< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Und Jehovah redete zu Mose und sprach:
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
Gebiete den Söhnen Israels und sprich zu ihnen: So ihr in das Land Kanaan kommet, so sei das das Land, das euch zum Erbe fällt, das Land Kanaan nach seinen Grenzen.
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
Und die Ecke im Mittag soll euch sein von der Wüste Zin an bei der Seite Edom, eure Mittagsgrenze soll sein vom Ende des Salzmeeres nach Osten zu.
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
Und es wendet sich euch die Grenze herum mittäglich von Maaleh Akkrabin und zieht sich nach Zin hinüber; und ihre Ausgänge seien mittäglich von Kadesch Barnea und gehen aus nach Chazar Addar und ziehen sich hinüber nach Azmon;
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
Und von Azmon wende sich die Grenze herum nach dem Bache Ägyptens, und ihre Ausgänge seien nach dem Meere hin.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
Und die Grenze nach dem Meere zu soll euch sein das große Meer und seine Grenze. Dies soll euch die Grenze nach dem Meere zu sein.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
Und die Grenze nach Mitternacht soll euch diese sein: Von dem großen Meere sollt ihr euch abmessen bis zum Berge Hor;
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
Vom Berge Hor sollt ihr abmessen bis man gen Hamath kommt, und sollen sein die Ausgänge der Grenze bis nach Zedad hin.
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
Und die Grenze gehe dann aus gen Siphron und ihre Ausgänge seien Chazar Enan. Dies soll euch die Grenze nach Mitternacht sein.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
Und messet ab für euch als Grenze gegen Osten von Chazar Enan bis Schepham.
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
Und die Grenze gehe hinab von Schepham nach Riblah östlich von Ain und die Grenze gehe hinab und stoße auf das Ufer des Meeres Kinnereth gegen den Osten.
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
Und die Grenze gehe hinab nach dem Jordan und ihre Ausgänge seien das Salzmeer. Das sei euch das Land nach seinen Grenzen ringsumher.
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
Und Mose gebot den Söhnen Israels und sprach: Dies ist das Land, das ihr unter euch durch das Los zum Erbe verteilen sollt, das Jehovah gebot zu geben den neun Stämmen und dem halben Stamm.
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
Denn es haben genommen der Stamm der Söhne des Rubeniten nach dem Hause ihrer Väter und der Stamm der Söhne des Gaditen nach dem Hause ihrer Väter und der halbe Stamm Menaschehs - sie haben ihr Erbe genommen.
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
Die zwei Stämme und der halbe Stamm haben ihr Erbe genommen diesseits des Jordans bei Jericho auf der Ostseite gegen den Aufgang.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
Und Jehovah redete zu Mose und sprach:
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Das sind die Namen der Männer, welche euch das Land zum Erbe verteilen sollen: Eleasar, der Priester, und Jehoschua, der Sohn Nuns.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
Und je einen Fürsten von dem Stamme sollt ihr nehmen, das Land als Erbe zu verteilen.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
Und das sind die Namen der Männer: Vom Stamme Judah Kaleb, der Sohn Jephunnehs.
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
Und vom Stamme der Söhne Schimeons Schemuel, Sohn Ammihuds.
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
Vom Stamme Benjamins Elidad, der Sohn Chislons.
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
Und vom Stamme der Söhne Dans ein Fürst, Bukki, Joglis Sohn.
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
Für die Söhne Josephs vom Stamme der Söhne Menaschehs ein Fürst, Hanniel, Ephods Sohn.
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
Und vom Stamme der Söhne Ephraims ein Fürst, Kemuel, ein Sohn Schiphtans.
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
Und vom Stamme der Söhne Sebuluns ein Fürst, Elizaphan, Parnachs Sohn.
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
Und vom Stamme der Söhne Issaschars ein Fürst, Paltiel, Assans Sohn.
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
Und vom Stamme der Söhne Aschers, ein Fürst, Achihud, Schelomis Sohn.
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
Und vom Stamme der Söhne Naphthalis ein Fürst, Pedahel, der Sohn Ammihuds.
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
Diese sind es, denen Jehovah gebot, den Söhnen Israels das Erbe zu verteilen im Lande Kanaan.

< Numeri 34 >