< Numeri 4 >

1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
و خداوند موسی و هارون را خطاب کرده، گفت:۱
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
«حساب بنی قهات را از میان بنی لاوی برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان بگیر.۲
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
از سی ساله و بالاتر تا پنجاه ساله، هر‌که داخل خدمت شود تا در خیمه اجتماع کار کند.۳
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
«و خدمت بنی قهات در خیمه اجتماع، کارقدس‌الاقداس باشد.۴
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
و هنگامی که اردو کوچ می‌کند هارون وپسرانش داخل شده، پوشش حجاب را پایین بیاورند، و تابوت شهادت را به آن بپوشانند.۵
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
و برآن پوشش پوست خز آبی بگذارند و جامه‌ای که تمام آن لاجوردی باشد بالای آن پهن نموده، چوب دستهایش را بگذرانند.۶
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
«و بر میز نان تقدمه، جامه لاجوردی بگسترانند و بر آن، بشقابها و قاشقها و کاسه‌ها وپیاله های ریختنی را بگذرانند و نان دائمی بر آن باشد.۷
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
و جامه قرمز بر آنها گسترانیده، آن را به پوشش پوست خز بپوشانند و چوبدستهایش رابگذرانند.۸
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
«و جامه لاجوردی گرفته، شمعدان روشنایی و چراغهایش و گلگیرهایش وسینی هایش و تمامی ظروف روغنش را که به آنهاخدمتش می‌کنند بپوشانند،۹
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
و آن را و همه اسبابش را در پوشش پوست خز گذارده، برچوب دستی بگذارند.۱۰
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
«و بر مذبح زرین، جامه لاجوردی گسترانیده، آن را به پوشش پوست خز بپوشانند، و چوب دستهایش را بگذرانند.۱۱
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
«و تمامی اسباب خدمت را که به آنها درقدس خدمت می‌کنند گرفته، آنها را در جامه لاجوردی بگذرانند، و آنها را به پوشش پوست خز پوشانیده، بر چوب دست بنهند.۱۲
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
«و مذبح را از خاکستر خالی کرده، جامه ارغوانی بر آن بگسترانند.۱۳
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
و جمیع اسبابش راکه به آنها خدمت آن را می‌کنند یعنی مجمرها وچنگالها و خاک اندازها و کاسه‌ها، همه اسباب مذبح را بر روی آن بنهند، و بر آن پوشش، پوست خز گسترانیده، چوب دستهایش را بگذرانند.۱۴
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
«و چون هارون و پسرانش در هنگام کوچ کردن اردو، از پوشانیدن قدس و تمامی اسباب قدس فارغ شوند، بعد از آن پسران قهات برای برداشتن آن بیایند، اما قدس را لمس ننمایند مبادابمیرند، این چیزها از خیمه اجتماع حمل بنی قهات می‌باشد.۱۵
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
«و ودیعت العازار بن هارون کاهن، روغن بجهت روشنایی و بخور خوشبو و هدیه آردی دائمی و روغن مسح و نظارت تمامی مسکن می‌باشد، با هرآنچه در آن است، خواه از قدس وخواه از اسبابش.»۱۶
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
و خداوند موسی و هارون را خطاب کرده، گفت:۱۷
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
«سبط قبایل قهاتیان را از میان لاویان منقطع مسازید.۱۸
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
بلکه با ایشان چنین رفتارنمایید تا چون به قدس‌الاقداس نزدیک آیند، زنده بمانند و نمیرند. هارون و پسرانش داخل آن بشوند، و هریک از ایشان را به خدمت و حمل خود بگمارند.۱۹
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
و اما ایشان بجهت دیدن قدس لحظه‌ای هم داخل نشوند، مبادا بمیرند.»۲۰
21 Yehova anawuza Mose kuti,
و خداوند موسی را خطاب کرده، گفت:۲۱
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
«حساب بنی جرشون را نیز برحسب خاندان آباو قبایل ایشان بگیر.۲۲
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
از سی ساله و بالاتر تاپنجاه ساله ایشان را بشمار، هر‌که داخل شود تادر خیمه اجتماع به شغل بپردازد و خدمت بنماید.۲۳
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
«این است خدمت قبایل بنی جرشون درخدمت گذاری و حمل،۲۴
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
که تجیرهای مسکن وخیمه اجتماع را با پوشش آن و پوشش پوست خز که بر بالای آن است، و پرده دروازه خیمه اجتماع را بردارند.۲۵
