< Numeri 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
Speak unto the children of Israel, and say unto them, If a man or a woman have vowed the special vow of a Nazarite, to consecrate themselves to Jehovah;
3 sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
he shall separate himself from wine and strong drink: he shall drink no vinegar of wine, nor vinegar of strong drink, neither shall he drink any liquor of grapes, nor eat grapes, fresh or dried.
4 Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
All the days of his separation shall he eat nothing that is made of the vine, from the seed-stones, even to the skin.
5 “‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
All the days of the vow of his separation there shall no razor come upon his head; until the days be fulfilled, that he hath consecrated himself to Jehovah, he shall be holy; he shall let the locks of the hair of his head grow.
6 Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
All the days that he hath consecrated himself to Jehovah, he shall come near no dead body.
7 Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
He shall not make himself unclean for his father, or for his mother, for his brother, or for his sister when they die; for the consecration of his God is upon his head.
8 Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
All the days of his separation he is holy to Jehovah.
9 “Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
And if any one die unexpectedly by him suddenly, and he hath defiled the head of his consecration, then he shall shave his head on the day of his cleansing; on the seventh day shall he shave it.
10 Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
And on the eighth day he shall bring two turtle-doves, or two young pigeons, to the priest, at the entrance of the tent of meeting.
11 Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
And the priest shall offer one for a sin-offering, and the other for a burnt-offering, and make an atonement for him, for that he sinned by the dead person; and he shall hallow his head that same day.
12 Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
And he shall [again] consecrate to Jehovah the days of his separation, and shall bring a yearling lamb for a trespass-offering. But the first days are forfeited, for his consecration hath been defiled.
13 “Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
And this is the law of the Nazarite on the day when the days of his consecration are fulfilled: he shall be brought to the entrance of the tent of meeting.
14 Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
And he shall present his offering to Jehovah, one yearling he-lamb without blemish for a burnt-offering, and one yearling ewe-lamb without blemish for a sin-offering, and one ram without blemish for a peace-offering;
15 ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
and a basket with unleavened bread, cakes of fine flour mingled with oil, and unleavened wafers anointed with oil, and their oblation, and their drink-offerings.
16 “Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
And the priest shall present them before Jehovah, and shall offer his sin-offering and his burnt-offering:
17 Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
and he shall offer the ram, a sacrifice of peace-offering to Jehovah, with the basket of unleavened bread; the priest shall offer also his oblation and his drink-offering.
18 “Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
And the Nazarite shall shave the head of his consecration at the entrance to the tent of meeting, and shall take the hair of the head of his consecration, and put it on the fire which is under the sacrifice of the peace-offering.
19 “Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
And the priest shall take the boiled shoulder of the ram, and one unleavened cake out of the basket, and one unleavened wafer, and shall put them upon the hands of the Nazarite, after he hath shaven [the hair of] his consecration.
20 Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
And the priest shall wave them as wave-offering before Jehovah; it is holy for the priest, with the breast of the wave-offering and with the shoulder of the heave-offering; and afterwards the Nazarite may drink wine.
21 “Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
This is the law of the Nazarite who hath vowed: his offering to Jehovah for his consecration, beside what his hand is able to get; according to the vow which he vowed, so shall he do, according to the law of his consecration.
22 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
23 “Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
Speak unto Aaron and unto his sons, saying, On this wise ye shall bless the children of Israel: saying unto them,
24 “‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
Jehovah bless thee, and keep thee;
25 Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
Jehovah make his face shine upon thee, and be gracious unto thee;
26 Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
Jehovah lift up his countenance upon thee, and give thee peace.
27 Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.
And they shall put my name upon the children of Israel; and I will bless them.

< Numeri 6 >