< Numeri 33 >

1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
Hae sunt mansiones filiorum Israel, qui egressi sunt de Aegypto per turmas suas in manu Moysi et Aaron,
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
quas descripsit Moyses iuxta castrorum loca, quae Domini iussione mutabant.
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
Profecti igitur de Ramesse mense primo, quintadecima die mensis primi, fecerunt altera die Phase filii Israel in manu excelsa videntibus cunctis Aegyptiis,
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
et sepelientibus primogenitos, quos percusserat Dominus (nam et in diis eorum exercuerat ultionem)
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
castrametati sunt in Soccoth.
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
Et de Soccoth venerunt in Etham, quae est in extremis finibus solitudinis.
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
Inde egressi venerunt contra Phihahiroth, quae respicit Beelsephon, et castrametati sunt ante Magdalum.
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
Profectique de Phihahiroth, transierunt per medium mare in solitudinem: et ambulantes tribus diebus per desertum Etham, castrametati sunt in Mara.
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
Profectique de Mara venerunt in Elim, ubi erant duodecim fontes aquarum, et palmae septuaginta: ibique castrametati sunt.
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
Sed et inde egressi, fixerunt tentoria super Mare rubrum. Profectique de Mari rubro,
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
castrametati sunt in deserto Sin.
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
Unde egressi, venerunt in Daphca.
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
Profectique de Daphca, castrametati sunt in Alus.
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
Egressique de Alus, in Raphidim fixere tentoria, ubi populo defuit aqua ad bibendum.
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
Profectique de Raphidim, castrametati sunt in deserto Sinai.
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
Sed et de solitudine Sinai egressi, venerunt ad sepulchra concupiscentiae.
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
Profectique de sepulchris concupiscentiae, castrametati sunt in Haseroth.
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
Et de Haseroth venerunt in Rethma.
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
Profectique de Rethma, castrametati sunt in Remmomphares.
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
Unde egressi venerunt in Lebna.
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
De Lebna castrametati sunt in Ressa.
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
Egressique de Ressa, venerunt in Ceelatha.
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
Unde profecti castrametati sunt in monte Sepher.
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
Egressi de monte Sepher, venerunt in Arada.
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
Inde proficiscentes, castrametati sunt in Maceloth.
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
Profectique de Maceloth, venerunt in Thahath.
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
De Thahath castrametati sunt in Thare.
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
Unde egressi, fixere tentoria in Methca.
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
Et de Methca castrametati sunt in Hesmona.
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
Profectique de Hesmona, venerunt in Moseroth.
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
Et de Moseroth castrametati sunt in Beneiaacan.
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
Profectique de Beneiaacan, venerunt in montem Gadgad.
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
Unde profecti, castrametati sunt in Ietebatha.
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
Et de Ietebatha venerunt in Hebrona.
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
Egressique de Hebrona, castrametati sunt in Asiongaber.
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
Inde profecti, venerunt in desertum Sin, haec est Cades.
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
Egressique de Cades, castrametati sunt in monte Hor, in extremis finibus Terrae Edom.
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
Ascenditque Aaron sacerdos in montem Hor iubente Domino: et ibi mortuus est anno quadragesimo egressionis filiorum Israel ex Aegypto, mense quinto, prima die mensis,
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
cum esset annorum centum viginti trium.
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
Audivitque Chananaeus rex Arad, qui habitabat ad meridiem, in Terram Chanaan venisse filios Israel.
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
Et profecti de monte Hor, castrametati sunt in Salmona.
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
Unde egressi, venerunt in Phunon.
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
Profectique de Phunon, castrametati sunt in Oboth.
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
Et de Oboth, venerunt in Ieabarim, quae est in finibus Moabitarum.
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
Profectique de Ieabarim, fixere tentoria in Dibongad.
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
Unde egressi, castrametati sunt in Helmondeblathaim.
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
Egressique de Helmondeblathaim, venerunt ad montes Abarim contra Nabo.
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
Profectique de montibus Abarim, transierunt ad campestria Moab, supra Iordanem contra Iericho.
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
Ibique castrametati sunt de Bethsimoth usque ad Abelsatim in planioribus locis Moabitarum,
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
ubi locutus est Dominus ad Moysen:
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
Praecipe filiis Israel, et dic ad eos: Quando transieritis Iordanem, intrantes Terram Chanaan,
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
disperdite cunctos habitatores Terrae illius: confringite titulos, et statuas comminuite, atque omnia excelsa vastate,
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
mundantes terram, et habitantes in ea. ego enim dedi vobis illam in possessionem,
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
quam dividetis vobis sorte. Pluribus dabitis latiorem, et paucioribus angustiorem. Singulis ut sors ceciderit, ita tribuetur hereditas. Per tribus et familias possessio dividetur.
55 “‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
Sin autem nolueritis interficere habitatores Terrae: qui remanserint, erunt vobis quasi clavi in oculis, et lanceae in lateribus, et adversabuntur vobis in Terra habitationis vestrae:
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”
et quidquid illis cogitaveram facere, vobis faciam.

< Numeri 33 >