa deres særlige Arbejde under Itamars, Præsten Arons Søns, Ledelse.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
Derimod gav han ikke Kehatiterne noget, thi dem var Arbejdet med de hellige Ting overdraget, og de skulde bære dem paa Skuldrene.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
Fremdeles bragte Øversterne Offergaver til Alterets Indvielse, dengang det blev salvet, og Øversterne bragte deres Offergaver hen foran Alteret.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
Da sagde HERREN til Moses: Lad hver af Øversterne faa sin Dag til at bringe sin Offergave til Alterets Indvielse.
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
Den, som første Dag bragte sin Offergave, var Nahasjon, Amminadabs Søn af Judas Stamme.
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
Og hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Nahasjons, Amminadabs Søns, Offergave.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
Anden Dag bragte Netan'el, Zuars Søn, Issakars Øverste, sin Offergave;
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
han bragte som Offergave et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Netan'els, Zuars Søns, Offergave.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
Tredje Dag kom Zebuloniternes Øverste, Eliab, Helons Søn;
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Eliabs, Helons Søns, Offergave.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
Fjerde Dag kom Rubeniternes Øverste, Elizur, Sjede'urs Søn;
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder,
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
et aargammelt Lam til Brændoffer, en Gedebuk til Syndoffer
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Elizurs, Sjede'urs Søns, Offergave.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
Femte Dag kom Simeoniternes Øverste, Sjelumiel, Zurisjaddajs Søn;
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Sjelumiels, Zurisjaddajs Søns, Offergave.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
Sjette Dag kom Gaditernes Øverste, Eljasaf, De'uels Søn;
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
hans Offergaver et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Eljasafs, De'uels Søns, Offergave.
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
Syvende Dag kom Efraimiternes Øverste, Elisjama, Ammihuds Søn:
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Elisjamas, Ammihuds Søns, Offergave.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
Ottende Dag kom Mannassiternes Øverste, Gamliel, Pedazurs Søn;
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Gamliels, Pedazurs Søns, Offergave.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
Niende Dag kom Benjaminiternes Øverste, Abidan, Gid'onis Søn;
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem, Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Abidans, Gid'onis Søns, Offergave.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
Tiende Dag kom Daniternes Øverste, Ahiezer, Ammisjaddajs Søn;
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Ahiezers, Ammisjaddajs Søns, Offergave.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
Ellevte Dag kom Aseriternes Øverste, Pag'iel, Okrans Søn;
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Pag'iels, Okrans Søns, Offergave.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
Tolvte Dag kom Naftaliternes Øverste, Ahira, Enans Søn;
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
hans Offergave var et Sølvfad, der vejede 130 Sekel, og en Sølvskaal paa 70 Sekel efter hellig Vægt, begge fyldte med fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer,
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
en Kande paa 10 Guldsekel, fyldt med Røgelse,
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
en ung Tyr, en Væder, et aargammelt Lam til Brændoffer,
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
en Gedebuk til Syndoffer
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
og til Takoffer to Stykker Hornkvæg, fem Vædre, fem Bukke og fem aargamle Lam. Det var Ahiras, Enans Søns, Offergave.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
Det var Gaverne fra Israeliternes Øverster til Alterets Indvielse, dengang det blev salvet: 12 Sølvfade, 12 Sølvskaale, 12 Guldkander,
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
hvert Sølvfad paa 130 Sekel og hver Sølvskaal paa 70 Sekel, alle Sølvkar tilsammen 2400 Sekel efter hellig Vægt;
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
12 Guldkander, fyldte med Røgelse, hver paa 10 Sekel efter hellig Vægt, alle Guldkander tilsammen 120 Sekel.
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
Kvæget til Brændofferet var i alt 12 unge Tyre, 12 Vædre, 12 aargamle Lam med tilhørende Afgrødeofre, 12 Gedebukke til Syndoffer;
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
Kvæget til Takofferet var i alt 24 unge Tyre, 60 Vædre, 60 Bukke og 60 aargamle lam. Det var Gaverne til Alterets Indvielse, efter at det var salvet.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
Da Moses gik ind i Aabenbaringsteltet for at tale med HERREN, hørte han Røsten tale til sig fra Sonedækket oven over Vidnesbyrdets Ark, fra Pladsen mellem de to Keruber. Og han talede til ham.