< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
Command the sons of Israel, and say to them, When ye come into the land of Canaan (this is the land that shall fall to you for an inheritance, even the land of Canaan according to the borders of it),
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
then your south quarter shall be from the wilderness of Zin along by the side of Edom. And your south border shall be from the end of the Salt Sea eastward.
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
And your border shall turn about southward of the ascent of Akrabbim, and pass along to Zin. And the goings out of it shall be southward of Kadesh-barnea. And it shall go forth to Hazar-addar, and pass along to Azmon.
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
And the border shall turn about from Azmon to the brook of Egypt, and the goings out of it shall be at the sea.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
And for the western border, ye shall have the great sea and the border of it. This shall be your west border.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
And this shall be your north border: From the great sea ye shall mark out for you mount Hor.
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
From mount Hor ye shall mark out to the entrance of Hamath. And the goings out of the border shall be at Zedad.
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
And the border shall go forth to Ziphron, and the goings out of it shall be at Hazar-enan. This shall be your north border.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
And ye shall mark out your east border from Hazar-enan to Shepham.
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
And the border shall go down from Shepham to Riblah, on the east side of Ain. And the border shall go down, and shall reach to the side of the sea of Chinnereth eastward.
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
And the border shall go down to the Jordan, and the goings out of it shall be at the Salt Sea. This shall be your land according to the borders of it round about.
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
And Moses commanded the sons of Israel, saying, This is the land which ye shall inherit by lot, which Jehovah has commanded to give to the nine tribes, and to the half-tribe.
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
For the tribe of the sons of Reuben according to their fathers' houses, and the tribe of the children of Gad according to their fathers' houses, have received, and the half-tribe of Manasseh have received, their inheritance.
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
The two tribes and the half-tribe have received their inheritance beyond the Jordan at Jericho eastward, toward the sunrise.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
These are the names of the men who shall divide the land to you for inheritance: Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
And ye shall take one ruler of every tribe, to divide the land for inheritance.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
And these are the names of the men: Of the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh.
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
And of the tribe of the sons of Simeon, Shemuel the son of Ammihud.
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
Of the tribe of Benjamin, Elidad the son of Chislon.
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
And of the tribe of the sons of Dan a ruler, Bukki the son of Jogli.
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
Of the sons of Joseph: of the tribe of the sons of Manasseh a ruler, Hanniel the son of Ephod,
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
and of the tribe of the sons of Ephraim a ruler, Kemuel the son of Shiphtan.
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
And of the tribe of the sons of Zebulun a ruler, Elizaphan the son of Parnach.
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
And of the tribe of the sons of Issachar a ruler, Paltiel the son of Azzan.
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
And of the tribe of the sons of Asher a ruler, Ahihud the son of Shelomi.
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
And of the tribe of the sons of Naphtali a ruler, Pedahel the son of Ammihud.
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
These are those whom Jehovah commanded to divide the inheritance to the sons of Israel in the land of Canaan.

< Numeri 34 >