< Numeri 4 >

1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
L’Éternel parla à Moïse et à Aaron en ces termes:
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
"Qu’on fasse le relevé des enfants de Kehath entre les autres descendants de Lévi, selon leurs familles, par maisons paternelles,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
depuis l’âge de trente ans et plus, jusqu’à l’âge de cinquante ans: quiconque est admissible au service, à l’exécution d’une tâche dans la tente d’assignation.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
Voici la tâche des enfants de Kehath, dans la tente d’assignation: elle concerne les choses très saintes.
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
Aaron entrera avec ses fils, lorsque le camp devra partir; ils détacheront le voile protecteur, et en couvriront l’arche du statut;
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
ils mettront encore dessus une housse de peau de tahach, étendront par-dessus une étoffe entièrement d’azur, puis ajusteront ses barres.
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
Sur la table de proposition ils étendront une étoffe d’azur, sur laquelle ils placeront les sébiles, les cuillers, les demi-tubes et les montants qui garnissent la table; quant au pain perpétuel, il restera dessus.
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
Ils étendront sur ces objets une étoffe d’écarlate, qu’ils couvriront d’une housse de peau de tahach; puis ils ajusteront ses barres.
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
ils prendront une étoffe d’azur, y envelopperont le candélabre servant à l’éclairage, avec ses lampes, ses mouchettes, ses godets et tous les vaisseaux à huile employés pour son service.
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
Et ils le mettront, avec tous ses ustensiles, dans une enveloppe de peau de tahach, et le poseront sur une civière.
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
Sur l’autel d’or ils étendront une étoffe d’azur, la couvriront d’une housse de peau de tahach, et ajusteront les barres;
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
ils prendront tous les ustensiles employés pour le service du sanctuaire, les mettront dans une étoffe d’azur, les couvriront d’une housse de peau de tahach, et les poseront sur une civière.
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
Ils enlèveront les cendres de l’autel, sur lequel ils étendront une étoffe de pourpre.
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
Ils mettront là-dessus tous les ustensiles destinés à son service: brasiers, fourches, pelles, bassins, tous les ustensiles de cet autel; ils déploieront par-dessus une housse de peau de tahach, et ajusteront les barres.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
Aaron et ses fils achèveront ainsi d’envelopper les choses saintes et tous les ustensiles sacrés, lors du départ du camp; alors seulement viendront les enfants de Kehath pour les porter, car ils ne doivent pas toucher aux choses saintes, sous peine de mort. C’Est là la charge des enfants de Kehath dans la tente d’assignation.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
Les fonctions d’Eléazar, fils d’Aaron le pontife, comprendront l’huile du luminaire, l’encens aromatique, l’oblation perpétuelle et l’huile d’onction, la surveillance du tabernacle entier et de tout ce qu’il renferme, du sanctuaire et de son appareil."
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
L’Éternel parla ainsi à Moïse et à Aaron:
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
"N’Exposez point la branche des familles issues de Kehath à disparaître du milieu des Lévites;
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
mais agissez ainsi à leur égard, afin qu’ils vivent au lieu de mourir, lorsqu’ils approcheront des saintetés éminentes: Aaron et ses fils viendront, et les commettront chacun à sa tâche et à ce qu’il doit porter,
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
de peur qu’ils n’entrent pour regarder, fût-ce un instant, les choses saintes, et qu’ils ne meurent."
21 Yehova anawuza Mose kuti,
L’Éternel parla à Moïse en ces termes:
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
"Il faut faire aussi le relevé des enfants de Gerson, par maisons paternelles, selon leurs familles.
