< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the LORD spoke to Moses, saying,
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
Command the children of Israel, and say to them, When ye come into the land of Canaan; (this is the land that shall fall to you for an inheritance, even the land of Canaan with its borders: )
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
Then your south quarter shall be from the wilderness of Zin along by the border of Edom, and your south border shall be the outmost coast of the salt sea eastward:
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
And your border shall turn from the south to the ascent of Akrabbim, and pass on to Zin: its border shall be from the south to Kadeshbarnea, and shall go on to Hazaraddar, and pass on to Azmon:
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
And the border shall form a circuit from Azmon to the river of Egypt, and the border of it shall be at the sea.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
And as for the western border, ye shall even have the great sea for a border: this shall be your west border.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
And this shall be your north border: from the great sea ye shall mark out for you mount Hor:
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
From mount Hor ye shall mark out your border to the entrance of Hamath; and the edge of the border shall be at Zedad:
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
And the border shall go on to Ziphron, and the border of it shall be at Hazarenan: this shall be your north border.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
And ye shall mark out your east border from Hazarenan to Shepham:
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
And the border shall go down from Shepham to Riblah, on the east side of Ain; and the border shall descend, and shall reach to the side of the sea of Chinnereth eastward:
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
And the border shall go down to Jordan, and the border of it shall be at the salt sea: this shall be your land with its border on all sides.
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
And Moses commanded the children of Israel, saying, This is the land which ye shall inherit by lot, which the LORD commanded to give to the nine tribes, and to the half tribe:
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
For the tribe of the children of Reuben according to the house of their fathers, and the tribe of the children of Gad according to the house of their fathers, have received their inheritance; and half the tribe of Manasseh have received their inheritance:
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
The two tribes and the half tribe have received their inheritance on this side of Jordan near Jericho eastward, toward the sunrising.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
And the LORD spoke to Moses, saying,
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
These are the names of the men who shall divide the land to you: Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
And ye shall take one prince of every tribe, to divide the land by inheritance.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
And the names of the men are these: Of the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh.
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
And of the tribe of the children of Simeon, Shemuel the son of Ammihud.
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
Of the tribe of Benjamin, Elidad the son of Chislon.
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
And the prince of the tribe of the children of Dan, Bukki the son of Jogli.
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
The prince of the children of Joseph, for the tribe of the children of Manasseh, Hanniel the son of Ephod.
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
And the prince of the tribe of the children of Ephraim, Kemuel the son of Shiphtan.
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
And the prince of the tribe of the children of Zebulun, Elizaphan the son of Parnach.
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
And the prince of the tribe of the children of Issachar, Paltiel the son of Azzan.
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
And the prince of the tribe of the children of Asher, Ahihud the son of Shelomi.
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
And the prince of the tribe of the children of Naphtali, Pedahel the son of Ammihud.
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
These are they whom the LORD commanded to divide the inheritance to the children of Israel in the land of Canaan.

< Numeri 34 >