< Numeri 5 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
Command [the] people of Israel so they may send away from the camp any [one who] has a skin disease and any [one who] has a discharge and any [person] unclean to a corpse.
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
From male unto female you will send away to from [the] outside of the camp you will send away them and not they will make unclean camps their which I [am] dwelling in midst of them.
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
And they did so [the] people of Israel and they sent away them to from [the] outside of the camp just as he had spoken Yahweh to Moses so they did [the] people of Israel.
And he spoke Yahweh to Moses saying.
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
Speak to [the] people of Israel a man or a woman if they will do any of all [the] sins of humankind by acting unfaithfully unfaithfulness against Yahweh and it will be guilty the person that.
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
And they will confess sin their which they have done and he will repay compensation its in sum its and fifth its let him add to it and he will give [it] to [the one] whom he was guilty to him.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
And if not [belongs] to the person a kinsman-redeemer to repay the compensation to him the compensation which is repaid [belongs] to Yahweh for the priest besides [the] ram of atonement which he will make atonement by it on him.
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
And every contribution to all [the] holy things of [the] people of Israel which they will bring near to the priest to him it will belong.
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
And everyone holy things his to him they will belong everyone [that] which he will give to the priest to him it will belong.
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
Speak to [the] people of Israel and you will say to them a man a man if she will turn aside wife his and she will act unfaithfully against him unfaithfulness.
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
And he will lie with a man with her a laying of seed and it will be hidden from [the] eyes of husband her and she will be undiscovered and she she has made herself unclean and [was] a witness there not against her and she not she was caught.
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
And it will pass over him a spirit of jealousy and he will be jealous of wife his and she she has made herself unclean or it has passed over him a spirit of jealousy and he will be jealous of wife his and she not she has made herself unclean.
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
And he will bring the man wife his to the priest and he will bring offering her on her tenth of ephah flour of barley not he will pour out on it oil and not he will put on it frankincense for [is] a grain offering of jealousi it a grain offering of remembrance [which] brings to remembrance iniquity.
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
And he will bring near her the priest and he will make stand her before Yahweh.
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
And he will take the priest water holy in a vessel of earthenware and some of the dust which it will be on [the] floor of the tabernacle he will take the priest and he will put [it] into the water.
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
And he will make stand the priest the woman before Yahweh and he will let loose [the] head of the woman and he will put on hands her [the] grain offering of remembrance [is] a grain offering of jealousi it and in [the] hand of the priest they will be [the] waters of bitter [things] which bring a curse.
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
And he will make swear her the priest and he will say to the woman if not he has lain with a man with you and if not you have turned aside uncleanness under husband your be free from [the] waters of bitter [things] which bring a curse these.
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
And you if you have turned aside under husband your and if you have made yourself unclean and he has given a man in you copulation his from except husband your.
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
And he will make swear the priest the woman with [the] oath of the curse and he will say the priest to the woman may he make Yahweh you into a curse and into a oath in among people your when makes Yahweh thigh your falling and belly your swollen.
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
And they will go the waters which bring a curse these in inward parts your to make swell a belly and to make fall a thigh and she will say the woman amen - amen.
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
And he will write the curses these the priest on the scroll and he will wipe [them] off into [the] waters of bitter [things].
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
And he will make drink the woman [the] waters of bitter [things] which bring a curse and they will go in her the waters which bring a curse to bitter [things].
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
And he will take the priest from [the] hand of the woman [the] grain offering of jealousi and he will wave the grain offering before Yahweh and he will bring near it to the altar.
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
And he will take a handful the priest of the grain offering memorial offering its and he will make [it] smoke the altar towards and after he will make drink the woman the waters.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
And he will make drink her the waters and she will be if she has made herself unclean and she has acted unfaithfully unfaithfulness against husband her and they will go in her the waters which bring a curse to bitter [things] and it will swell belly her and it will fall thigh her and she will become the woman a curse in [the] midst of people her.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
And if not she has made herself unclean the woman and [is] pure she and she will be free and she will be impregnated seed.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
This [is] [the] law of jealousi that she will turn aside a wife under husband her and she will make herself unclean.
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
Or a man whom it will pass over him a spirit of jealousy and he will be jealous of wife his and he will make stand the woman before Yahweh and he will do to her the priest all the law this.
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
And he will be free the man from iniquity and the woman that she will bear iniquity her.