< Numeri 4 >

1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
Et l’Éternel parla à Moïse et à Aaron, disant:
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Relève la somme des fils de Kehath d’entre les fils de Lévi, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
depuis l’âge de 30 ans et au-dessus, jusqu’à l’âge de 50 ans, tous ceux qui entrent en service pour faire l’œuvre dans la tente d’assignation.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
C’est ici le service des fils de Kehath, dans la tente d’assignation: c’est une chose très sainte.
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
– Et lorsque le camp partira, Aaron et ses fils entreront, et ils démonteront le voile qui sert de rideau, et en couvriront l’arche du témoignage;
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
et ils mettront dessus une couverture de peaux de taissons, et étendront par-dessus un drap tout de bleu; et ils y placeront les barres.
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
Et ils étendront un drap de bleu sur la table des pains de proposition, et mettront sur elle les plats, et les coupes, et les vases, et les gobelets de libation; et le pain continuel sera sur elle.
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
Et ils étendront sur ces choses un drap d’écarlate, et ils le couvriront d’une couverture de peaux de taissons, et ils y placeront les barres.
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
Et ils prendront un drap de bleu, et en couvriront le chandelier du luminaire, et ses lampes, et ses mouchettes, et ses vases à cendre, et tous ses vases à huile, dont on fait usage pour son service;
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
et ils le mettront, avec tous ses ustensiles, dans une couverture de peaux de taissons, et le mettront sur une perche.
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
Et sur l’autel d’or ils étendront un drap de bleu, et le couvriront d’une couverture de peaux de taissons, et y placeront les barres.
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
Et ils prendront tous les ustensiles du service avec lesquels on sert dans le lieu saint, et ils les mettront dans un drap de bleu, et les couvriront d’une couverture de peaux de taissons, et les mettront sur une perche.
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
Et ils ôteront les cendres de l’autel, et ils étendront sur lui un drap de pourpre.
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
Et ils mettront dessus tous ses ustensiles dont on fait usage pour son service: les brasiers, les fourchettes, et les pelles, et les bassins, tous les ustensiles de l’autel; et ils étendront dessus une couverture de peaux de taissons, et y placeront les barres.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
– Et lorsque Aaron et ses fils auront achevé de couvrir le lieu saint et tous les ustensiles du lieu saint, lors du départ du camp, après cela les fils de Kehath viendront pour les porter, afin qu’ils ne touchent pas les choses saintes, et ne meurent pas. C’est là ce que les fils de Kehath porteront de la tente d’assignation.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
Et Éléazar, fils d’Aaron, le sacrificateur, aura la surveillance de l’huile du luminaire, et de l’encens des drogues odoriférantes, et de l’offrande de gâteau continuelle, et de l’huile de l’onction, la surveillance de tout le tabernacle et de tout ce qui y est, du lieu saint et de ses ustensiles.
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
Et l’Éternel parla à Moïse et à Aaron, disant:
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
Ne faites pas que la tribu des familles des Kehathites soit retranchée d’entre les Lévites;
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
et faites ceci pour eux, afin qu’ils vivent et ne meurent pas, en s’approchant du lieu très saint: Aaron et ses fils viendront, et les placeront chacun à son service et à son fardeau.
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
Et ils n’entreront pas pour voir, quand on enveloppera les choses saintes, afin qu’ils ne meurent pas.
