< Numeri 4 >
1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
And the Lord spoke unto Moses and unto Aaron, saying,
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Take the sum of the sons of Kehath from among the sons of Levi, after their families, by their divisions,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
From thirty years old and upward even until fifty years old, all that are fitted for the service, to do work at the tabernacle of the congregation.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
This shall be the service of the sons of Kehath at the tabernacle of the congregation: The most holy things.
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
And Aaron shall come with his sons, when the camp setteth forward, and they shall take down the vail of the separation, and cover therewith the ark of the testimony;
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
And they shall put over it a covering of badgers' skins, and they shall spread over all a cloth wholly of blue [woollen yarn], and they shall put in its staves.
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
And over the table of the showbread shall they spread a cloth of blue, and put thereon the dishes, and the spoons, and the tubes, and the staves of the covering; and the continual bread shall be thereon:
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
And they shall spread over them a cloth of scarlet, and cover the same with a covering of badgers' skins; and they shall put in its staves.
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
And they shall take a cloth of blue, and cover the candlestick of the lighting, and its lamps, and its tongs, and its snuff-dishes, and all the oil-vessels thereof, wherewith they minister by it:
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
And they shall put it and all its vessels within a covering of badgers' skins, and they shall put it upon a barrow.
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
And over the golden altar shall they spread a cloth of blue, and cover it with a covering of badgers' skins; and they shall put in its staves.
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
And they shall take all the vessels of the service, wherewith they minister in the sanctuary, and put them in a cloth of blue, and cover them with a covering of badgers' skins; and they shall put them on a barrow.
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
And they shall take away the ashes from the altar, and spread over it a cloth of purple;
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
And they shall put upon it all its vessels, wherewith they minister upon it, the fire-pans, the forks, and the shovels, and the basins, all the vessels of the altar; and they shall spread over it a covering of badgers' skins, and put in its staves.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
And when Aaron and his sons have thus made an end of covering the sanctuary, and all the vessels of the sanctuary, when the camp is to set forward: then shall, after that, the sons of Kehath come to carry it; but they shall not touch any holy thing, lest they die; these are the things which the sons of Kehath are to carry at the tabernacle of the congregation.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
And under the supervision of Elazar the son of Aaron the priest shall be the oil for the lighting, and the incense of spices, and the daily meat-offering, and the anointing-oil; the supervision of all the tabernacle, and of all that is therein, over the sanctuary, and over its vessels.
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
And the Lord spoke unto Moses and unto Aaron, saying,
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
Do ye not cause the tribe of the families of the Kehathites to be cut off from among the Levites;
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
But thus do unto them, that they may live, and not die, when they approach unto the most holy things: Aaron and his sons shall go in, and appoint them, every one, to his service and to his burden;
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
That they may not go in to see when the holy things are covered, and die.
21 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
Take also the sum of the sons of Gershon, by their divisions, after their families;
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
From thirty years old and upward until fifty years old shalt thou number them; all that are fitted for the service, to do work in the tabernacle of the congregation.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
This shall be the service of the families of the Gershunites, to serve, and to carry:
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
They shall carry the curtains of the tabernacle, and of the tent of the congregation, its covering, and the covering of the badgers' skins that is over it above, and the hanging for the door of the tabernacle of the congregation,
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
And the hangings of the court, and the hanging for the door of the gate of the court, which is by the tabernacle and by the altar round about, and their cords, and all the vessels of their service; and all that is delivered to them shall they perform.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
By the order of Aaron and his sons shall be all the service of the sons of the Gershunites, in all their carrying, and in all their service: and ye shall designate unto them in charge all which they have to carry.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
This is the service of the families of the sons of the Gershunites at the tabernacle of the congregation; their charge shall be under the supervision of Ithamar the son of Aaron the priest.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
The sons of Merari, shalt thou number after their families, by their divisions;
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
From thirty years old and upward, even until fifty years old, shalt thou number them, every one that is fitted for the service, to do the work of the tabernacle of the congregation.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
And this is what is confided to them to carry, regarding all their service at the tabernacle of the congregation: The boards of the tabernacle, and its bars, and its pillars, and its sockets,
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
And the pillars of the court round about, and their sockets, and their pins, and their cords, with all their instruments, and all which belongeth thereto; and by name shall ye designate [to them] the vessels which are confided to them to carry.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
This is the service of the families of the sons of Merari, regarding all their service, at the tabernacle of the congregation, under the supervision of Ithamar the son of Aaron, the priest.
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
And Moses with Aaron and the princes of the congregation numbered the sons of the Kehathites after their families, and after their divisions,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
From thirty years old and upward, even until fifty years old, every one that was fitted for the service, for the work at the tabernacle of the congregation.
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
And those that were numbered of them after their families were two thousand seven hundred and fifty.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
These were they that were numbered of the families of the Kehathites, all that could do service at the tabernacle of the congregation, whom Moses with Aaron numbered by the order of the Lord through the hand of Moses.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
And those that were numbered of the sons of Gershon, after their families, and after their divisions,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
From thirty years old and upward, even until fifty years old, every one that was fitted for the service, for the work at the tabernacle of the congregation,
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
Even those that were numbered of them, after their families, after their divisions, were two thousand and six hundred and thirty.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
These are they that were numbered of the families of the sons of Gershon, all that could do service at the tabernacle of the congregation, whom Moses with Aaron numbered by the order of the Lord.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
And those that were numbered of the families of the sons of Merari, after their families, after their divisions,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
From thirty years old and upward, even until fifty years old, every one that was fitted for the service, for the work at the tabernacle of the congregation.
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
Even those that were numbered of them after their families, were three thousand and two hundred.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
These are those that were numbered of the families of the sons of Merari, whom Moses with Aaron numbered by the order of the Lord through the hand of Moses.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
All those that were numbered of the Levites, whom Moses with Aaron and the chiefs of Israel numbered, after their families, and after their divisions,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
From thirty years old and upward, even until fifty years old, every one that came to do the service of the ministry, and the service of the carrying at the tabernacle of the congregation,
Even those that were numbered of them, were eight thousand and five hundred and eighty.
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
By the order of the Lord through the hand of Moses, did he appoint them, every one to his proper service, and to his proper carrying: and they were numbered, as the Lord had commanded Moses.