< Numeri 5 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Gospod je spregovoril Mojzesu, rekoč:
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
»Zapovej Izraelovim otrokom, da naj iz tabora odstranijo vsakega gobavca in vsakega, ki ima izliv in vsakogar, ki je omadeževan z mrtvim.
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
Tako moškega in žensko boste poslali ven. Zunaj tabora jih boste poslali, da ne omadežujejo svojih taborov, v sredi katerih prebivam.«
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
Izraelovi otroci so tako storili in jih poslali ven, zunaj tabora. Kakor je Gospod spregovoril Mojzesu, tako so Izraelovi otroci storili.
Gospod je spregovoril Mojzesu, rekoč:
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
»Govori Izraelovim otrokom: ›Kadar bosta moški ali ženska zagrešila kakršenkoli greh, ki ga ljudje zagrešijo, da storita prestopek zoper Gospoda in da je oseba kriva,
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
potem bosta priznala svoj greh, ki sta ga storila. In svoj prestopek bo poplačal z glavnico in ji dodal peti del od tega in to bo dal tistemu, zoper katerega je kršil.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
Toda če človek nima nobenega sorodnika, da mu povrne prestopek, naj prestopek poplača Gospodu, celo duhovniku, poleg ovna sprave, s čimer bo zanj opravljena sprava.
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
Vsaka daritev vseh svetih stvari Izraelovih otrok, ki jih prinesejo duhovniku, bo njegova.
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
Vse človekove posvečene stvari bodo njegove; karkoli katerikoli človek daje duhovniku, to bo njegovo.‹«
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
Gospod je spregovoril Mojzesu, rekoč:
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
»Govorite Izraelovim otrokom in jim recite: ›Če žena kateregakoli moškega zaide proč in zoper njega zagreši prestopek
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
in moški z njo meseno leži in je to skrito pred očmi njenega soproga in je zadržano zaprto in je ona omadeževana in tam ni nobene priče zoper njo niti ona ni zasačena,
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
in pride nanj duh ljubosumnosti in je ljubosumen na svojo ženo in je ona omadeževana, ali če pride nanj duh ljubosumnosti in je ljubosumen na svojo ženo, pa ona ni omadeževana,
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
potem bo moški svojo ženo privedel k duhovniku in zanjo prinesel dar, desetino škafa ječmenove moke. Na to ne bo izlil olja niti nanj ne bo položil kadila, kajti to je daritev ljubosumnosti, daritev spominjanja, da bi v spomin privedla krivičnost.
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
Duhovnik jo bo privedel bliže in jo postavil pred Gospoda.
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
Duhovnik bo vzel sveto vodo v lončeni posodi in od prahu, ki je na tleh šotorskega svetišča, bo duhovnik vzel in to dal v vodo.
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
Duhovnik bo žensko postavil pred Gospoda in odkril glavo ženske in v njene roke dal daritev spominjanja, kar je daritev ljubosumja. Duhovnik bo imel v svoji roki grenko vodo, ki povzroča prekletstvo,
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
in duhovnik ji bo s prisego naročil ter ženski rekel: ›Če s teboj ni ležal noben moški in če nisi zašla v nečistost z drugim namesto svojega soproga, bodi čista pred to grenko vodo, ki povzroča prekletstvo.
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
Toda če si zašla k drugemu namesto svojega soproga in če si omadeževana in je poleg tvojega soproga s teboj ležal nek moški,
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
potem bo duhovnik žensko zaprisegel s prisego prekletstva in duhovnik bo ženski rekel: › Gospod naj te naredi za prekletstvo in prisego med tvojim ljudstvom, ko Gospod tvojemu stegnu stori, da zgnije in tvoj trebuh oteče,
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
in ta voda, ki povzroča prekletstvo, bo šla v tvojo notranjost, da tvojemu trebuhu povzroči, da oteče in tvojemu stegnu, da zgnije.‹ In ženska naj reče: ›Amen, amen.‹
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
Duhovnik bo ta prekletstva zapisal v knjigo in jih spral z grenko vodo.
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
Žensko bo primoral, da pije grenko vodo, ki povzroča prekletstvo in voda, ki povzroča prekletstvo, bo vstopila vanjo in postala grenka.
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
Potem bo duhovnik vzel daritev ljubosumnosti iz roke ženske in daritev bo majal pred Gospodom in jo daroval na oltarju.
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
Duhovnik bo vzel prgišče daritve, torej njen spomin in to sežgal na oltarju in potem bo ženski povzročil, da spije vodo.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
Ko jo je primoral piti vodo, potem se bo zgodilo, da če je omadeževana in je storila prestopek zoper svojega soproga, da bo voda, ki povzroča prekletstvo, vstopila vanjo in postala grenka in njen trebuh bo otekel in njeno stegno bo zgnilo, in ženska bo prekletstvo med svojim ljudstvom.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
Če pa ženska ni omadeževana, temveč je čista, potem naj bo prosta in bo spočela seme.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
To je postava ljubosumnosti, ko žena zaide k drugemu namesto svojega soproga in je omadeževana
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
ali kadar pride nadenj duh ljubosumnosti in je ljubosumen na svojo ženo in bo ženo postavil pred Gospoda in bo duhovnik nad njo izvršil vso to postavo.
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
Potem bo mož brez krivde pred krivičnostjo, ta ženska pa bo nosila svojo krivičnost.‹«