< Numeri 7 >

1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
Mose chun houbuh atundoh nichun thao anun, atheng in atum koi tai. Aman thilkeo jouse jong thao anun, houbuh sung manchahho, maicham phung leh athilkeo ho jong atheng in atum akoi tai.
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
Chuin Israelte lamkai ho - akilom a um miho min jihlut a pang phung lamkaiho- ahung un, ama ama thilto ahin pohlut cheh uvin ahi.
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
Amahon abonchauvin Sakol kangtalai lentahtah gup toh Bongchal Somle ni ahin kaiyun ahi. Sakol kangtalai khat chu lamkai ni a ahin, Bongchal khat cheh chu Lamkai khat cheh a ahi. Hicheho cheng hi Pakai a ding Houbuh mai a chun apeuvin ahi.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
Chuin Pakaiyin Mose kom a seiyin,
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
“Thilpeh hochu sang in, Sakol kangtalai leh bongchalho chu houbuh pohle na a nanei ding ahi. Levite chu atoh dungjui cheh un homkhen in.”
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
Hitichun Mosen kangtalaiho leh bongchal ho chu Levite apetan ahi.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
Mosen Kangtalai ni le Bongchal li chu Gershonten anatohnauva amanchah ding uvin apetan ahi,
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
Chuleh Kangtalai li le Bongchal get chu Merariten anatoh nauva amanchah ding uvin apetai. Na kitong jouse aboncha a thempu Aaron chapa Ithamar vaihom nanoiya umsoh kei ahi.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
Ahinlah Houbuh a kimang cha thil theng hochu alengkou uva apoh ding u ahijeh chun Kohatte vangchu kangtalaiho le Bongchalho imacha apepon ahi.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
Lamkaiho jousen jong kilhanthengna thilpeh ahin kichoi cheh uvin, kisuhtheng nikho chun maicham phung nga akoi cheh tauve.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
Pakaiyin Mose kom a aseiyin, “Maicham kithensona ding in lamkai khat in thilpeh khat cheh hintoh hen.”
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
Nikho masapen tah chu Nahson kiti Aminadab chapa Judah phung lamkai chun maicham a ahin pelut in ahi.
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
Nahson in ahinto doh thilho chu sum-eng lheng, agihdan shekel jakhat le somthum a gih chule sum-eng lheng khat houin sung nga dangka kholna ahin, hiche ho jouse hi changbong kitahna chule chanbong neljet Olive thao toh ania kisung dim cheh ahiye.
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Nahson chun sana a kisem thilkoina li gimnamtui dimset chu ahin choiyin ahiye.
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Nahson in Bongnou khat toh, kumkhat lhingsa kelngoi chal chu pumgo maicham ding in,
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
Chule kelchal khat chu chonset kithoina maichama pang ding in ahin kai in ahi.
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
Chamna maicham adin Bongchal ni, kelngoi achal lhingset nga, kelchal nga, kelngoi kumkhat lhingsa hochu ahinkai in ahi. Hichengse hi Amminadab chapa Nahson in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
Nikhoni lhinni in Zuar chapa Nethanel, Issachar phung lamkai pan, amaicham ahintoh doh in ahi.
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
Ama hinto ho chu, sum-eng hopthum ahin tohdoh in chule sum-eng kong khat sopna agih diu khat hichu houin nathilgih tetoh na kila ahi. Hiche sum-eng kong tuihi chang bong kitang Olive thao kisun khum ahiye.
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
chuleh sana a kisem thilkoina gimnamtui dimset ahi.
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Zuar chapa Nethenel in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
Anithum lhinnin Helon chapa Eliab, Zebulunte phung lamkai pan jong amaicham ahin tohdoh in ahi.
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
Ama hinto ho chu, sum-eng hopthum ahin tohdoh in chule sum-eng kong khat sopna agih diu khat hichu houin nathilgih tetoh na kila ahi. Hiche sum-eng kong tuihi chang bong kitang Olive thao kisun khum ahiye.
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
chuleh sana a kisem thilkoina gimnamtui dimset ahi.
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Helon chapa Eliab in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
Nili lhinnin Sheduer chapa Elizur, Reuben phung lamkai pan jong amaicham ahin tohdoh in ahi.
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
Aman sum-eng kong khat chule houbuh sunga thiltena kitetoh chat ahin, hihcu changbong jaona Olive thao toh kihel khomma ahiye.
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Eliazur in jong sana dangka kong ahin choijin hichu gimnamtui jaona ahi.
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Sheduer chapa Elizur in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
Ni-nga lhinna in Zurisaddi chapa Shelumiel, Simeon phung Lamkai pan jong amaicham ahin tohdoh in ahi.
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Shelumeul chun maicham hohi sum-eng kong tong gihtah ahin, amaho shelul kitena dungjuiyin Houin sunga kimanchahna bang chun changbong neldijet Olive thaotoh kihel chu ahiye.
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
Sana dangka kong jing ahin kitetoh in agih Gram li tobang ahin hiche chu gimnamtui a dimset e.
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Zurisaddi chapa Shelumiel in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
Ni-gup lhinnin Deuel chapa Eliasaph, Gad phung Lamkaipan jong amaicham ahin tohdoh in ahi.
