< Numeri 5 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
I mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
Přikaž synům Izraelským, ať vyženou z stanů každého malomocného a každého trpícího tok semene, i každého nad mrtvým poškvrněného.
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
I muže i ženu vyženete, ven za stany vyženete je, aby nepoškvrňovali vojska těch, mezi nimiž já přebývám.
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
I učinili tak synové Izraelští, a vyhnali je ven za stany. Jakož byl mluvil Hospodin k Mojžíšovi, tak učinili synové Izraelští.
5 Yehova anati kwa Mose,
Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi, řka:
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
Mluv k synům Izraelským: Muž aneb žena, když učiní nějaký hřích lidský, dopouštěje se výstupku proti Hospodinu, a byla by vinna duše ta:
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
Tedy vyzná hřích svůj, kterýž učinil, navrátí pak to, čímž vinen byl, v cele, a pátý díl přidá nad to, a dá tomu, proti komuž zavinil.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
A neměl-li by muž ten přítele, jemuž by nahradil tu škodu, pokuta dána buď Hospodinu a knězi, mimo skopce očištění, jímž očištěn býti má.
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
Též všeliká obět všech věcí posvěcených od synů Izraelských, kterouž přinesou knězi, jemu se dostane.
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
Tak i věci posvěcené od kohokoli jemu se dostanou; a dal-li kdo co knězi, také jeho bude.
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
Mluvil ještě Hospodin k Mojžíšovi, řka:
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
Mluv k synům Izraelským a rci jim: Kdyby od některého muže uchýlila se žena, a dopustila by se výstupku proti němu,
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
Tak že by obýval někdo jiný s ní, a bylo by to skryto před očima muže jejího, a tajila by se, jsuci poškvrněna, a svědka by nebylo proti ní, a ona nebyla by postižena;
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
Pohnul-li by se duch muže horlivostí velikou, tak že by horlil proti ženě své, kteráž by poškvrněna byla; aneb pohnul-li by se duch muže velikou horlivostí, tak že by horlil proti ženě své, kteráž by poškvrněna nebyla:
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
Tedy přivede muž ženu svou k knězi, a přinese obět její při ní, desátý díl efi mouky ječné. Nenalejeť na ni oleje, aniž dá na ni kadidla; nebo obět veliké horlivosti jest, obět suchá pamětná, uvozující v pamět nepravost.
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
I bude ji kněz obětovati, a postaví ji před Hospodinem.
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
A nabere vody svaté do nádoby hliněné, a vezma prachu, kterýž jest na zemi v příbytku, dá jej do té vody.
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
Potom postaví kněz ženu tu před Hospodinem, a odkryje hlavu její, a dá jí do rukou obět suchou pamětnou, kteráž jest obět veliké horlivosti; v ruce pak kněze bude voda hořká zlořečená.
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
I zaklínati bude ji kněz a řekne k ní: Jestliže neobcoval s tebou žádný, a jestliže jsi neuchýlila se k nečistotě od muže svého, budiž čistá od vody této hořké zlořečené.
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
Paklis se uchýlila od muže svého a nečistá jsi, a obcoval-li někdo jiný s tebou kromě manžela tvého,
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
(Zaklínati pak bude kněz tu ženu, čině klatbu zlořečenství, a řekne jí: ) Dejž tebe Hospodin v zlořečení a v prokletí u prostřed lidu tvého, dopustě, aby lůno tvé hnilo a břicho tvé oteklo.
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
Vejdiž voda zlořečená tato do života tvého, aby oteklo břicho tvé, a lůno tvé shnilo. I odpoví žena ta: Amen, amen.
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
Napíše pak všecko zlořečenství toto do knihy, a smyje je tou vodou hořkou.
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
I dá ženě, aby pila vodu hořkou a zlořečenou; a vejdeť do ní voda zlořečená, a obrátí se v hořkosti.
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
Potom vezme kněz z ruky ženy obět veliké horlivosti, a obraceti ji bude sem i tam před Hospodinem, a bude ji obětovati na oltáři.
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
A vezma plnou hrst pamětného jejíhoz oběti suché, páliti to bude na oltáři; a potom dá vypíti ženě tu vodu.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
A když jí dá píti tu vodu, stane se, jestliže nečistá byla, a dopustila se výstupku proti muži svému, že vejde do ní voda zlořečená, a obrátí se v hořkost, i odme se břicho její, a vyhnije lůno její; i bude žena ta v zlořečení u prostřed lidu svého.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
Pakli není poškvrněna žena ta, ale čistá jest, tedy bez viny bude, a roditi bude děti.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
Ten jest zákon veliké horlivosti, když by se uchýlila žena od muže svého, a byla by poškvrněna,
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
Aneb když by se pohnul duch veliké horlivosti v manželu, tak že by horlil velmi proti ženě své, aby postavil ji před Hospodinem, a aby vykonal při ní kněz všecko vedlé zákona tohoto.
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
I bude ten muž očištěn od hříchu, žena pak ponese nepravost svou.

< Numeri 5 >