< Numeri 6 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Господ говори още на Моисея, казвайки:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
Говори на израилтяните, казвайки им: Когато мъж или жена направи изричен обрек на назирейство, за да посвети себе си Господу,
3 sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
тогава да се отказва от вино и от спиртни питиета, да не пие оцет от вино или оцет от спиртни питиета, нито да пие какво да е питие направено от грозде, нито да яде прясно или сухо грозде.
4 Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
През всичкото време на назирейството си да не яде нищо, което се прави от лозе, от зърното до ципата.
5 “‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
През всичкото време на назирейския си обрек да не тури бръснач на главата си; догдето се изпълни времето, което е обрекъл Господу, ще бъде свет, и нека остави да растат космите на главата му.
6 Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
През всичкото време на обрека си, че ще бъде назирей Господу, да не се приближи при мъртвец;
7 Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
да се не оскверни, заради баща си или майка си, брата си или сестра си, когато умрат; понеже назирейският обрек на Бога му е на главата му.
8 Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
През всичкото време на назирейството си той е свет Господу.
9 “Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
И ако някой умре ненадейно при него, и главата на назирейството му се оскверни, тогава, в деня на очищението си, той да обръсне главата си; на седмия ден да я обръсне.
10 Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
А на осмия ден да донесе две гургулици или две гълъбчета при свещеника при входа на шатъра за срещане;
11 Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
и свещеникът да принесе едното в принос за грях, а другото за всеизгаряне; и да направи умилостивение за него, понеже е съгрешил поради мъртвеца, и в същия ден да освети главата му.
12 Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
След това изново да посвети Господу дните на назирейството си и да донесе едногодишно агне в принос за престъпление; а по-предишните дни няма да се считат, защото се е осквернило назирейството му.
13 “Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
И ето законът за назирея, когато се изпълни времето на назирейството му: да се приведе при входа на шатъра за срещане;
14 Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
и той да принесе в принос за себе си Господу едно мъжко едногодишно агне без недостатък в принос за грях, един овен без недостатък за примирителен принос,
15 ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
кош с безквасни пити от чисто брашно, смесени с дървено масло, безквасни кори, намазани с масло и хлебния им принос с възлиянията им.
16 “Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
И свещеникът да ги представи пред Господа, и да принесе приноса му за грях и всеизгарянето му;
17 Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
и да принесе овена за примирителна жертва Господу, с коша на безквасните хлябове; свещеникът да принесе още хлебния принос с възлиянието му.
18 “Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
И назиреят да обръсне главата на назирейството си при входа на шатъра за срещане и да вземе космите на посветената си глава и да ги тури на огъня, който е под примирителната жертва.
19 “Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
И свещеникът да вземе сварената плешка на овена, една безквасна пита от коша и една безквасна кора и да ги тури на ръцете на назирея след като обръсне той главата на назирейството си;
20 Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
и свещеникът да ги подвижи за движим принос пред Господа; това, заедно с гърдите на движимия принос и бедрото на възвишаемия принос, е свето на свещеника; и след това назиреят може да пие вино.
21 “Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
Това е закон за назирея, който е направил обрек и за приноса му Господ поради назирейството му, освен онова, което му дава ръка; съгласно с обрека, който е направил, така да постъпва според закона за назирейството си.
22 Yehova anawuza Mose kuti,
Господ говори още на Моисея, казвайки:
23 “Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
Говори на Аарона и на синовете му, казвайки: Така благославяйте израилтяните, като им говорите:
24 “‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
Господ да те благослови и да те пази!
25 Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
Господ да осияе с лицето Си над тебе и да ти покаже милост!
26 Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
Господ да издигне лицето Си над тебе и да ти даде мир!
27 Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.
Така да възлагат Името Ми върху израилтяните; и Аз ще ги благославям.