21 Yehova anawuza Mose kuti,
Et l’Éternel parla à Moïse, disant:
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
Relève aussi la somme des fils de Guershon, selon leurs maisons de pères, selon leurs familles;
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
tu les dénombreras depuis l’âge de 30 ans et au-dessus, jusqu’à l’âge de 50 ans: tous ceux qui entrent en service pour s’employer au service, à la tente d’assignation.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
C’est ici le service des familles des Guershonites, pour servir et pour porter:
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
ils porteront les tapis du tabernacle et la tente d’assignation, sa couverture, et la couverture de peaux de taissons qui est sur elle par-dessus, et le rideau de l’entrée de la tente d’assignation,
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
et les tentures du parvis, et le rideau de l’entrée de la porte du parvis qui entoure le tabernacle et l’autel, et leurs cordages, et tous les ustensiles de leur service; tout ce qui doit être fait avec eux constituera leur service.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
Tout le service des fils des Guershonites, dans tout ce qu’ils portent et dans tout leur service, sera selon les ordres d’Aaron et de ses fils; et vous leur donnerez en charge tout ce qu’ils doivent porter.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
C’est là le service des familles des fils des Guershonites à la tente d’assignation; et leur charge sera sous la main d’Ithamar, fils d’Aaron, le sacrificateur.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Quant aux fils de Merari, tu les dénombreras selon leurs familles, selon leurs maisons de pères.
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
Tu les dénombreras depuis l’âge de 30 ans et au-dessus, jusqu’à l’âge de 50 ans, tous ceux qui entrent en service pour s’employer au service de la tente d’assignation.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
Et c’est ici la charge de ce qu’ils auront à porter, selon tout leur service à la tente d’assignation: les ais du tabernacle, et ses traverses, et ses piliers, et ses bases,
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
et les piliers du parvis tout autour, et leurs bases, et leurs pieux, et leurs cordages, tous leurs ustensiles, selon tout leur service; et vous leur compterez, [en les désignant] par nom, les objets qu’ils auront charge de porter.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
C’est là le service des familles des fils de Merari, pour tout leur service à la tente d’assignation, sous la main d’Ithamar, fils d’Aaron, le sacrificateur.
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Et Moïse et Aaron, et les princes de l’assemblée, dénombrèrent les fils des Kehathites, selon leurs familles et selon leurs maisons de pères,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
depuis l’âge de 30 ans et au-dessus, jusqu’à l’âge de 50 ans, tous ceux qui entraient en service pour servir dans la tente d’assignation:
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
leurs dénombrés, selon leurs familles, furent 2 750.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Ce sont là les dénombrés des familles des Kehathites, tous ceux qui servaient dans la tente d’assignation, que Moïse et Aaron dénombrèrent selon le commandement de l’Éternel par Moïse.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Et ceux qui furent dénombrés d’entre les fils de Guershon, selon leurs familles, et selon leurs maisons de pères,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
depuis l’âge de 30 ans et au-dessus, jusqu’à l’âge de 50 ans, tous ceux qui entraient en service pour servir à la tente d’assignation:
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
leurs dénombrés, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères, furent 2 630.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Ce sont là les dénombrés des familles des fils de Guershon, tous ceux qui servaient à la tente d’assignation, que Moïse et Aaron dénombrèrent selon le commandement de l’Éternel.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Et ceux qui furent dénombrés d’entre les familles des fils de Merari, selon leurs familles, selon leurs maisons de pères,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
depuis l’âge de 30 ans et au-dessus, jusqu’à l’âge de 50 ans, tous ceux qui entraient en service pour servir à la tente d’assignation:
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
leurs dénombrés, selon leurs familles, furent 3 200.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
Ce sont là les dénombrés des familles des fils de Merari, que Moïse et Aaron dénombrèrent selon le commandement de l’Éternel par Moïse.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Tous ceux qui furent dénombrés, que Moïse et Aaron et les princes d’Israël dénombrèrent, savoir les Lévites, selon leurs familles et selon leurs maisons de pères,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
depuis l’âge de 30 ans et au-dessus, jusqu’à l’âge de 50 ans, tous ceux qui entraient pour s’employer à l’œuvre du service et à l’œuvre du portage, à la tente d’assignation,
48 analipo 8,580.
– les dénombrés, furent 8 580.
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
On les dénombra selon le commandement de l’Éternel par Moïse, chacun selon son service et selon son fardeau; et ils furent dénombrés par lui, comme l’Éternel l’avait commandé à Moïse.

< Numeri 4 >