< Numeri 35 >

1 Ku zigwa za Mowabu pafupi ndi Yorodani ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
I mluvil Hospodin k Mojžíšovi na rovinách Moábských, při Jordánu proti Jerichu, řka:
2 “Lamula Aisraeli kuti apereke kwa Alevi midzi yoti azikhalamo kuchokera pa cholowa chomwe adzalandira. Muwapatsenso malo oweteramo ziweto kuzungulira midziyo.
Přikaž synům Izraelským, ať dadí Levítům z dědictví, kterýmž vládnouti budou, města k bydlení, i podměstí měst vůkol nich,
3 Midziyo idzakhala yawo ndipo azidzakhala mʼmenemo. Malo a msipu adzakhala a ngʼombe, nkhosa ndi zoweta zawo zina zonse.
Aby měli města k bydlení, podměstí pak jejich pro dobytky jejich, i pro statky jejich, a pro všecka hovada jejich.
4 “Malo a msipu a mudziwo amene mudzawapatse Aleviwo, adzayambire ku khoma la mudzi ndipo adzatuluke kunja mamita 450, kuzungulira mudziwo.
Podměstí pak měst, kteráž dáte Levítům, vzdálí budou ode zdi městské na tisíc loktů zevnitř vůkol.
5 Kunja kwa mudzi yezani mamita 900 kummawa, mamita 900 kumpoto ndipo mudziwo ukhale pakati. Adzakhala ndi dera limeneli ngati malo a midziyo, owetera ziweto zawo.
Protož vyměříte vně za každým městem na východ slunce dva tisíce loktů, na poledne též dva tisíce loktů, také na západ dva tisíce loktů, i na půlnoci dva tisíce loktů, tak aby bylo město v prostředku. Ta bude míra podměstí měst jejich.
6 “Isanu ndi umodzi mwa midzi imene mudzapereke kwa Alevi idzakhala mizinda yopulumukirako, kumene munthu wopha mnzake adzathawireko. Ndipo mudzawapatsenso midzi ina 42.
Z těch pak měst, kteráž dáte Levítům, oddělíte šest měst k útočišti, aby tam utekl, kdož by někoho zabil; a k těm přidáte jim ještě čtyřidceti dvě města.
7 Midzi yonse imene mudzapereke kwa Alevi idzakhale 48, pamodzi ndi malo oweterako ziweto.
I bude všech měst, kteráž dáte Levítům, čtyřidceti osm měst i s podměstími jejich.
8 Pamene mukupatula midzi imeneyi pa cholowa cha Aisraeli, muchotsepo midzi yambiri pa mafuko aakulu, ndipo midzi pangʼono pa mafuko aangʼono. Fuko lililonse lidzapereka kwa Alevi molingana ndi kukula kwa cholowa chimene lalandira.”
Těch pak měst, kteráž dáte z vládařství synů Izraelských, od těch, kteříž více mají, více vezmete, a od těch, kteříž méně mají, méně vezmete; jedno každé pokolení vedlé velikosti dědictví, jímž vládnouti budou, dá z měst svých Levítům.
9 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
I mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
10 “Yankhula ndi Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mu Kanaani,
Mluv k synům Izraelským a rci jim: Když přejdete Jordán, a vejdete do země Kananejské,
11 sankhani midzi ina kuti ikhale mizinda yanu yopulumukirako, kumene munthu wopha munthu wina mwangozi angathawireko.
Vybéřete sobě města, a ta města budete míti k utíkání, aby tam utekl ten, kterýž by někoho zabil z nedopatření.
12 Adzakhala malo obisalako pothawa munthu wofuna kulipsira, kuti munthu wopha mnzake mwangozi asaphedwe mpaka akayime pamaso pa gulu la anthu kuti akaweruzidwe.
A budou vám ta města k útočišti před přítelem, aby neumřel ten, kdož zabil, dokudž by se nepostavil před shromážděním k soudu.
13 Midzi isanu ndi umodzi imene muyiperekeyi idzakhala mizinda yopulumukirako.
Z těch tedy měst, kteráž dáte, šest měst k útočišti míti budete.
14 Mupereke itatu mbali ino ya Yorodani ndi itatu ina mu Kanaani kuti ikhale mizinda yopulumukirako.
Tři města dáte před Jordánem, též tři města dáte v zemi Kananejské; i budou města útočiště.
15 Midzi isanu ndi umodzi idzakhala malo opulumukirako Aisraeli, alendo ndi anthu ena onse okhala pakati pawo kuti wina aliyense wopha mnzake mwangozi adzathawireko.
Synům Izraelským i příchozímu, i podruhu mezi nimi bude těch šest měst k útočišti, aby tam utekl, kdož by koli ranil někoho z nedopatření.
16 “‘Ngati munthu amenya mnzake ndi chitsulo, munthuyo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha ndipo wakuphayo aphedwe.
Jestliže by pak železem ranil někoho, tak až by umřel, vražedlník jest; smrtí umře vražedlník takový.
17 Kapenanso ngati wina wake ali ndi mwala mʼdzanja mwake womwe ungaphe munthu, ndipo agenda nawo wina, munthu winayo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha ndipo wakuphayo adzayenera kuphedwa.
Pakli by hodě kamenem, jímž by mohl zabiti, udeřil někoho, tak že by umřel, vražedlník jest; smrtí umře vražedlník takový.
18 Kapenanso ngati wina ali ndi chibonga mʼdzanja mwake choti nʼkupha nacho munthu, namenya nacho munthu, munthuyo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha, wakuphayo ayenera kuphedwa.
Pakli by hodě dřevem, kterýmž by mohl zabiti, udeřil někoho, tak že by umřel, vražedlník jest; smrtí umře vražedlník takový.
