< Numeri 36 >

1 Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
Тада приступише старешине из породице синова Галада сина Махира сина Манасијиног од племена синова Јосифових, и рекоше пред Мојсијем и пред кнезовима, главарима од домова отачких међу синовима Израиљевим,
2 Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
И говорише: Господару нашем заповеди Господ да подели жребом земљу у наследство синовима Израиљевим; и господар наш има заповест од Господа да да наследство Салпада, брата нашег кћерима његовим.
3 Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
Ако се оне удаду за кога из другог племена синова Израиљевих, онда ће се наследство њихово откупити од наследства отаца наших и додаће се наследству оног племена у које се удаду, и тако ће се део наш окрњити.
4 Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
И кад буде опросна година синовима Израиљевим, опет ће остати наследство њихово с наследством оног племена у које се буду удале, и тако ће од наследства племена отаца наших остати откинуто наследство њихово.
5 Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
Тада заповеди Мојсије синовима Израиљевим по заповести Господњој говорећи: Право говори племе синова Јосифових.
6 Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
Ово заповеди Господ за кћери Салпадове и рече: Нека се удаду за кога им буде воља, али у породици племена свог нека се удаду.
7 kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
Да се не би преносило наследство синова Израиљевих од једног племена на друго; јер ће синови Израиљеви држати сваки наследство племена отаца својих.
8 Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
И свака кћи у племенима синова Израиљевих којој допадне наследство, нека се удаје за кога из породице племена оца свог, да би синови Израиљеви држали сваки наследство отаца својих,
9 Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
Да се не би преносило наследство од једног племена синова Израиљевих да држи своје наследство.
10 Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
Како заповеди Господ Мојсију, тако учинише кћери Салпадове.
11 Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
Јер Мала и Терса и Егла и Мелха и Нуја, кћери Салпадове, удадоше се за синове стричева својих,
12 Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
У породице синова Манасије сина Јосифовог удадоше се, и оста наследство њихово у племену породице оца њиховог.
13 Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.
То су заповести и закони, које заповеди Господ преко Мојсија синовима Израиљевим у пољу моавском на Јордану према Јерихону.

< Numeri 36 >