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
C’Est depuis l’âge de trente ans et plus, jusqu’à l’âge de cinquante ans, que tu les recenseras: quiconque est apte à participer au service, à faire une besogne dans la tente d’assignation.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
Voici ce qui est imposé aux familles nées de Gerson, comme tâche et comme transport:
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
elles porteront les tapis du tabernacle, le pavillon d’assignation, sa couverture et la housse de tahach qui la couvre extérieurement, ainsi que le rideau-portière de la tente d’assignation;
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
les toiles du parvis, le rideau d’entrée servant de porte à ce parvis, qui s’étend autour du tabernacle et de l’autel, et leurs cordages, et toutes les pièces de leur appareil; enfin, tout ce qui s’y rattache, elles s’en occuperont.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
C’Est sur l’ordre d’Aaron et de ses fils qu’aura lieu tout le service des descendants de Gerson, pour tout ce qu’ils ont à porter comme à exécuter; et vous commettrez à leur garde tout ce qu’ils devront transporter.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
Telle est la tâche des familles descendant de Gerson, dans la tente d’assignation; et leur surveillance appartient à Ithamar, fils d’Aaron le pontife.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Les enfants de Merari, selon leurs familles, par maisons paternelles, tu les recenseras.
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
De l’âge de trente ans et au-dessus, jusqu’à l’âge de cinquante ans, tu les recenseras: tous ceux qui sont admissibles au service, pouvant faire la besogne de la tente d’assignation.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
Voici ce qu’ils sont tenus de porter, selon le détail de leur emploi dans la tente d’assignation: les solives du tabernacle, ses traverses, ses piliers et ses socles;
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
les piliers du pourtour du parvis, leurs socles, leurs chevilles et leurs cordages, avec toutes leurs pièces et tout ce qui s’y rattache. Vous leur attribuerez nominativement les objets dont le transport leur est confié.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
Telle est la tâche des familles descendant de Merari, le détail de leur service dans la tente d’assignation, sous la direction d’Ithamar, fils d’Aaron le pontife."
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Moïse et Aaron, et les phylarques de la communauté, firent le recensement des Kehathites, par familles et maisons paternelles,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
depuis l’âge de trente ans et au-delà, jusqu’à l’âge de cinquante ans, de quiconque était admissible au service, à un emploi dans la tente d’assignation.
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
Recensés ainsi par familles, ils étaient deux mille sept cent cinquante.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Tel fut le contingent des familles nées de Kehath, employées dans la tente d’assignation, ainsi que Moïse et Aaron les recensèrent d’après l’ordre de l’Éternel, transmis par Moïse.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Pour le contingent des enfants de Gerson, dénombrés selon leurs familles et leurs maisons paternelles,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
depuis l’âge de trente ans et au-delà, jusqu’à l’âge de cinquante ans, tous ceux qui étaient admissibles au service, à un emploi dans la tente d’assignation,
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
comptés par familles, selon leurs maisons paternelles, leur nombre fut de deux mille six cent trente.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Tel fut le contingent des familles nées de Gerson, employées dans la tente d’assignation, ainsi que Moïse et Aaron les recensèrent sur l’ordre de l’Éternel.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Et le contingent des familles des enfants de Merari, classés par familles, selon leurs maisons paternelles,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
depuis l’âge de trente ans et au-delà, jusqu’à l’âge de cinquante ans, tous ceux qui étaient admissibles au service, à une tâche dans la tente d’assignation,
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
leur contingent, par familles, fut de trois mille deux cents.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
Tel fut le contingent des familles des enfants de Merari, que Moïse et Aaron dénombrèrent sur l’ordre de l’Éternel, transmis par Moïse.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Total du dénombrement opéré par Moïse, Aaron et les phylarques d’Israël à l’égard des Lévites, selon leurs familles et leurs maisons paternelles,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
de l’âge de trente ans et au-delà, jusqu’à l’âge de cinquante ans, tous ceux qui étaient admissibles à l’exécution d’un service ou à celle d’un transport dans la tente d’assignation:
48 analipo 8,580.
leur nombre fut de huit mille cinq cent quatre-vingts.
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
D’Après l’ordre de l’Éternel, on leur assigna, sous la direction de Moïse, à chacun son service et les objets à transporter ainsi que ses préposés, désignés par l’Éternel à Moïse.

< Numeri 4 >