< Numeri 5 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh said to Moses/me,
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
“Tell this to the Israeli people: ‘You must send away from your (camp/area where you have your tents) any man or woman who has leprosy and anyone who has a discharge [of some fluid from his body], and anyone who has become unacceptable to God because of [having touched] a corpse.
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
Send them away from there in order that they will not [touch people in the camp area] where I live among you and cause them to become unacceptable to me.’”
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
So [Moses/I told that to the Israeli people, and] the Israeli people obeyed what Yahweh commanded Moses/me.
Yahweh also told Moses/me,
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
“Tell this to the Israeli people: ‘If someone (commits a crime against/does something wrong to) another person, [I consider that] that person has done wrong to me.
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
That person must confess that he or she is guilty, and he or she must pay to the person to whom wrong was done [what others consider to be a suitable/proper payment] for what he has done, and he must pay an extra 20 percent.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
If the person against whom the wrong was done [has died and] there is no relative to whom the money can be paid, then the money belongs to me, and it must be paid to the priest. In addition, the one who did the wrong must give a male sheep to the priest [to sacrifice] in order that (that person’s sin may be forgiven/I can forgive that person for his sin).
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
All the sacred offerings that the Israelis bring to the priest belong to the priest.
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
The priest can keep those gifts.’”
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh also said this to Moses/me:
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
“Tell this to the Israeli people: ‘Suppose a man thinks that his wife has slept with another man,
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
but neither he nor anyone else knows if it is true or not, because no one saw her doing that.
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
But if the woman’s husband is jealous, and if he suspects that she has committed adultery, and he wants to know whether that is true or not,
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
he should take his wife to the priest. He must take along as an offering two quarts/liters of barley flour. The priest must not pour [olive] oil or incense on it, because this is an offering that the man has brought because he (is jealous/wants his wife to sleep only with him). It is an offering to find out if she is guilty or not. [Neither olive oil nor incense should be used because are associated with joy and this is not a time for joy.]
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
The priest must tell the woman to stand [in front of the altar] in my presence.
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
He must put some sacred water in a clay jar, and then he must put some dirt from the floor of the Sacred Tent into the water.
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
He must untie/unfasten the woman’s hair. Then he must put in her hands the grain that her jealous husband is offering to determine whether she has committed adultery or not. The priest must hold [the bowl that contains] bitter water that will cause (the woman to be cursed/bad things to happen to the woman) [if she is guilty].
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
The priest must require her to solemnly declare [that she will tell the truth]. Then he must say to her, “Has another man had sex [EUP] with you? Have you faithfully [slept only with your husband] or not? If you have not slept with another man, nothing bad will happen to you if you drink the water.
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
But if you have had sex with another man, [Yahweh will curse you].
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
Your womb will shrivel up and your stomach will swell up. You will never be able to give birth to children, and as a result, everyone will curse you and avoid you. If you have committed adultery, [when you drink] this water, that is what will happen to you.” Then the woman must answer, “[If I am guilty], I will not object if that happens.”
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
‘Then the priest must write [with ink] on a small scroll these (curses/bad things that will happen to her if she is guilty) [and then wash the ink off into the bitter water].
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
The priest must take from her the offering of barley flour [that she is holding], and lift it up to dedicate it to me. Then he must put it on the altar
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
and burn part of it as a sacrifice. Then the woman must drink the bitter water.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
If the woman has committed adultery, the water will cause her to suffer greatly. Her stomach will swell up and her womb will shrink, [and she will be unable to give birth to children]. And then her (relatives/fellow Israelis) will curse her.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
But if she (is innocent/has not committed adultery), her body will not be harmed, and she will still be able to give birth to children.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
‘That is the ritual that must be performed when a woman who is married has been unfaithful to her husband,
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
or when a man is jealous and suspects that his wife [has had sex with another man]. The priest must tell that woman to stand [at the altar] in my presence and obey these instructions.
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
Even if the woman has not done what the husband suspected, he will not be punished [MTY] for doing something wrong [by bringing his wife to the priest]. But if his wife is guilty, she will suffer as a result.’”