< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
L'Éternel parla à Moïse, et dit:
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
Donne cet ordre aux enfants d`Israël, et dis-leur: Lorsque vous entrerez dans le pays de Canaan, le pays qui vous sera donné en héritage, le pays de Canaan, selon ses limites,
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
votre quart méridional partira du désert de Tsin, le long du côté d`Édom, et votre limite méridionale partira de l`extrémité de la mer Salée, à l`orient.
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
Votre frontière tournera au sud de la montée d'Akrabbim, et passera à Tsin; elle passera au sud de Kadès Barnea; de là, elle ira à Hazar Addar, et passera à Azmon.
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
La frontière tournera depuis Azmon vers le ruisseau d'Égypte, et s'arrêtera à la mer.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
"'Pour la frontière occidentale, tu auras la grande mer et son bord. Ce sera ta frontière occidentale.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
« Voici quelle sera votre limite septentrionale: depuis la grande mer, vous tracerez pour vous la montagne de Hor.
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
De la montagne de Hor, vous marquerez l'entrée de Hamath, et la frontière passera par Zedad.
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
Puis la frontière ira jusqu'à Ziphron, et se terminera à Hazar Enan. Ce sera votre frontière nord.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
Tu délimiteras ta frontière orientale de Hazar Enan à Shepham.
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
La frontière descendra de Shepham à Riblah, à l'est d'Ain. La limite descendra et s'étendra jusqu'au bord de la mer de Chinnereth, à l'est.
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
La frontière descendra jusqu'au Jourdain et se terminera à la mer Salée. Tel sera votre pays, selon les frontières qui l'entourent. »
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
Moïse donna cet ordre aux enfants d'Israël: Voici le pays dont vous hériterez par le sort, et que l'Éternel a ordonné de donner aux neuf tribus et à la demi-tribu.
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
La tribu des fils de Ruben, selon les maisons de leurs pères, la tribu des fils de Gad, selon les maisons de leurs pères, et la demi-tribu de Manassé, ont reçu leur héritage.
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
Les deux tribus et la demi-tribu ont reçu leur héritage au-delà du Jourdain, à Jéricho, à l'est, vers le soleil levant. »
16 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahvé parla à Moïse, et dit:
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Voici les noms des hommes qui vous partageront le pays en héritage: Le prêtre Éléazar et Josué, fils de Nun.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
Tu prendras un prince de chaque tribu, pour partager le pays en héritage.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
Voici les noms de ces hommes: Pour la tribu de Juda: Caleb, fils de Jephunné.
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
Pour la tribu des fils de Siméon: Shemuel, fils d'Ammihud.
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
pour la tribu de Benjamin: Elidad, fils de Chislon
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
pour la tribu des fils de Dan: un prince, Bukki, fils de Jogli
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
Pour les fils de Joseph: de la tribu des fils de Manassé, le prince Hanniel, fils d'Ephod.
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
pour la tribu des fils d'Éphraïm: le prince Kemuel, fils de Shiphtan
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
pour la tribu des fils de Zabulon: le prince Elizaphan, fils de Parnach
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
pour la tribu des fils d'Issacar, le prince Paltiel, fils d'Azzan.
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
pour la tribu des fils d'Aser, le prince Ahihud, fils de Shelomi
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
pour la tribu des fils de Nephthali, le prince Pedahel, fils d'Ammihud ».
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
Tels sont ceux à qui Yahvé ordonna de faire le partage de l'héritage des enfants d'Israël dans le pays de Canaan.

< Numeri 34 >