< Numeri 36 >

1 Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
And the chief fathers of families of the sons of Gilead, the son of Machir, the son of Manasseh, of the families of the sons of Joseph, came near, and spoke before Moses, and before the princes, the chief fathers of the children of Israel:
2 Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
and they said, Jehovah commanded my lord to give the land for an inheritance by lot to the children of Israel; and my lord was commanded by Jehovah to give the inheritance of Zelophehad our brother to his daughters.
3 Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
Now if they be married to any of the sons of the [other] tribes of the children of Israel, then shall their inheritance be taken from the inheritance of our fathers, and shall be added to the inheritance of the tribe to which they shall belong; and it shall be taken from the lot of our inheritance.
4 Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
And when the jubilee of the children of Israel shall come, then shall their inheritance be added to the inheritance of the tribe to which they shall belong; and their inheritance shall be taken away from the inheritance of the tribe of our fathers.
5 Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
And Moses commanded the children of Israel according to the word of Jehovah, saying, The tribe of the sons of Joseph hath said well.
6 Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
This is the thing which Jehovah hath commanded concerning the daughters of Zelophehad, saying, Let them marry whom they please; only they shall marry one of the tribe of their father,
7 kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
that no inheritance of the children of Israel pass from tribe to tribe; for every one of the children of Israel shall keep to the inheritance of the tribe of his fathers.
8 Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
And every daughter that possesseth an inheritance among the tribes of the children of Israel, shall be married to one of the family of the tribe of her father, that the children of Israel may possess every one the inheritance of his fathers,
9 Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
and the inheritance shall not pass from one tribe to another tribe; for each of the tribes of the children of Israel shall keep to his inheritance.
10 Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
Even as Jehovah had commanded Moses, so did the daughters of Zelophehad;
11 Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
and Mahlah, Tirzah, and Hoglah, and Milcah, and Noah, the daughters of Zelophehad, were married unto their uncles' sons.
12 Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
To those that were of the families of the sons of Manasseh the son of Joseph were they married; and their inheritance remained in the tribe of the family of their father.
13 Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.
These are the commandments and the ordinances which Jehovah commanded through Moses to the children of Israel, in the plains of Moab, by the Jordan of Jericho.

< Numeri 36 >