< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
YHWH spoke to Moses, saying,
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
"Command the children of Israel, and tell them, 'When you come into the land of Canaan (this is the land that shall fall to you for an inheritance, even the land of Canaan according to its borders),
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
then your south quarter shall be from the wilderness of Zin along by the side of Edom, and your south border shall be from the end of the Salt Sea eastward;
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
and your border shall turn about southward of the ascent of Akrabbim, and pass along to Zin; and the goings out of it shall be southward of Kadesh Barnea; and it shall go forth to Hazar Addar, and pass along to Azmon;
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
and the border shall turn about from Azmon to the Wadi of Egypt, and the goings out of it shall be at the sea.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
"'For the western border, the Great Sea shall be a border to you; this shall be your west border.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
"'This shall be your north border: from the Great Sea you shall mark out for you Mount Hor;
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
from Mount Hor you shall mark out to Lebo Hamath; and the goings out of the border shall be at Zedad;
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
and the border shall go forth to Ziphron, and the goings out of it shall be at Hazar Enan: this shall be your north border.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
"'You shall mark out your east border from Hazar Enan to Shepham;
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
and the border shall go down from Shepham to Riblah, on the east side of Ain; and the border shall go down, and shall reach to the side of the sea of Kinnereth eastward;
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
and the border shall go down to the Jordan, and the goings out of it shall be at the Salt Sea. This shall be your land according to its borders around it.'"
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
Moses commanded the children of Israel, saying, "This is the land which you shall inherit by lot, which YHWH has commanded to give to the nine tribes, and to the half-tribe;
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
for the tribe of the people of Reuben according to their fathers' houses, and the tribe of the people of Gad according to their fathers' houses, have received, and the half-tribe of Manasseh have received, their inheritance:
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
the two tribes and the half-tribe have received their inheritance beyond the Jordan at Jericho eastward, toward the sunrise."
16 Yehova anawuza Mose kuti,
YHWH spoke to Moses, saying,
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
"These are the names of the men who shall divide the land to you for inheritance: Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
You shall take one prince of every tribe, to divide the land for inheritance.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
These are the names of the men: Of the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh.
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
Of the tribe of the people of Simeon, Shemuel the son of Ammihud.
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
Of the tribe of Benjamin, Elidad the son of Chislon.
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
Of the tribe of the people of Dan a prince, Bukki the son of Jogli.
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
Of the people of Joseph: of the tribe of the people of Manasseh a prince, Hanniel the son of Ephod.
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
Of the tribe of the people of Ephraim a prince, Kemuel the son of Shiphtan.
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
Of the tribe of the people of Zebulun a prince, Elizaphan the son of Parnach.
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
Of the tribe of the people of Issachar a prince, Paltiel the son of Azzan.
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
Of the tribe of the people of Asher a prince, Ahihud the son of Shelomi.
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
Of the tribe of the people of Naphtali a prince, Pedahel the son of Ammihud."
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
These are they whom YHWH commanded to divide the inheritance to the children of Israel in the land of Canaan.

< Numeri 34 >