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
و تجیرهای صحن و پرده مدخل دروازه صحن، که پیش مسکن و به اطراف مذبح است، و طنابهای آنها و همه اسباب خدمت آنها و هرچه به آنها باید کرده شود، ایشان بکنند.۲۶
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
و تمامی خدمت بنی جرشون در هر حمل وخدمت ایشان، به فرمان هارون و پسران او بشود، و جمیع حملهای ایشان را بر ایشان ودیعت گذارید.۲۷
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
این است خدمت قبایل بنی جرشون در خیمه اجتماع. و نظارت ایشان به‌دست ایتامار بن هارون کاهن باشد.۲۸
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
«و بنی مراری را برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان بشمار.۲۹
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
از سی ساله و بالاتر تاپنجاه ساله هرکه به خدمت داخل شود، تا کارخیمه اجتماع را بنماید. ایشان را بشمار.۳۰
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
این است ودیعت حمل ایشان، در تمامی خدمت ایشان در خیمه اجتماع، تختهای مسکن وپشت بندهایش و ستونهایش و پایه هایش۳۱
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
وستونهای اطراف صحن و پایه های آنها و میخهای آنها و طنابهای آنها با همه اسباب آنها، و تمامی خدمت آنها، پس اسباب ودیعت حمل ایشان رابه نامها حساب کنید.۳۲
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
این است خدمت قبایل بنی مراری در تمامی خدمت ایشان در خیمه اجتماع، زیردست ایتامار بن هارون کاهن.»۳۳
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
و موسی و هارون و سروران جماعت، بنی قهات را برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان شمردند.۳۴
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
از سی ساله و بالاتر تا پنجاه ساله هرکه به خدمت داخل می‌شد تا در خیمه اجتماع مشغول شود.۳۵
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
و شمرده شدگان ایشان برحسب قبایل ایشان، دو هزار و هفتصد و پنجاه نفر بودند.۳۶
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
اینانند شمرده شدگان قبایل قهاتیان، هرکه درخیمه اجتماع کار می‌کرد که موسی و هارون ایشان را برحسب آنچه خداوند به واسطه موسی فرموده بود، شمردند.۳۷
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
و شمرده شدگان بنی جرشون برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان،۳۸
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
از سی ساله وبالاتر تا پنجاه ساله، هرکه به خدمت داخل می‌شدتا در خیمه اجتماع کار کند.۳۹
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
و شمرده شدگان ایشان برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان، دوهزار و ششصد و سی نفر بودند.۴۰
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
اینانند شمرده شدگان قبایل بنی جرشون، هرکه در خیمه اجتماع کار می‌کرد که موسی و هارون ایشان رابرحسب فرمان خداوند شمردند.۴۱
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
و شمرده شدگان قبایل بنی مراری برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان،۴۲
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
از سی ساله وبالاتر تا پنجاه ساله، هرکه به خدمت داخل می‌شدتا در خیمه اجتماع کار کند.۴۳
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
و شمرده شدگان ایشان برحسب قبایل ایشان سه هزار و دویست نفر بودند.۴۴
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
اینانند شمرده شدگان قبایل بنی مراری که موسی و هارون ایشان را برحسب آنچه خداوند به واسطه موسی فرموده بود، شمردند.۴۵
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
جمیع شمرده شدگان لاویان که موسی وهارون و سروران اسرائیل ایشان را برحسب قبایل و خاندان آبای ایشان شمردند،۴۶
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
از سی ساله و بالاتر تا پنجاه ساله هرکه داخل می‌شد تاکار خدمت و کار حملها را در خیمه اجتماع بکند.۴۷
48 analipo 8,580.
شمرده شدگان ایشان هشت هزار وپانصد و هشتاد نفر بودند،۴۸
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
برحسب فرمان خداوند به توسط موسی، هرکس موافق خدمتش و حملش شمرده شد. و چنانکه خداوند موسی را امر فرموده بود، اوایشان را شمرد.۴۹

< Numeri 4 >