< Numeri 36 >

1 Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
Forsothe and the princes of the meynees of Galaad sone of Machir, sone of Manasses, of the generacioun of the sones of Joseph, neiyiden, and spaken to Moises bifor the princes of Israel,
2 Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
and seiden, The Lord comaundide to thee oure lord, that thou schuldist departe the lond bi lot to the sones of Israel, and that thou schuldist yyue to the douytris of Salphaat, oure brothir, possessioun due to the fadir.
3 Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
And if men of anothir lynage schulen take to wyues these douytris, her possessioun schal sue, and it schal be translatid to anothir lynage, and schal be decreessid fro oure eritage;
4 Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
and so it schal be doon, that whanne the iubilee, that is, the fiftithe yeer of remyssioun, cometh, the departyng of lottis be schent, and that the possessioun of othere men passe to othere men.
5 Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
Moises answeride to the sones of Israel, and seide, for the Lord comaundide, The lynage of the sones of Joseph spak riytfuli,
6 Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
and this lawe is denounsid of the Lord on the douytris of Salphaat; be thei weddid to whiche men thei wolen, oneli to the men of her lynage;
7 kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
lest the possessioun of the sones of Joseph be meddlid fro lynage in to lynage. For alle men schulen wedde wyues of her lynage and kynrede;
8 Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
and alle wymmen schulen take hosebondis of the same lynage, that the erytage dwelle in meynees,
9 Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
and lynagis be not meddlid to hem silf, but dwelle so,
10 Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
as tho ben departid of the Lord. And the douytris of Salphaat diden, as it was comaundid to hem.
11 Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
And Maala, and Thersa, and Egla, and Melcha, and Noha, weren weddid to the sones of her fadris brother,
12 Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
of the meynee of Manaasses, that was `the sone of Joseph, and the possessioun that was youun to hem, dwellide in the lynage and meynee of her fadir.
13 Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.
These ben the comaundementis and domes, whiche the Lord comaundide, bi the hond of Moyses, to the sones of Israel, in the feeldi places of Moab, aboue Jordan, ayens Jericho.

< Numeri 36 >