< Numeri 4 >

1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
Yahvé habló a Moisés y a Aarón, diciendo:
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
“Haz un censo de los hijos de Coat de entre los hijos de Leví, por sus familias, por las casas de sus padres,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
desde los treinta años en adelante hasta los cincuenta años, todos los que entren en el servicio para hacer el trabajo en la Tienda del Encuentro.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
“Este es el servicio de los hijos de Coat en la Tienda del Encuentro, en lo que respecta a las cosas más sagradas.
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
Cuando el campamento avance, Aarón entrará con sus hijos; y ellos quitarán el velo de la cortina, cubrirán con él el Arca del Testimonio,
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
le pondrán una cubierta de piel de tejones, extenderán sobre ella un paño azul y colocarán sus varas.
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
“Sobre la mesa del pan de la función extenderán un paño azul, y pondrán sobre él los platos, las cucharas, los tazones y las copas con las que se sirve; y sobre él estará el pan continuo.
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
Extenderán sobre ella un paño de color escarlata y la cubrirán con un revestimiento de piel de tejón, y pondrán sus varas.
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
“Tomarán un paño azul y cubrirán el candelabro de la lámpara, sus lámparas, sus apagadores, sus tabaqueras y todos sus recipientes de aceite, con los que la atienden.
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
La pondrán, junto con todos sus recipientes, dentro de una cubierta de piel de tejón, y la pondrán sobre el armazón.
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
“Sobre el altar de oro extenderán un paño azul y lo cubrirán con una cubierta de piel de tejón, y pondrán sus varas.
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
“Tomarán todos los utensilios del ministerio con los que ministran en el santuario, los pondrán en un paño azul, los cubrirán con una funda de piel de tejón y los pondrán sobre el bastidor.
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
“Quitarán la ceniza del altar y extenderán sobre él un paño de color púrpura.
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
Pondrán sobre él todos los utensilios con los que ministran a su alrededor, las sartenes para el fuego, los ganchos para la carne, las palas y las palanganas, todos los utensilios del altar; y extenderán sobre él una cubierta de piel de tejón, y pondrán sus varas.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
“Cuando Aarón y sus hijos hayan terminado de cubrir el santuario y todos los muebles del santuario, mientras el campamento avanza; después de eso, los hijos de Coat vendrán a llevarlo; pero no tocarán el santuario, para no morir. Los hijos de Coat llevarán estas cosas que pertenecen a la Tienda de reunión.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
“La tarea del sacerdote Eleazar, hijo de Aarón, será el aceite para la luz, el incienso aromático, la ofrenda continua y el aceite para la unción, los requisitos de todo el tabernáculo y de todo lo que hay en él, el santuario y su mobiliario.”
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
Yahvé habló a Moisés y a Aarón, diciendo:
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
“No eliminen a la tribu de las familias de los coatitas de entre los levitas;
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
sino que hagan esto con ellos, para que vivan y no mueran cuando se acerquen a las cosas más santas: Aarón y sus hijos entrarán y asignarán a cada uno su servicio y su carga;
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
pero no entrarán a ver el santuario ni siquiera por un momento, para que no mueran.”
21 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahvé habló a Moisés diciendo:
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
“Haz un censo también de los hijos de Gersón, por las casas de sus padres, por sus familias;
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
los contarás desde los treinta años en adelante hasta los cincuenta años: todos los que entran a servir, a hacer el trabajo en la Tienda del Encuentro.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
“Este es el servicio de las familias de los gersonitas, para servir y llevar cargas:
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
llevarán las cortinas del tabernáculo y de la Tienda de reunión, su cubierta, la cubierta de piel de sello que está sobre ella, la cortina de la puerta de la Tienda de reunión,
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
las cortinas del atrio, la cortina de la puerta del atrio que está junto al tabernáculo y alrededor del altar, sus cuerdas y todos los instrumentos de su servicio, y todo lo que se haga con ellos. Ellos servirán allí.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
A las órdenes de Aarón y de sus hijos estará todo el servicio de los hijos de los gersonitas, en toda su carga y en todo su servicio; y les asignarás su deber en todas sus responsabilidades.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
Este es el servicio de las familias de los hijos de los gersonitas en la Tienda de Reunión. Su deber estará bajo la mano de Itamar, hijo del sacerdote Aarón.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
“En cuanto a los hijos de Merari, los contarás por sus familias, por las casas de sus padres;
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
los contarás desde los treinta años y hasta los cincuenta, todos los que entren en el servicio, para hacer la obra de la Tienda de reunión.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
Esta es la tarea de su carga, según todo su servicio en la Tienda de reunión: las tablas del tabernáculo, sus barras, sus pilares, sus bases,
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
los pilares del atrio que lo rodea, sus bases, sus clavijas, sus cuerdas, con todos sus instrumentos y con todo su servicio. Les asignarás los instrumentos del servicio de su carga por su nombre.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
Este es el servicio de las familias de los hijos de Merari, según todo su servicio en la Tienda de reunión, bajo la mano de Itamar hijo del sacerdote Aarón.”
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Moisés y Aarón y los príncipes de la congregación contaron a los hijos de los coatitas por sus familias y por las casas de sus padres,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
desde los treinta años y hasta los cincuenta, a todos los que entraban en el servicio para trabajar en la Tienda del Encuentro.
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
Los contados de ellos por sus familias fueron dos mil setecientos cincuenta.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Estos son los que fueron contados de las familias de los coatitas, todos los que servían en la Tienda del Encuentro, los cuales fueron contados por Moisés y Aarón según el mandato de Yahvé por medio de Moisés.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Los que fueron contados de los hijos de Gersón, por sus familias y por las casas de sus padres,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
desde los treinta años de edad hasta los cincuenta, todos los que entraron en el servicio para trabajar en la Tienda del Encuentro,
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
los que fueron contados de ellos, por sus familias y por las casas de sus padres, fueron dos mil seiscientos treinta.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Estos son los que fueron contados de las familias de los hijos de Gersón, todos los que servían en la Tienda del Encuentro, los cuales fueron contados por Moisés y Aarón según el mandamiento de Yahvé.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Los que fueron contados de las familias de los hijos de Merari, por sus familias, por las casas de sus padres,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
de treinta años en adelante hasta los cincuenta años, todos los que entraron en el servicio para trabajar en la Tienda de Reunión,
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
hasta los que fueron contados de ellos por sus familias, fueron tres mil doscientos.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
Estos son los que fueron contados de las familias de los hijos de Merari, que Moisés y Aarón contaron según el mandato de Yahvé por medio de Moisés.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Todos los contados de los levitas que Moisés y Aarón y los príncipes de Israel contaron, por sus familias y por las casas de sus padres,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
de treinta años en adelante hasta los cincuenta, todos los que entraron a hacer el trabajo de servicio y el trabajo de llevar cargas en la Tienda del Encuentro,
48 analipo 8,580.
los contados de ellos, fueron ocho mil quinientos ochenta.
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
Según el mandato de Yahvé fueron contados por Moisés, cada uno según su servicio y según su cargo. Así fueron contados por él, como Yahvé le ordenó a Moisés.

< Numeri 4 >