< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Awurade ka kyerɛɛ Mose sɛ,
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
“Ka kyerɛ Israelfoɔ no sɛ, ‘Sɛ mobɛduru Kanaan asase no so a, asase a mede rema mo sɛ mo ankasa asase no a, sɛi na mo ahyeɛ bɛyɛ:
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
“‘Asase no anafoɔ fam no bɛyɛ Sin ɛserɛ so a ɛda Edom ano. Anafoɔ hyeɛ no ano bɛfiri Nkyene Ɛpo no.
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
Ɛbɛtoa so akɔtra Akrabbim wɔ anafoɔ hɔ a ɛrekɔ Sin no. Nʼanafoɔ pa ara no bɛyɛ Kades-Barnea, na ɛfiri hɔ akɔsi Hasarada de akɔwie Asmon.
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
Ɛfiri Asmon a, ɛhyeɛ no bɛkɔ ara akɔsi Misraim asuwa no mu na ano akɔpem Po Kɛseɛ no ano.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
Mo hyeɛ a ɛwɔ atɔeɛ no bɛyɛ Po Kɛseɛ a ɛda hɔ no.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
Mo hyeɛ a ɛda atifi no bɛfiti aseɛ wɔ Po Kɛseɛ no ano, na atoa so akɔ apueeɛ fam akɔsi bepɔ Hor,
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
de akɔ Lebo Hamat na akɔ Sedad
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
ne Sifron akɔ Hasar-Enan.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
Apueeɛ hyeɛ no bɛfiri Hasar-Enan anafoɔ akɔ Sefam
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
akɔsi Ribla wɔ Ain apueeɛ fam. Ɛfiri hɔ a, ɛbɛkɔ akɔpem Kineret ɛpo no wɔ apueeɛ fam,
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
na asiane afiri Asubɔnten Yordan, na akɔpem Nkyene Ɛpo no. “‘Sɛdeɛ mo asase ahyeɛ teɛ nie.’”
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
Afei Mose ka kyerɛɛ Israelfoɔ no sɛ, “Yei ne asase a mobɛbɔ so ntonto akyekyɛ afa no. Awurade ahyɛ sɛ mmusua nkron ne fa a aka no na wɔbɛkyekyɛ mu afa.
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
Ruben ne Gad mmusuakuo no ne Manase abusua fa no deɛ, wɔama wɔn asase no bi
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
wɔ Yordan apueeɛ fam a ɛne Yeriko di nhwɛanimu no.”
16 Yehova anawuza Mose kuti,
Awurade ka kyerɛɛ Mose sɛ,
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
“Nnipa a wɔn edin didi so yi na mayi wɔn sɛ wɔnkyekyɛ asase no mu: ɔsɔfoɔ Eleasa, Nun babarima Yosua.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
Yi abusua biara mu ɔpanin baako na ɔmmoa wɔn nni saa dwuma yi.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
“Wɔn edin na ɛdidi soɔ yi: “Yuda abusuakuo ntuanoni, Yefune babarima Kaleb;
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
Simeon abusuakuo ntuanoni, Amihud babarima Semuel;
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
Benyamin abusuakuo ntuanoni, Kislon babarima Elidad;
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
Dan abusuakuo ntuanoni, Yogli babarima Buki;
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
Yosef babarima Manase abusuakuo ntuanoni, Efod babarima Haniel;
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
Yosef babarima Efraim abusuakuo ntuanoni, Siftan babarima Kemuel;
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
Parknak babarima Elisafan, Sebulon abusuakuo ntuanoni;
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
Asan babarima Paltiel, Isakar abusuakuo ntuanoni;
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
Selomi babarima Ahihud, Aser abusuakuo ntuanoni;
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
Amihud babarima Pedahel, Naftali abusuakuo ntuanoni.”
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
Saa nnipa yi na Awurade yii wɔn sɛ wɔnhwɛ nkyekyɛ Kanaan asase no mu mma Israelfoɔ no.

< Numeri 34 >