< Numeri 4 >
1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
And the LORD spake unto Moses and unto Aaron, saying,
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Take the sum of the sons of Kohath from among the sons of Levi, by their families, by their fathers’ houses,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
from thirty years old and upward even until fifty years old, all that enter upon the service, to do the work in the tent of meeting.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
This is the service of the sons of Kohath in the tent of meeting, [about] the most holy things:
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
when the camp setteth forward, Aaron shall go in, and his sons, and they shall take down the veil of the screen, and cover the ark of the testimony with it:
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
and shall put thereon a covering of sealskin, and shall spread over it a cloth all of blue, and shall put in the staves thereof.
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
And upon the table of shewbread they shall spread a cloth of blue, and put thereon the dishes, and the spoons, and the bowls, and the cups to pour out withal: and the continual bread shall be thereon:
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
and they shall spread upon them a cloth of scarlet, and cover the same with a covering of sealskin, and shall put in the staves thereof.
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
And they shall take a cloth of blue, and cover the candlestick of the light, and its lamps, and its tongs, and its snuffdishes, and all the oil vessels thereof, wherewith they minister unto it:
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
and they shall put it and all the vessels thereof within a covering of sealskin, and shall put it upon the frame.
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
And upon the golden altar they shall spread a cloth of blue, and cover it with a covering of sealskin, and shall put in the staves thereof:
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
and they shall take all the vessels of ministry, wherewith they minister in the sanctuary, and put them in a cloth of blue, and cover them with a covering of sealskin, and shall put them on the frame.
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
And they shall take away the ashes from the altar, and spread a purple cloth thereon:
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
and they shall put upon it all the vessels thereof, wherewith they minister about it, the firepans, the fleshhooks, and the shovels, and the basons, all the vessels of the altar; and they shall spread upon it a covering of sealskin, and put in the staves thereof.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
And when Aaron and his sons have made an end of covering the sanctuary, and all the furniture of the sanctuary, as the camp is to set forward; after that, the sons of Kohath shall come to bear it: but they shall not touch the sanctuary, lest they die. These things are the burden of the sons of Kohath in the tent of meeting.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
And the charge of Eleazar the son of Aaron the priest shall be the oil for the light, and the sweet incense, and the continual meal offering, and the anointing oil, the charge of all the tabernacle, and of all that therein is, the sanctuary, and the furniture thereof.
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
And the LORD spake unto Moses and unto Aaron, saying,
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
Cut ye not off the tribe of the families of the Kohathites from among the Levites:
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
but thus do unto them, that they may live, and not die, when they approach unto the most holy things: Aaron and his sons shall go in, and appoint them every one to his service and to his burden:
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
but they shall not go in to see the sanctuary even for a moment, lest they die.
21 Yehova anawuza Mose kuti,
And the LORD spake unto Moses, saying,
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
Take the sum of the sons of Gershon also, by their fathers’ houses, by their families;
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
from thirty years old and upward until fifty years old shalt thou number them; all that enter in to wait upon the service, to do the work in the tent of meeting.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
This is the service of the families of the Gershonites, in serving and in bearing burdens:
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
they shall bear the curtains of the tabernacle, and the tent of meeting, its covering, and the covering of sealskin that is above upon it, and the screen for the door of the tent of meeting;
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
and the hangings of the court, and the screen for the door of the gate of the court, which is by the tabernacle and by the altar round about, and their cords, and all the instruments of their service, and whatsoever shall be done with them, therein shall they serve.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
At the commandment of Aaron and his sons shall be all the service of the sons of the Gershonites, in all their burden, and in all their service: and ye shall appoint unto them in charge all their burden.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
This is the service of the families of the sons of the Gershonites in the tent of meeting: and their charge shall be under the hand of Ithamar the son of Aaron the priest.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
As for the sons of Merari, thou shalt number them by their families, by their fathers’ houses;
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
from thirty years old and upward even unto fifty years old shalt thou number them, every one that entereth upon the service, to do the work of the tent of meeting.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
And this is the charge of their burden, according to all their service in the tent of meeting; the boards of the tabernacle, and the bars thereof, and the pillars thereof, and the sockets thereof;
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
and the pillars of the court round about, and their sockets, and their pins, and their cords, with all their instruments, and with all their service: and by name ye shall appoint the instruments of the charge of their burden.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
This is the service of the families of the sons of Merari, according to all their service, in the tent of meeting, under the hand of Ithamar the son of Aaron the priest.
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
And Moses and Aaron and the princes of the congregation numbered the sons of the Kohathites by their families, and by their fathers’ houses,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
from thirty years old and upward even unto fifty years old, every one that entered upon the service, for work in the tent of meeting:
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
and those that were numbered of them by their families were two thousand seven hundred and fifty.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
These are they that were numbered of the families of the Kohathites, all that did serve in the tent of meeting, whom Moses and Aaron numbered according to the commandment of the LORD by the hand of Moses.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
And those that were numbered of the sons of Gershon, by their families, and by their fathers’ houses,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
from thirty years old and upward even unto fifty years old, every one that entered upon the service, for work in the tent of meeting,
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
even those that were numbered of them, by their families, by their fathers’ houses, were two thousand and six hundred and thirty.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
These are they that were numbered of the families of the sons of Gershon, all that did serve in the tent of meeting, whom Moses and Aaron numbered according to the commandment of the LORD.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
And those that were numbered of the families of the sons of Merari, by their families, by their fathers’ houses,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
from thirty years old and upward even unto fifty years old, every one that entered upon the service, for work in the tent of meeting,
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
even those that were numbered of them by their families, were three thousand and two hundred.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
These are they that were numbered of the families of the sons of Merari, whom Moses and Aaron numbered according to the commandment of the LORD by the hand of Moses.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
All those that were numbered of the Levites, whom Moses and Aaron and the princes of Israel numbered, by their families, and by their fathers’ houses,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
from thirty years old and upward even unto fifty years old, every one that entered in to do the work of service, and the work of bearing burdens in the tent of meeting,
even those that were numbered of them, were eight thousand and five hundred and fourscore.
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
According to the commandment of the LORD they were numbered by the hand of Moses, every one according to his service, and according to his burden: thus were they numbered of him, as the LORD commanded Moses.