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Phung lamkai dang hon atobang chun Eliasaph in jong lhingsel in a maicham ho ahin kipeh lut e. Sum-eng changbong neldi jet jaona hichu Olive thaotoh kihelsoh keija ahiye.
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Eliasaph in Sana dangka jaonan gimnam tui dimsetna kikoi chu ahintoh doh in ahi.
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Eliasaph chapa Deuel in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
Nisagi lhinna in Amihud chapa Elishaph, Ephraimte phung Lamkaipan jong amaicham ahin tohdoh in ahi.
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Amachu phung sagi hou lamkai cheh in atodoh u akibang chet in sum-eng chang bong ho chu Olive thaova kihel soh keija ahiye.
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Elishamma in sana dangka chule gim namtui tui dimsetna kikoi ahi.
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Amihud chapa Elisaph in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
Niget lhina in Pedazur Chapa Gamaliel, Manassehte phung lamkaipan jong amaicham ahin tohdoh in ahi.
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
to consider
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
Todoh maicham phung sung hotoh aki bang chat nalaiyin ahi.
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Amihud chapa Elisaph in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
Niko lhinnah in Gideon chapa Abidan, Benjamin phunga Lamkai pan amaicham ahin tohdoh in ahi.
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
to reconsider
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Chuleh kelchal khat chonset maicham kilhainan apang in ahi.
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Gideon chapa Abidan in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
Nisom lhinna in, Ammishaddai chapa Ahiezer, Dan phung lamkaipan amaicham ahin tohdoh in ahi.
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Ahiezer lin maichamma ahin todoh hiche hohi ahiye. Sum-eng khon sopna Israelte houdan thua thiltena toh kitohchetna kite, changbong deitah ki subong chule kisuh neldijet Olive thao toh kinu khom ding ahi.
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Ahiezer kite Amishaddai chapa in Sana dangka chule gim namtui thao jaonan ahin tohdoh in ahi.
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Ammishaddai chapa Ahiezer in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
Nisomlehkhat lhin in Ocran chapa Pagiel, Asher phung lamkai pan anoija hohi maicham a din ahin tohdoh e.
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Sumeng khon sopna theija gih hiche sum-eng lhengkong tunna chu leh changbong neldisel jaona hichu Olive thao toh kihal ding ahi.
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Sana dangka le lhengkong chule gimnamtui dimset jao nan ahin toh e.
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Bongchal nou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Ocran chapa Pagiel in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
Nisom le ni lhinna in Enan chapa Ahira, Napthali phung lamkaipan amaicham ahin tohdoh in ahi.
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Ahira maicham ho sum eng jaonan chang bong hichu Olive thao jaonan ahin todoh ahi.
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Ahira in sana dangka jaonan gimnamtui toh ahin toh doh in ahi.
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Bongchal anou khat, kelchal khat chule kelngoi achal kum khat lhingsa chu pumgo maichamma a ding in,
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
chule kelchal khat chonset kithoina maicham a pang ding in ahinkai in ahi.
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
Chamna maicham a din Bongchal ni, kelngoichal lhingset nga, kelchal nga, chule kelngoi kumkhat lhingsel-nga ahin kai in ahi. Hichengse hi Enan chapa Ahira in kilhaina thilto a ahinto ho chu ahiye.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
Israel a phung lamkai hon maichamphung thao ana kinu a kilhandohna maicham dia ahintodoh hou chu: Sumeng lheng kong len som le ni, Sumeng kisilna kong som le ni, Gimnamtui kikholna Sana lhengkongho ahiuve.
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
Houintheng a shekel kitena a ilep leh Sumeng lhengkong len khat gihdan chu 3-1/4 pounds ahin chuleh Sumeng kisilna kong khat gihdan chu 1-3/4 pounds ahi. Sumeng mong mong agihdan chu 60 pounds ahi.
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
Houintheng a shekel kitena a ilep leh Sana lhengkong somleni khat cheh gimnamtui jaona a agihdan chu 4 ounces ahin. Sana mong mong agom a agihdan chu 3 pounds ahi.
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
Bongchal anou somleni, kelngoi achal lhingset somleni, kum khat lhing cheh kelngoi achal som le ni pumgo thilto a ding in ahung kitoh in, todoh ding a umsa lhosoh maicham jong ahi. Chonset kilheina maicham ding in kelcha achal som le ni ahung kikailut in ahi.
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
Chamna maicham ding in Bongchal somni le li, kelngoi achal lhingset somgup, kelchal somgup, kumkhat lhingsa kelngoi chal somgup ahung kitohdoh in ahi. Hicheng hi maicham phung thao akinu jouva maicham phung a dia kikatdohna maicham dia hung kitohho ahi.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
Mose chu Pakai toh kihou ding a Houbuh sunga alutji teng, aman houpina awgin thingkhong akhu (Themmona akon a themchanna mun - Kitepna thingkhong chung a kinga) chung a Cherubim teni lailung a kon chun aja jin ahi. Hiche lai mun a kon a chu Pakai in amachu ahin houpi ji ahiye.

< Numeri 7 >