< Numeri 4 >
1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
Yavé habló a Moisés y a Aarón:
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Toma la cuenta de los hijos de Coat de entre los hijos de Leví, según sus familias y casas paternas,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
de edad de 30 años para arriba hasta 50 años, todos los que entran a hacer servicio en el Tabernáculo de Reunión.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
El servicio de los hijos de Coat en el Tabernáculo de Reunión será de las cosas más sagradas.
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
Cuando el campamento se traslade, Aarón y sus hijos entrarán y descolgarán el velo de separación, con el cual cubrirán el Arca del Testimonio.
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
Sobre ella pondrán la cubierta de piel de tejón. Extenderán encima un paño completamente azul y le pondrán sus varas.
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
También extenderán un paño azul sobre la mesa de la Presencia. Sobre él pondrán los tazones, las cucharas y las copas de libación. El pan quedará sobre ella perpetuamente.
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
Luego extenderán sobre estas cosas un paño carmesí. Lo taparán con la cubierta de piel de tejón, y le pondrán sus varas.
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
Después tomarán un paño azul y cubrirán el candelabro del alumbrado y sus lámparas, despabiladeras y platillos y todos los recipientes del aceite con los cuales se le hace servicio.
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
Lo envolverán con todos sus utensilios en una cubierta de piel de tejón, y lo pondrán sobre dos varas gruesas arregladas con tablas.
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
Extenderán también un paño azul sobre el altar de oro. Lo cubrirán con una cubierta de piel de tejón, y le pondrán sus varas.
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
Tomarán todos los utensilios del servicio con los cuales ministran en el Santuario y los envolverán en un paño azul. Los cubrirán con una cubierta de piel de tejón, y los pondrán sobre un par de varas gruesas arregladas con tablas para cargarlos.
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
Después quitarán la ceniza del altar y extenderán sobre él un paño púrpura.
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
Pondrán todos sus utensilios con los cuales ministran sobre él: braseros, tenedores, paletas, tazones y todos los instrumentos del altar. Extenderán sobre él una cubierta de piel de tejón y le pondrán sus varas.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
Cuando Aarón y sus hijos terminen de cubrir los objetos sagrados con todos los utensilios del Santuario para mover el campamento, los hijos de Coat llegarán a transportarlos, pero no tocarán el Santuario, pues morirían. Estas son las cosas del Tabernáculo de Reunión que los hijos de Coat transportarán.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
Eleazar, hijo del sacerdote Aarón, estará encargado del aceite del alumbrado, incienso aromático, ofrenda vegetal permanente y del aceite de la unción. Estará encargado de todo el Tabernáculo y todo lo que hay en él, del Santuario y sus utensilios.
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
Yavé habló a Moisés y a Aarón:
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
No permitan que el grupo de las familias de los coatitas sea exterminado de entre los levitas.
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
Esto harán con ellos para que vivan y no mueran cuando se acerquen a los objetos santísimos. Aarón y sus hijos entrarán y asignarán a cada uno su tarea y su carga,
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
pero no entrarán para mirar los objetos sagrados, no sea que mueran.
21 Yehova anawuza Mose kuti,
Yavé habló a Moisés:
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
Haz también la cuenta de los hijos de Gersón según sus casas paternas y sus familias.
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
Los contarás de 30 años para arriba hasta 50, todos los que entran a prestar servicio en el Tabernáculo de Reunión.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
Esta será la obra de las familias de Gersón para servir y para transportar:
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
Transportarán las cortinas del Tabernáculo, el Tabernáculo de Reunión, su cubierta, la cubierta de pieles de tejón que está encima de él, la cortina de la entrada al Tabernáculo de Reunión;
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
también las cortinas del patio, la cortina de la entrada al patio que está alrededor del Tabernáculo y del altar, sus cuerdas, todos los utensilios y todo el servicio perteneciente a ellos.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
Toda la obra de los hijos de Gersón, en todos sus cargos y en todo su servicio, será según lo que digan Aarón y sus hijos. Les encomendarán la responsabilidad de todo lo que transportan.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
Tal es el servicio de las familias gersonitas en el Tabernáculo de Reunión. Sus deberes estarán bajo la dirección de Itamar, hijo del sacerdote Aarón.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Contarás también a los hijos de Merari, según sus familias y sus casas paternas.
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
Contarás todos los que entran para servir en el Tabernáculo de Reunión desde los 30 años para arriba hasta los 50 años de edad.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
Su deber en cuanto a la carga en todo su servicio en el Tabernáculo de Reunión es: los tablones del Tabernáculo, sus travesaños, columnas y basas,
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
las columnas del patio que lo rodea, sus basas, estacas y cuerdas, todos sus utensilios para todo su servicio. Anotarán por nombre los utensilios que ellos tienen que transportar.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
Tal es el servicio de las familias meraritas en toda su obra en el Tabernáculo de Reunión bajo la dirección de Itamar, hijo del sacerdote Aarón.
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Así, pues, Moisés, Aarón y los jefes de la congregación contaron a los hijos de Coat según sus familias y sus casas paternas,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
todos los que entran a servir en el Tabernáculo de Reunión desde los 30 años para arriba hasta los 50 años de edad.
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
Los contados según sus familias fueron 2.750.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Estos fueron los contados de las familias de Coat, todos los que sirven en el Tabernáculo de Reunión, a quienes Moisés y Aarón contaron, conforme al mandato de Yavé por medio de Moisés.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Los contados de los hijos de Gersón, según sus familias y casas paternas,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
desde la edad de 30 años para arriba hasta los 50, todos los que entran a servir en el Tabernáculo de Reunión.
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
Los contados por sus familias y casas paternas fueron 2.630.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Estos fueron los contados de las familias de los hijos de Gersón, los que sirven en el Tabernáculo de Reunión, a quienes Moisés y Aarón contaron conforme al mandato de Yavé.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Los contados de las familias de los hijos de Merari según sus familias y casas paternas,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
desde la edad de 30 años para arriba hasta los 50, los que entran en el servicio para ministrar en el Tabernáculo de Reunión.
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
Los contados según sus familias fueron 3.200.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
Tales fueron los contados de las familias de los hijos de Merari, a quienes Moisés y Aarón contaron conforme al mandato de Yavé por medio de Moisés.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Todos los levitas y los jefes de Israel contados por Moisés y Aarón, según sus familias y casas paternas,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
de 30 años para arriba hasta los 50 años de edad, todos los que entran en el Tabernáculo de Reunión para servir
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
Fueron contados como Yavé mandó por medio de Moisés. Cada uno fue contado según su oficio y lo que debía cargar como Yavé ordenó a Moisés.