< Numeri 5 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
I rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
Rozkaż synom Izraelskim, aby wyrzucili z obozu każdego trędowatego, i każdego, który cierpi płynienie nasienia, i każdego, który się splugawił nad umarłym;
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
Tak mężczyznę jako i niewiastę wyrzucicie; precz za obóz wyrzucicie je, aby nie splugawili obozu tych, między którymi Ja mieszkam.
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
I uczynili tak synowie Izraelscy, a wygnali je precz za obóz; jako rozkazał Pan Mojżeszowi, tak uczynili synowie Izraelscy.
5 Yehova anati kwa Mose,
Nad to rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
Powiedz synom Izraelskim: Mąż albo niewiasta, gdyby popełnili jakikolwiek grzech ludzki, dopuściwszy się występku przeciwko Panu, a byłaby winna ona dusza:
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
Tedy wyznają grzech swój, którego się dopuścili, i wrócą to, w czem by winni byli cale; a przydawszy jeszcze nad to piątą część, oddadzą onemu, przeciw któremu zgrzeszyli.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
A jeźliby nie było tego, komu by szkodę trzeba nagrodzić, ona szkoda oddana będzie Panu, i zostanie kapłanowi oprócz barana oczyszczenia, przez którego ma być oczyszczony.
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
Każda też ofiara podnoszenia ze wszech rzeczy poświęconych od synów Izraelskich, którą przyniosą do kapłana, jemu się dostanie.
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
Owe rzeczy poświęcone od kogożkolwiek, jego będą; i kto by co oddał kapłanowi, jemu zostanie.
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
Zatem rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
Mów do synów Izraelskich, a powiedz im: Każdy mąż, którego by żona wystąpiła, i dopuściłaby się grzechu przeciwko niemu;
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
A złączyłby się inszy z nią złączeniem nasienia, a byłoby to skryte przed oczyma męża jej, i taiłaby się, będąc splugawioną, a świadka by nie było przeciwko niej, aniby jej zastano;
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
Jednak przypadłby nań duch zapalczywości, i miałby w podejrzeniu żonę swą, która by splugawiona była; albo żeby przypadł nań duch zapalczywości, i miałby w podejrzeniu żonę swą, która by splugawiona nie była:
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
Tedy przywiedzie on mąż żonę swoję do kapłana, i przyniesie z nią ofiarę jej, dziesiątą część efy mąki jęczmiennej nie lejąc na nią oliwy, ani kładąc na nią kadzidła; albowiem jest ofiara podejrzenia, ofiara śniedna, pamiętna, przywodząca na pamięć grzech.
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
A tak będzie ją ofiarował kapłan, i stawi ją przed oblicznością Pańską.
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
I weźmie kapłan wody świętej w naczynie gliniane, i prochu, który będzie na tle przybytku, weźmie kapłan, a wsypie do wody.
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
Potem postawi kapłan niewiastę przed Panem, i odkryje głowę niewiasty, a da w ręce jej ofiarę śniedną pamiętną; ofiara to śniedna podejrzenia; a kapłan będzie miał w ręce wodę gorzką przeklęstwa.
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
I poprzysięże ją kapłan, i rzecze do niewiasty: Jeźli nie spał kto inszy z tobą, a jeźliś się nie uniosła w grzech nieczysty przy mężu swym, bądź nienaruszona od tej wody gorzkiej przeklęstwa;
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
Ale jeźliżeś ustąpiła od męża twego, i jesteś splugawiona, a kto inny spał z tobą oprócz męża twego:
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
Tedy poprzysięże kapłan niewiastę onę przysięgą przeklęstwa, i rzecze do niej: Niechaj cię poda Pan na złorzeczenie, i na przeklinanie między ludem twoim, przepuściwszy, aby łono twoje wypadło, i żywot twój opuchł:
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
Niechże przenikną te wody przeklęte wnętrzności twoje, aby opuchł żywot twój, i wypadło łono twoje; i odpowie niewiasta: Amen. Amen.
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
Tedy napisze te przeklęstwa kapłan na księgach, a omyje je oną wodą gorzką;
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
I da się napić niewieście wody gorzkiej przeklęstwa, i przenikną ją wody przeklęstwa, i obrócą się w gorzkość.
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
Potem weźmie kapłan z rąk niewiasty onej ofiarę śniedną podejrzenia, a będzie ją podnosił przed Panem, ofiarując ją na ołtarzu;
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
Weźmie też kapłan na garść pamiętnego z ofiary śniednej, i spali to na ołtarzu, potem da wypić wodę niewieście.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
A gdy się jej da napić onej wody, stanie się, jeźliby splugawiona była, i wystąpiła grzechem przeciwko mężowi swemu, że ją przenikną wody przeklęstwa, i obrócą się w gorzkość, i opuchnie żywot jej, i wypadnie łono jej, i stanie się niewiasta ona przeklęstwem między ludem swoim.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
A jeźliby nie była splugawiona niewiasta, aleby czysta była, niewinna zostanie, i dziatki rodzić będzie.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
Tać jest ustawa podejrzenia, gdyby ustąpiła żona od męża swego, i byłaby splugawiona;
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
Albo żeby na męża przypadł duch zapalczywy, a miałby w podejrzeniu żonę swoję, i postawiłby ją przed Panem, a uczyniłby z nią kapłan wszystko według tej ustawy;
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
Tedy nie będzie mąż on winien grzechu; ale niewiasta ona poniesie nieprawość swoję.

< Numeri 5 >