< Numeri 33 >

1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
Nanka amalombolombo ohambo lwabako-Israyeli ekuphumeni kwabo eGibhithe ngamaviyo abo bekhokhelwa nguMosi lo-Aroni.
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
Ngokulaya kukaThixo waloba walonda izigaba zamalombolombo ohambo lwabo. Nantu uhambo lwabo ngezigaba zakhona:
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
Abako-Israyeli basuka eRamesesi ngosuku lwetshumi lanhlanu lwenyanga yakuqala, ngosuku kwedlule iPhasika. Baphuma ngesibindi bekhangelwe ngamaGibhithe wonke,
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
wona eyephathekile engcwaba wonke amazibulo awo, lawo ayebulewe nguThixo phakathi kwawo; ngoba uThixo wayehlulele ngokujezisa onkulunkulu bawo.
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
Abako-Israyeli basuka eRamesesi bayamisa izihonqo zabo eSukhothi.
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
Basuka eSukhothi bayamisa izihonqo zabo e-Ethamu, emaphethelweni enkangala.
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
Basuka e-Ethamu, baphenduka baya ePhi-Hahirothi; beqonda empumalanga yaseBhali-Zefoni, babuye njalo bamisa izihonqo zabo eMigidoli.
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
Basuka ePhi-Hahirothi badabula olwandle bangena enkangala, bathi sebehambe okwensuku ezintathu enkangala ye-Ethamu, bamisa izihonqo zabo eMara.
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
Basuka eMara baya e-Elimi, lapho okwakulezintombo zamanzi ezilitshumi lambili kanye lezihlahla zohlobo lwelala ezingamatshumi ayisikhombisa, bafika bamisa izihonqo khonapho.
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
Basuka e-Elimi bayamisa izihonqo zabo besekele uLwandle oluBomvu.
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
Basuka oLwandle oluBomvu bayamisa enkangala yaseSini.
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
Basuka enkangala yeSini bayamisa eDofuka.
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
Basuka eDofuka bayamisa e-Alusha.
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
Basuka e-Alusha bayamisa eRefidimu, lapho okwakungelamanzi okunathwa ngabantu.
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
Basuka eRefidimu bayamisa enkangala yeSinayi.
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
Basuka enkangala yeSinayi bayamisa eKhibhrothi Hathava.
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
Basuka eKhibhrothi Hathava bayamisa eHazerothi.
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
Basuka eHazerothi bayamisa eRithima.
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
Basuka eRithima bayamisa eRimoni-Pherezi.
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
Basuka eRimoni-Pherezi bayamisa eLibhina.
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
Basuka eLibhina bayamisa eRisa.
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
Basuka eRisa bayamisa eKhehelatha.
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
Basuka eKhehelatha bayamisa eNtabeni yaseShefa.
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
Basuka eNtabeni yaseShefa bayamisa eHarada.
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
Basuka eHarada bayamisa eMakhelothi.
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
Basuka eMakhelothi bayamisa eThahathi.
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
Basuka eThahathi bayamisa eThera.
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
Basuka eThera bayamisa eMithika.
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
Basuka eMithika bayamisa eHashimona.
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
Basuka eHashimona bayamisa eMosera.
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
Basuka eMosera bayamisa eBhene Jayakhani.
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
Basuka eBhene Jayakhani bayamisa eHori-Hagidigadi.
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
Basuka eHori-Hagidigadi bayamisa eJothibhatha.
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
Basuka eJothibhatha bayamisa e-Abhurona.
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
Basuka e-Abhurona bayamisa e-Eziyoni-Gebheri.
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
Basuka e-Eziyoni-Gebheri bayamisa eKhadeshi, eNkangala yaseZini.
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
Basuka eKhadeshi bayamisa eNtabeni yaseHori, emngceleni wase-Edomi.
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
Ngokulaya kukaThixo, u-Aroni umphristi wakhwela eNtabeni yaseHori, lapho afela khona ngosuku lwakuqala lwenyanga yesihlanu yomnyaka wamatshumi amane emva kokuphuma kwabako-Israyeli eGibhithe.
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
U-Aroni wayeseleminyaka elikhulu elileminyaka engamatshumi amabili lemithathu yokuphila ekufeni kwakhe eNtabeni yaseHori.
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
Inkosi yase-Aradi engumKhenani eyayihlala eNegebi yaseKhenani, yezwa ukuthi abako-Israyeli babesiza.
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
Basuka eNtabeni yaseHori bayamisa eZalimona.
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
Basuka eZalimona bayamisa ePhunoni.
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
Basuka ePhunoni bayamisa e-Obhothi.
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
Basuka e-Obhothi bayamisa e-Iye-Abharimi, emngceleni waseMowabi.
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
Basuka e-Iye-Abharimu bayamisa eDibhoni Gadi.
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
Basuka eDibhoni Gadi bayamisa e-Alimoni-Dibhilathayimi.
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
Basuka e-Alimoni-Dibhilathayimi bayamisa ezintabeni zase-Abharimi, phansi kweNebho.
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
Basuka ezintabeni zase-Abharimi bayamisa emagcekeni aseMowabi besekele uJodani ngaphetsheya malungana leJerikho.
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
Khonapho emagcekeni aseMowabi bamisa izihonqo zabo belandela umfula uJodani kusukela eBhethi-Jeshimothi kusiya e-Abheli-Shithima.
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
Emagcekeni aseMowabi ngasemfuleni uJodani ngaphetsheya uvelela ngaseJerikho uThixo wathi kuMosi,
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
“Khuluma kwabako-Israyeli ubatshele lokhu uthi: ‘Nxa lichapha uJodani lingena eKhenani,
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
xotshani phambi kwenu bonke abahlala kulelolizwe. Dilizani zonke izithombe zabo ezibaziweyo kanye lezibunjiweyo, njalo libhidlize zonke izindawo eziphakemeyo zokukhonzela.
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
Thumbani ilizwe lelo lihlale kulo, ngoba ngilinike ukuthi libe ngelenu.
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
Yabelanani ilizwe ngenkatho, kusiya ngokwensendo zenu. Ixuku elikhulu kaliphiwe isabelo esikhulu, kuthi ixuku elincinyane liphiwe isabelo esincinyane. Okuzakuya kubo ngenkatho akube ngokwabo. Kwabelananeni kusiya ngezizwana zabokhokho benu.
55 “‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
Kodwa nxa lingaxotshanga abahlala kulelolizwe, abaseleyo babo bazakuba lukhophe emehlweni enu njalo babe ngameva enyameni yenu. Bazakuba luhlupho ezweni elizahlala kulo.
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”
Ngakho-ke ngizakwenza kini lokho engizimisele ukukwenza kubo.’”

< Numeri 33 >