< Numeri 5 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
Command the children of Israel, that they send out of the camp every leper, and every one that hath an issue, and whosoever is defiled by the dead:
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
Both male and female shall ye send out, to without the camp shall ye send them; that they defile not their camps, in the midst whereof I dwell.
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
And the children of Israel did so, and they sent them out to without the camp: as the Lord had spoken unto Moses, so did the children of Israel.
And the Lord spoke unto Moses, saying,
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
Speak unto the children of Israel, If any man or woman commit any sin against a fellow-man, thereby doing a trespass against the Lord, and this person thus become guilty:
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
Then shall they confess their sin which they have committed; and he shall make restitution for his trespass with the principal thereof, and its fifth part shall he add thereto, and give it unto him against whom he hath trespassed.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
But if the man have no kinsman to whom restitution could be made for the trespass, then shall the trespass which is restored unto the Lord, belong to the priest; besides the ram of the atonement, whereby an atonement shall be made for him.
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
And every offering of all the holy things of the children of Israel, which they bring unto the priest, shall be his.
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
And every man's hallowed things shall be his: whatsoever any man giveth to the priest, shall belong to him.
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
Speak unto the children of Israel, and say unto them, If the wife of any man go aside, and commit a trespass against him,
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
And a man lie with her carnally, and it be hidden from the eyes of her husband, because she hath been secretly defiled; and there be no witness against her, and she have not been detected and in the fact;
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
And the spirit of jealousy come over him, and he be jealous of his wife, and she have been defiled; or the spirit of jealousy come over him, and he be jealous of his wife, and she have not been defiled:
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
Then shall the man bring his wife unto the priest, and he shall bring her offering for her, the tenth part of an ephah of barley-meal; he shall not pour any oil upon it, nor put any frankincense thereupon; for it is a meat-offering of jealousy, a meat-offering of memorial, bringing iniquity to remembrance.
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
And the priest shall bring her near, and place her before the Lord;
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
And the priest shall take holy water in an earthen vessel; and of the dust that is on the floor of the tabernacle the priest shall take, and put it into the water;
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
And the priest shall place the woman before the Lord, and uncover the woman's head, and put upon her hands the meat-offering of memorial, it is the meat-offering of jealousy; and in the hand of the priest shall be the bitter waters that bring the curse.
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
And the priest shall charge her by an oath, and he shall say unto the woman, If no man have lain with thee, and if thou hast not gone aside to uncleanness behind thy husband: then be thou free from these bitter waters that bring the curse.
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
But if thou hast gone aside behind thy husband, and if thou hast been defiled, and some man have lain with thee besides thy husband: —
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
And the priest shall charge the woman with an oath of imprecation, and the priest shall say unto the woman, The Lord then make thee a curse and an oath among thy people, when the Lord doth cause thy thigh to fall away, and thy belly to swell;
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
And these waters that bring the curse shall go into thy bowels, to cause the belly to swell, and the thigh to fall away; and the woman shall say, Amen, amen.
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
And the priest shall write these curses on a roll, and he shall blot them out with the bitter waters.
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
And he shall cause the woman to drink the bitter waters that bring the curse: and the waters that bring the curse shall enter into her for bitterness.
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
And the priest shall take out of the woman's hand the meat-offering of jealousy, and he shall wave the meat-offering before the Lord, and bring it near to the altar:
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
And the priest shall take a handful from the meat-offering, as its memorial, and burn it upon the altar, and after that shall he cause the woman to drink the water.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
And when he hath made her drink the water, then shall it come to pass, if she have been defiled, and have committed a trespass against her husband, that the waters that bring the curse shall enter into her, for bitterness, and her belly shall swell, and her thigh shall fall away; and the woman shall become a curse among her people.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
And if the woman have not been defiled, but be clean: then shall she remain unharmed, and she shall conceive seed.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
This is the law of jealousies, when a woman goeth aside behind her husband, and hath been defiled;
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
Or when the spirit of jealousy cometh over him, and he be jealous of his wife; and he shall place the woman before the Lord, and the priest shall do unto her altogether according to this law.
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
And the man shall be guiltless from iniquity; but this woman shall bear her iniquity.