< Numeri 34 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi, řka:
2 “Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
Přikaž synům Izraelským a rci jim: Když vejdete do země Kanán, (tať jest země, kteráž se dostane vám v dědictví, země Kananejská s pomezími svými),
3 “‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
Strana polední vaše bude poušť Tsin vedlé pomezí Edomských; a bude vaše pomezí polední od břehu moře slaného k východu.
4 Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
A zatočí se to pomezí polední k Maleakrabim, a půjde až k Tsin, a potáhne se od poledne přes Kádesbarne; a odtud vyjde ke vsi Addar, a vztáhne se až k Asmon.
5 kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
Od Asmon zatočí se pomezí to vůkol až ku potoku Egyptskému, a tu se skonávati bude k západu.
6 “‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
Pomezí pak západní budete míti moře veliké; to bude vaše pomezí západní.
7 “‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
A pomezí půlnoční toto míti budete: Od moře velikého vyměříte sobě k hoře řečené Hor.
8 ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
Od hory Hor vyměříte sobě, až kde se vchází do Emat, a skonávati se bude pomezí to u Sedad.
9 ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
A odtud půjde pomezí to k Zefronu, a konec jeho u vsi Enan; to bude pomezí vaše k straně půlnoční.
10 “‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
Vyměříte sobě také pomezí k východu od vsi Enan až do Sefama.
11 Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
A od Sefama schýlí se to pomezí až k Reblata, od východu maje Ain; a schýlí se pomezí to, a přijde k straně moře Ceneret k východu.
12 Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
A vztáhne se to pomezí k Jordánu, a bude konec jeho u slaného moře. Ta země vaše bude po svých pomezích vůkol.
13 Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
Tedy oznámil to Mojžíš synům Izraelským, řka: Ta jest země, kterouž dědičně obdržíte losem, jakož přikázal Hospodin, abych ji dal devateru pokolení a polovici pokolení Manassesova.
14 chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
Nebo vzalo pokolení synů Ruben po domích otců svých, a pokolení synů Gád po domích otců svých, a polovice pokolení Manassesova vzali dědictví své.
15 Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
Půl třetího pokolení vzali dědictví své před Jordánem proti Jerichu, k straně na východ slunce.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
Mluvil opět Hospodin k Mojžíšovi, řka:
17 “Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Tato jsou jména mužů, kteříž v dědictví rozdělí vám zemi: Eleazar kněz, a Jozue, syn Nun.
18 Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
Kníže také jedno z každého pokolení vezmete k rozdělování dědictví země.
19 Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
A tato jsou jména mužů: Z pokolení Juda Kálef, syn Jefonův;
20 Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
Z pokolení synů Simeon Samuel, syn Amiudův;
21 Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
Z pokolení Beniaminova Helidad, syn Chaselonův;
22 Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
Z pokolení synů Dan kníže Bukci, syn Jogli;
23 Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
Z synů Jozefových z pokolení synů Manasses kníže Haniel, syn Efodův;
24 Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
Z pokolení synů Efraim kníže Kamuel, syn Seftanův;
25 Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
A z pokolení synů Zabulon kníže Elizafan, syn Farnachův;
26 Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
Z pokolení synů Izachar kníže Faltiel, syn Ozanův;
27 Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
A z pokolení synů Asser kníže Ahiud, syn Salonův;
28 Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
A z pokolení synů Neftalím kníže Fedael, syn Amiudův.
29 Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.
Ti jsou, jimž přikázal Hospodin, aby rozdělili země k dědictví synům Izraelským v zemi Kananejské.