< Numeri 4 >

1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
Yahvé parla à Moïse et à Aaron, et dit:
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
« Recensez les fils de Kehath parmi les fils de Lévi, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
depuis l'âge de trente ans et au-dessus jusqu'à l'âge de cinquante ans, tous ceux qui entrent au service pour faire le travail dans la tente de la Rencontre.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
Voici le service des fils de Kehath dans la tente d'assignation, en ce qui concerne les choses très saintes.
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
Lorsque le camp avancera, Aaron entrera avec ses fils; ils ôteront le voile du rideau, en couvriront l'arche du Témoignage,
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
la couvriront d'une peau de phoque, étendront sur elle un tissu bleu et placeront ses barres.
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
« Sur la table des pains de proposition, on étendra un drap bleu, et l'on mettra dessus les plats, les cuillères, les coupes et les gobelets pour les verser; le pain de proposition sera dessus.
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
On étendra sur elle un drap écarlate, on la couvrira d'une couverture de peau de phoque, et on y placera ses barres.
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
« Ils prendront un linge bleu et couvriront le chandelier du luminaire, ses lampes, ses éteignoirs, ses plats à priser et tous ses vases à huile, avec lesquels ils le servent.
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
Ils le mettront, ainsi que tous ses ustensiles, dans une enveloppe de peau de phoque, et ils la poseront sur le cadre.
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
« Sur l'autel d'or, on étendra un linge bleu, on le couvrira d'une housse de peau de phoque, et l'on mettra ses perches.
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
« Ils prendront tous les ustensiles avec lesquels on fait le service dans le sanctuaire, ils les mettront dans un drap bleu, les couvriront d'une enveloppe de peau de phoque, et les mettront sur le cadre.
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
« Ils enlèveront les cendres de l'autel, et ils étendront sur lui un tissu de pourpre.
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
Ils y mettront tous les ustensiles avec lesquels on fait le service, les poêles à feu, les crochets à viande, les pelles et les bassins, tous les ustensiles de l'autel; ils étendront sur lui une couverture de peau de phoque, et ils mettront ses barres.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
« Quand Aaron et ses fils auront fini de couvrir le sanctuaire et tous les meubles du sanctuaire, pendant que le camp avancera, les fils de Kehath viendront les porter; mais ils ne toucheront pas le sanctuaire, de peur de mourir. Les fils de Kehath porteront ces objets appartenant à la Tente d'assignation.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
« Le devoir du prêtre Éléazar, fils d'Aaron, sera l'huile pour le feu, le parfum doux, l'offrande perpétuelle et l'huile d'onction, les exigences de tout le tabernacle et de tout ce qui s'y trouve, du sanctuaire et de son mobilier. »
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
Yahvé parla à Moïse et à Aaron, et dit:
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
« N'extermine pas la tribu des familles des Kehathites du milieu des Lévites;
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
mais fais-leur ceci, afin qu'ils vivent et ne meurent pas, lorsqu'ils s'approcheront des choses très saintes: Aaron et ses fils entreront et assigneront chacun à son service et à sa charge;
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
mais ils n'entreront pas pour voir le sanctuaire, même pour un instant, de peur de mourir. »
21 Yehova anawuza Mose kuti,
L'Éternel parla à Moïse, et dit:
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
« Recense aussi les fils de Guershon, selon les maisons de leurs pères, selon leurs familles;
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
tu les compteras depuis l'âge de trente ans et au-dessus jusqu'à l'âge de cinquante ans, tous ceux qui entrent pour faire le service, pour faire l'ouvrage dans la tente de la Rencontre.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
« C'est ici le service des familles des Guershonites, en servant et en portant des fardeaux:
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
Ils porteront les tapis du tabernacle et de la tente d'assignation, sa couverture, la couverture en peau de phoque qui la recouvre, le rideau de l'entrée de la tente d'assignation,
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
les tentures du parvis, le rideau de l'entrée de la porte du parvis qui est près du tabernacle et autour de l'autel, leurs cordages, tous les instruments de leur service, et tout ce qu'on fera avec eux. C'est là qu'ils feront leur service.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
Sur l'ordre d'Aaron et de ses fils, il y aura tout le service des fils des Gershonites, dans toute leur charge et dans tout leur service, et vous leur assignerez leur tâche dans toutes leurs responsabilités.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
Voici le service des familles des fils des Gershonites dans la Tente d'assignation. Leur service sera sous la responsabilité d'Ithamar, fils du prêtre Aaron.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
« Tu compteras les fils de Merari selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères;
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
tu les compteras depuis l'âge de trente ans et au-dessus jusqu'à l'âge de cinquante ans, tous ceux qui entrent dans le service, pour faire le travail de la Tente de la Rencontre.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
Voici la charge qui leur incombe, selon tout le service qu'ils font dans la Tente d'assignation: les planches de la tente, ses barres, ses piliers, ses socles,
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
les piliers du parvis qui l'entourent, leurs socles, leurs broches, leurs cordes, avec tous leurs instruments et avec tout leur service. Tu leur désigneras par leur nom les instruments du service de leur charge.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
Tel est le service des familles des fils de Merari, selon tout leur service dans la Tente d'assignation, sous la direction d'Ithamar, fils du prêtre Aaron. »
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Moïse, Aaron et les chefs de l'assemblée firent le compte des fils des Kehathites, selon leurs familles et selon les maisons de leurs pères,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
depuis l'âge de trente ans et au-dessus jusqu'à l'âge de cinquante ans, tous ceux qui entraient en service pour travailler dans la tente de la Rencontre.
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
Ceux dont on fit le compte, selon leurs familles, furent deux mille sept cent cinquante.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Tels sont ceux qui furent comptés parmi les familles des Kehathites, tous ceux qui faisaient le service dans la Tente de la Rencontre, et dont Moïse et Aaron firent le compte, selon le commandement de l'Éternel par Moïse.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Ceux des fils de Guershon dont on fit le dénombrement, selon leurs familles et leurs maisons de pères,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
depuis l'âge de trente ans et au-dessus jusqu'à l'âge de cinquante ans, tous ceux qui se mirent au service de la Tente d'assignation,
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
ceux dont on fit le dénombrement, selon leurs familles et leurs maisons de pères, furent deux mille six cent trente.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
Tels sont ceux qui furent comptés parmi les familles des fils de Guershon, tous ceux qui servirent dans la Tente de la Rencontre, et dont Moïse et Aaron firent le compte, selon le commandement de l'Éternel.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Ceux des familles des fils de Merari dont on fit le dénombrement, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
depuis l'âge de trente ans et au-dessus jusqu'à l'âge de cinquante ans, tous ceux qui furent admis à travailler dans la tente d'assignation,
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
ceux dont on fit le dénombrement selon leurs familles, furent trois mille deux cents.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
Tels sont ceux des familles des fils de Merari dont Moïse et Aaron firent le compte, selon le commandement de l'Éternel par Moïse.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Tous ceux des Lévites dont Moïse, Aaron et les chefs d'Israël firent le dénombrement, selon leurs familles et selon les maisons de leurs pères,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
depuis l'âge de trente ans et au-dessus jusqu'à l'âge de cinquante ans, tous ceux qui entraient pour faire le service et porter les fardeaux dans la tente d'assignation,
48 analipo 8,580.
ceux qui furent dénombrés parmi eux, furent huit mille cinq cent quatre-vingts.
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
Ils furent comptés par Moïse, selon le commandement de l'Éternel, chacun selon son service et selon son fardeau. C'est ainsi qu'ils furent comptés par lui, comme Yahvé l'avait ordonné à Moïse.

< Numeri 4 >