< Numeri 6 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
BAWIPA ni Mosi hah a pato teh,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
Isarel catounnaw koe dei pouh. Ahnimouh koe tongpa thoseh, napui thoseh BAWIPA koe ama Nazirite lawkkamnae la hanlah, a kâkapek teh a kâhmoun toteh,
3 sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
misur hoi yamu tek mahoeh. Misurtui hoi yamucang hai net mahoeh. Misurtui nei e hoi misurpaw katha e khumbei dawk vaw teh kamyai e hai cat mahoeh.
4 Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
A kâkapek nah yunglam pueng teh misurkung dawk hoi a mu thoseh, atui thoseh cat awh mahoeh.
5 “‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
A kâkapeknae lawk a kam nah thung pueng teh, a lû ngaw mahoeh. BAWIPA hmalah a kâpeknae hnin a pha hoehroukrak teh kathounge lah ao han. Hottelah a sam a hlung vaiteh, a sai sak han.
6 Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
BAWIPA hanlah a kâkapeknae thung pueng teh, tami ro koe hnai mahoeh.
7 Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
A na pa thoseh, a manu thoseh, a hmaunawngha thoseh, a tawncanu thoseh, a duenae kong dawk hai kâkhinsak hanh naseh. Bangkongtetpawiteh, Cathut hanlah a kâkapeknae a lû dawk ao.
8 Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
A kâkapek yunglam teh BAWIPA hanlah kathounge lah ao han.
9 “Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
Ateng vah, pouk laipalah tami koe dout pawiteh, a kâkapeknae a lû dawk khin sak pawiteh, a kamthoung nah hnin vah, a lû a ngaw vaiteh, a hnin sari hnin vah a pâkhamuen a ngaw han.
10 Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
A hnin taroe hnin vah, kamkhuengnae lukkareiim takhang koe e vaihma koe bakhu kahni touh thoseh, Âbakhu kahni touh thoseh a sin awh han.
11 Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
Vaihma ni buet touh teh yon thueng nahanlah a poe vaiteh, alouke buet touh teh hmaisawi thueng nahan, tami kadout kecu dawk a sakpayon e dawk a yontha nahanlah a sak pouh han. Hot hnin vah a lû hah a thoung sak han.
12 Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
Hahoi kâtapoe thuengnae dawkvah kum touh ka pha e tuca a tan a thokhai vaiteh, kâkapeknae hnin teh BAWIPA koe vah a katha lah a tâcokhai han. Bangkongtetpawiteh, kâkapeknae hah a khin sak toung dawkvah, ahmaloe e teh banglah tho mahoeh toe.
13 “Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
Hahoi Nazirite a kâkapeknae hnin a kuep toteh, a sak awh hane kâlawk doeh. Kamkhuengnae lukkareiim takhang koe na ceikhai awh han.
14 Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
Hahoi BAWIPA koe thuengnae hah a poe han. Tutan kacueme hmaisawi thuengnae koe buet touh, yon thueng nahanelah tulaca kacueme buet touh, roum thueng nahanelah, kacueme tutanca buet touh,
15 ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
tonphuenhoehe tavai hah a kanui e tavai satui hoi kanawk e tavai tueng buet touh satui hluk e tavai ka rapamca e a tabu buet touh, tavai thuengnae hoi lannae thueng hoi na poe awh han.
16 “Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
Hahoi vaihma ni tavai hah BAWIPA hmalah a thokhai vaiteh, yon thuengnae hoi hmaisawi thuengnae hah a poe han.
17 Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
Hahoi tutan hah tonphuenhoehe tavai tabu dawk hoi roum thuengnae hah Bawipa koe a poe han. Vaihma ni tavai thuengnae, nei thuengnae hoi a poe sin han.
18 “Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
Nazirite tami ni, kamkhuengnae lukkareiim takhang koe a sam hah a ngaw vaiteh, roum thuengnae a saknae koe hmai hoi a sawi han.
19 “Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
Hahoi vaihma ni tutan e a loung a thawng e hoi tonphuenhoehe a tabu dawk a ta e vaiyei buet touh, tonphuenhoehe vaiyei ka rapam e phen buet touh, a la vaiteh, Nazirite niyah a kâhmounnae a sam koung a ngaw hnukkhu hoi a kut dawk a ta han.
20 Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
Hahoi vaihma ni kahek thuengnae dawkvah, BAWIPA hmalah a kahek han. Hetheh vaihma hmang lah kaawm han. Hetheh vaihma e ham lah kaawm han. Kahek e a takuep hoi a kahek e a phai teh a thoung han, hahoi teh Nazirite tami ni misur a nei thai han toe, telah a ti.
21 “Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
Hetheh Nazirite lawkkam a kâhmounnae hoi poehno e BAWIPA koe lawkkamnae kasakkung e kâlawk lah ao. Hothloilah a ma kut hoi ka dam sak e pueng hah lawkkamnae a sak e patetlah a kâhmounnae kâlawk patetlah a sak roeroe han.;
22 Yehova anawuza Mose kuti,
BAWIPA ni Mosi hah a pato teh,
23 “Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
Aron hoi a capanaw koevah, het patetlah Isarel catounnaw yawhawi na poe han, ahnimouh koe,
24 “‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
BAWIPA ni yawhawi na poe awh teh, na khenyawn awh naseh.
25 Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
BAWIPA ni a minhmai nangmouh koe kho lah a sei vaiteh, na pahren awh naseh.
26 Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
BAWIPA teh nangmouh koelah kangvawi seh, roumnae na poe awh han, telah dei pouh awh telah a dei.
27 Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.
Hot patetlah sak e ni Isarel catounnaw koe ka min a kamnue sak awh han. Kai ni ahnimouh teh yawhawi ka poe han, telah a ti.