< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahvé habló a Moisés, diciendo:
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
“Manda a los hijos de Israel y diles: ‘Cuando lleguéis a la tierra de Canaán (ésta es la tierra que os corresponderá en herencia, la tierra de Canaán según sus límites),
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
vuestro límite sur será desde el desierto de Zin a lo largo del lado de Edom, y vuestro límite sur será desde el extremo del Mar Salado hacia el este.
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
Tu frontera girará hacia el sur de la subida de Acrabim, y pasará por Zin; y pasará por el sur de Cades Barnea; y de allí irá a Hasar Adar, y pasará por Asmón.
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
La frontera girará desde Asmón hasta el arroyo de Egipto, y terminará en el mar.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
“‘Para la frontera occidental, tendrás el gran mar y su frontera. Esta será tu frontera occidental.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
“‘Esta será vuestra frontera del norte: desde el gran mar os marcaréis el monte Hor.
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
Desde el monte Hor marcaréis hasta la entrada de Hamat, y la frontera pasará por Zedad.
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
Luego la frontera irá hasta Zifrón, y terminará en Hazar Enán. Esta será vuestra frontera norte.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
“‘Marcarás tu frontera oriental desde Hazar Enán hasta Sefam.
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
La frontera bajará desde Sefam hasta Ribla, al lado oriental de Ain. La frontera descenderá y llegará hasta el lado del mar de Cineret, hacia el este.
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
La frontera bajará hasta el Jordán y terminará en el Mar Salado. Esta será tu tierra según sus límites alrededor”.
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
Moisés ordenó a los hijos de Israel diciendo: “Esta es la tierra que heredaréis por sorteo, que Yahvé ha ordenado dar a las nueve tribus y a la media tribu;
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
porque la tribu de los hijos de Rubén según las casas de sus padres, la tribu de los hijos de Gad según las casas de sus padres y la media tribu de Manasés han recibido su herencia.
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
Las dos tribus y la media tribu han recibido su herencia al otro lado del Jordán, en Jericó, hacia el este, hacia la salida del sol.”
16 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahvé habló a Moisés diciendo:
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
“Estos son los nombres de los hombres que te repartirán la tierra en herencia El sacerdote Eleazar y Josué, hijo de Nun.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
Tomarás un príncipe de cada tribu para repartir la tierra en herencia.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
Estos son los nombres de los hombres: De la tribu de Judá, Caleb hijo de Jefone.
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
De la tribu de los hijos de Simeón, Semuel hijo de Amiud.
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
De la tribu de Benjamín, Elidad hijo de Quislón.
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
De la tribu de los hijos de Dan, un príncipe, Buqui hijo de Jogli.
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
De los hijos de José: de la tribu de los hijos de Manasés, un príncipe, Haniel hijo de Efod.
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
De la tribu de los hijos de Efraín, un príncipe, Kemuel hijo de Siftán.
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
De la tribu de los hijos de Zabulón, un príncipe: Elizafán, hijo de Parnac.
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
De la tribu de los hijos de Isacar, un príncipe: Paltiel, hijo de Azán.
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
De la tribu de los hijos de Aser, un príncipe: Ahiud, hijo de Selomi.
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
De la tribu de los hijos de Neftalí un príncipe, Pedael hijo de Amiud”.
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
Estos son los que Yahvé mandó a repartir la herencia a los hijos de Israel en la tierra de Canaán.

< Numeri 34 >