< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
Command [the] people of Israel and you will say to them if you [are] about to go into the land Canaan this [is] the land which it will fall to you an inheritance [the] land of Canaan to borders its.
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
And it will be of you [the] side of [the] south from [the] wilderness of Zin on [the] hands of Edom and it will be of you border of [the] southward from [the] end of [the] Sea of Salt east-ward.
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
And it will turn of you the border from [the] south to [the] ascent of scorpions and it will pass on Zin towards (and they will be *Q(K)*) extremities its from [the] south of Kadesh Barnea and it will go out Hazar Addar and it will pass on Azmon towards.
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
And it will turn the border from Azmon [the] wadi of towards Egypt and they will be extremities its the sea towards.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
And [the] border of [the] west and it will be for you the sea great and a border this it will be of you border of [the] west.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
And this it will be of you border of [the] north from the sea great you will mark out for yourselves Hor the mountain.
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
From Hor the mountain you will mark out Lebo Hamath and they will be [the] extremities of the border Zedad towards.
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
And it will go out the border Ziphron towards and they will be extremities its Hazar Enan this it will be of you border of [the] north.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
And you will mark for yourselves for [the] border of east-ward from Hazar Enan Shepham towards.
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
And it will go down the border from Shepham Riblah from [the] east of Ain and it will go down the border and it will reach to [the] shoulder of [the] sea of Kinnereth east-ward.
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
And it will go down the border the Jordan towards and they will be extremities its [the] Sea of Salt this it will be of you the land to borders its all around.
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
And he commanded Moses [the] people of Israel saying this [is] the land which you will inherit it by lot which he has commanded Yahweh to give to [the] nine the tribes and [the] half of the tribe.
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
For they have taken [the] tribe of [the] descendants of the Reubenite[s] to [the] house of ancestors their and [the] tribe of [the] descendants of the Gadite[s] to [the] house of ancestors their and [the] half of [the] tribe of Manasseh they have taken inheritance their.
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
[the] two The tribes and [the] half of the tribe they have taken inheritance their from [the] other side of [the] Jordan of Jericho east-ward east-ward.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
These [are] [the] names of the men who they will give as inheritance to you the land Eleazar the priest and Joshua [the] son of Nun.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
And a leader one a leader one from a tribe you will take to give as inheritance the land.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
And these [are] [the] names of the men of [the] tribe of Judah Caleb [the] son of Jephunneh.
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
And of [the] tribe of [the] descendants of Simeon Shemuel [the] son of Ammihud.
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
Of [the] tribe of Benjamin Elidad [the] son of Chislon.
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
And of [the] tribe of [the] descendants of Dan a leader Bukki [the] son of Jogli.
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
Of [the] sons of Joseph of [the] tribe of [the] descendants of Manasseh a leader Hanniel [the] son of Ephod.
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
And of [the] tribe of [the] descendants of Ephraim a leader Kemuel [the] son of Shiphtan.
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
And of [the] tribe of [the] descendants of Zebulun a leader Elizaphan [the] son of Parnach.
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
And of [the] tribe of [the] descendants of Issachar a leader Paltiel [the] son of Azzan.
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
And of [the] tribe of [the] descendants of Asher a leader Ahihud [the] son of Shelomi.
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
And of [the] tribe of [the] descendants of Naphtali a leader Pedahel [the] son of Ammihud.
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
These [are those] whom he commanded Yahweh to apportion as an inheritance to [the] people of Israel in [the] land of Canaan.

< Numeri 34 >