< Numeri 34 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
Byd Israelitterne og sig til dem: Når i kommer til Kana'ans Land det er det Land, der skal tilfalde eder som Arvelod, Kana'ans Land i hele dets Udstrækning
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
så skal eders Sydside strække sig fra Zins Ørken langs med Edom; eders Sydgrænse skal mod Øst begynde ved Enden af Salthavet;
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
så skal eders Grænse dreje sønden om Akrabbimpasset, nå til Zin og ende sønden for Kadesj Barnea; så skal den løbe hen til Hazar Addar øg nå til Azmon;
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
fra Azmon skal Grænsen dreje hen til Ægyptens Bæk og ende ved Havet.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
Hvad Vestgrænsen angår, skal det store Hav være eders Grænse; det skal være eders Vestgrænse.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
Eders Nordgrænse skal være følgende: Fra det store Hav skal I udstikke eder en Linie til Bjerget Hor;
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
fra Bjerget Hor skal I udstikke en Linie til Egnen hen imod Hamat, så at Grænsen ender ved Zedad;
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
derpå skal Grænsen gå til Zifron og ende ved Hazar Enan. Det skal være eders Nordgrænse.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
Men til Østgrænse skal I afmærke eder en Linie fra Hazar Enan til Sjefam;
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
og fra Sjefam skal Grænsen gå ned til Ribla østen for Ajin, og Grænsen skal løbe videre ned, til den støder til Bjergskrænten østen for Kinneretsøen;
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
derpå skal Grænsen løbe ned langs Jordan og ende ved Salthavet. Det skal være eders Land i hele dets Udstrækning til alle Sider.
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
Og Moses bød Israelitterne og sagde: Det er det Land, I skal udskifte mellem eder ved Lodkastning, og som efter HERRENs Bud skal gives de ni Stammer og den halve Stamme.
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
Thi Rubeniternes Stamme efter deres Fædrenehuse og Gaditernes Stamme efter deres Fædrenehuse og Manasses halve Stamme har allerede fået deres Arvelod.
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
De to Stammer og den halve Stamme har fået deres Arvelod hinsides Jordan over for Jeriko, mod Øst, mod Solens Opgang.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
Og HERREN talede til Moses og sagde:
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Navnene på de Mænd, der skal udskifte Landet mellem eder, er følgende: Præsten Eleazar og Josua, Nuns Søn;
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
desuden skal I udtage een Øverste af hver Stamme til at udskifte Landet.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
Navnene på disse Mænd er følgende: Af Judas Stamme Kaleb, Jefunnes Søn,
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
af Simeoniternes Stamme Sjemuel, Ammihuds Søn,
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
af Benjamins Stamme Elidad, Kislons Søn,
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
af Daniternes Stamme een Øverste, Bukki, Joglis Søn,
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
af Josefs Sønner: af Manassiternes Stamme een Øverste, Hanniel, Efods Søn,
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
og af Efraimiternes Stamme een Øverste, Kemuel, Sjiftans Søn,
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
af Zebuloniternes Stamme een Øverste, Elizafan, Parnaks Søn,
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
af Issakariternes Stamme een Øverste, Paltiel, Azzans Søn,
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
af Aseriternes Stamme een Øverste, Ahihud, Sjelomis Søn,
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
og af Naftaliternes Stamme een Øverste, Pedael, Ammibuds Søn.
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
Det var dem, HERREN pålagde at udskifte Kana'ans Land mellem Israelitterne.

< Numeri 34 >