19 Wolipsira adzamuphanso wakuphayo. Pamene akumana naye adzayenera kumupha ndithu.
Přítel zabitého zabije vražedlníka toho; kdyžkoli ho dostane, on sám zabije ho.
20 Ndipo ngati wina wake, chifukwa cha udani, aganiza zokankha munthu wina kapena kumuponyera chinthu china mwadala munthuyo nʼkufa,
Aneb jestliže by z nenávisti strčil někým, aneb shodil by něco na něho z úkladu, tak že by od toho umřel;
21 kapena ngati, chifukwa cha udani, amenya mnzake ndi nkhonya, mnzakeyo ndi kufa, munthuyo ayenera kuphedwa. Iyeyo ndi wakupha. Wolipsira adzamuphe wakuphayo pamene akumana naye.
Aneb jestliže by z nepřátelství rukou udeřil někoho, tak že by umřel: smrtí umře bitec ten, vražedlník jest; přítel zabitého zabije vražedlníka toho, jakž ho nejprv dostane.
22 “‘Koma ngati popanda udani wina uliwonse, mwadzidzidzi akankha wina kapena kumuponyera chinthu osati mwadala,
Jestliže by pak náhodou a ne z nepřátelství strčil někým, aneb shodil by na něho nějakou věc bez úkladu;
23 kapena mosamuona nʼkumuponyera mwala womwe utha kumupha, munthuyo nʼkufa, tsono pakuti sanali mdani wake ndipo sanaganizire zomupweteka,
Aneb jaký koli kámen, od něhož by umříti mohl, shodil by na něj z nedopatření, tak že by umřel, nebyv s ním v nepřátelství, ani nehledaje zlého jeho:
24 gulu liweruze pakati pa iye ndi wolipsira monga mwa malamulo ake.
Tedy souditi bude shromáždění mezi bitcem a mezi přítelem zabitého vedlé soudů těchto.
25 Gulu lidzapulumutsa munthu wakuphayo mʼmanja mwa wolipsira uja ndi kumubwezera ku mzinda wopulumukirako kumene anathawira. Ayenera kukhala kumeneko kufikira imfa ya mkulu wa ansembe, amene anadzozedwa ndi mafuta oyera.
A vysvobodí shromáždění vražedlníka toho z rukou přítele zabitého, a káže se jemu navrátiti shromáždění k městu útočiště jeho, do něhož utekl; i bude bydliti v něm, dokudž neumře kněz nejvyšší, kterýž pomazán jest olejem svatým.
26 “‘Koma ngati wolakwayo atuluka kunja kwa malire a mzinda wopulumukirako kumene anathawira
Jestliže by pak ten, kterýž zabil člověka, vyšel z mezí města útočiště svého, do něhož utekl,
27 ndipo wobwezera choyipa nʼkumupeza kunja kwa mzindawo, wolipsirayo atha kumupha wolakwayo popanda kugamula mlandu wakupha.
A přítel zabitého našel by jej vně, an přešel meze města útočiště svého, a zabil by přítel zabitého vražedlníka toho, nebude vinen krví.
28 Wolakwayo ayenera kukhala mu mzinda wopulumukiramowo mpaka imfa ya mkulu wa ansembe ndipo pamenepo atha kubwerera kwawo. Pokhapokha atafa mkulu wa ansembe ndi pamene angathe kubwerera ku malo ake.
Nebo v městě útočiště svého bydliti má, dokudž by neumřel kněz nejvyšší. Když by pak umřel kněz nejvyšší, navrátí se vražedlník do země vládařství svého.
29 “‘Amenewa akhale malamulo ndi malangizo kwa inu nthawi zonse ndi ku mibado ya mʼtsogolo, kulikonse kumene mudzakhalako.
A bude vám toto za ustanovení soudné v pronárodech vašich, ve všech příbytcích vašich.
30 “‘Aliyense wopha munthu ayeneranso kuphedwa ngati pali umboni okwanira. Koma wina asaphedwe ngati pali mboni imodzi yokha.
Kdož by koli měl na smrt vydati někoho, podlé vyznání svědků sáhne na vražedlníka; ale jeden svědek nebude moci svědčiti proti někomu na smrt.
31 “‘Osalola kulandira dipo lowombolera munthu wakupha yemwe ayenera kuphedwa. Wakupha ayenera kuphedwa.
Nevezmete pak výplaty za člověka vražedlníka, kterýž, jsa nešlechetný, jest smrti hoden, než smrtí ať umře.
32 “‘Simuyeneranso kulandira dipo kwa munthu amene wathawira ku mzinda wopulumikirako kuti wothawayo abwerere kwawo, pokhapokha ngati mkulu wa ansembe wamwalira.
Aniž také vezmete výplaty od toho, kterýž utekl do města útočiště svého, aby se navrátil k bydlení do země své, prvé než by umřel kněz,
33 “‘Musayipitse dziko limene mukukhalamolo. Magazi amayipitsa dziko ndipo nʼkosatheka kulipirira dziko chifukwa cha magazi amene akhetsedwa mʼmenemo, kupatula pokhetsa magazi a munthu amene anakhetsa magaziyo.
Abyste nepoškvrnili země, v níž jste. Nebo krev taková poškvrnila by země, aniž také země očištěna býti může od krve, kteráž jest vylita na ní, jediné krví toho, kterýž vylil ji.
34 Choncho musadetse dziko limene mukukhalamo, dziko limene Inenso ndimakhalamo, pakuti Ine Yehova, ndimakhala pakati pa Aisraeli.’”
Protož nepoškvrňujte země, v kteréž bydlíte, kdežto já přebývám; nebo já Hospodin přebývám u prostřed synů Izraelských.

< Numeri 35 >