< Numeri 36 >

1 Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
Les chefs de famille des fils de Galaad, fils de Makir, fils de Manassé, des familles des fils de Joseph, s'approchèrent et parlèrent devant Moïse et devant les princes, les chefs de famille des enfants d'Israël.
2 Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
Ils dirent: « Yahvé a ordonné à mon seigneur de donner le pays en héritage par tirage au sort aux enfants d'Israël. Mon seigneur a reçu l'ordre de Yahvé de donner l'héritage de Zelophehad, notre frère, à ses filles.
3 Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
Si elles se marient à l'un des fils des autres tribus des enfants d'Israël, leur héritage sera retranché de l'héritage de nos pères et ajouté à l'héritage de la tribu à laquelle elles appartiendront. Il sera ainsi retranché du lot de notre héritage.
4 Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
Quand viendra le jubilé des enfants d'Israël, leur héritage sera ajouté à l'héritage de la tribu à laquelle ils appartiendront. Ainsi leur héritage sera retranché de l'héritage de la tribu de nos pères. »
5 Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
Moïse donna aux enfants d'Israël un ordre conforme à la parole de Yahvé, en disant: « La tribu des fils de Joseph dit ce qui est juste.
6 Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
Voici ce que l'Éternel ordonne pour les filles de Zelophehad: Qu'elles se marient à qui bon leur semble, mais elles se marieront dans la famille de la tribu de leur père.
7 kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
Ainsi, aucun héritage des enfants d'Israël ne passera d'une tribu à l'autre, car les enfants d'Israël conserveront tous l'héritage de la tribu de leurs pères.
8 Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
Toute fille qui possédera un héritage dans une tribu des enfants d'Israël sera la femme d'un membre de la famille de la tribu de son père, afin que les enfants d'Israël possèdent chacun l'héritage de leurs pères.
9 Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
Ainsi, aucun héritage ne passera d'une tribu à une autre tribu, car les tribus des enfants d'Israël garderont chacune leur héritage.'"
10 Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
Les filles de Tselophehad firent ce que l'Éternel avait ordonné à Moïse:
11 Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
car Mahla, Tirza, Hogla, Milca et Noé, filles de Tselophehad, furent mariées aux fils des frères de leur père.
12 Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
Elles furent mariées dans les familles des fils de Manassé, fils de Joseph. Leur héritage resta dans la tribu de la famille de leur père.
13 Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.
Tels sont les commandements et les ordonnances que Yahvé a prescrits par Moïse aux enfants d'Israël dans les plaines de Moab, près du Jourdain, à Jéricho.

< Numeri 36 >