< Numeri 33 >
1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
イスラエルの子孫がモーセとアロンに導かれ其軍旅にしたがひてエジプトの國より出きたりて經たる旅路は左のごとし
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
モーセ、ヱホバの命に依りその旅路にしたがひてこれが發程を記せりその發程によればその旅路は左のごとくなり
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
彼らは正月の十五日にラメセスより出立り即ぢ逾越の翌日にイスラエルの子孫は一切のエジプト人の目の前にて高らかなる手によりて出たり
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
時にエジプト人はヱホバに撃ころされし其長子を葬りて居りヱホバはまた彼らの神々にも罰をかうむらせたまへり
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
イスラエルの子孫ラメセスより出立てスコテに營を張り
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
スコテより出立て曠野の極端なるエタムに營を張り
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
エタムより出立てバアルゼポンの前なるピハヒロテに轉りゆきてミグドルに營を張り
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
ピハヒロテの前より出立ち海の中を通りて曠野にいりエタムの曠野に三日路ほど入てメラに營を張り
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
メラより出立てヱリムに至れりエリムには泉十二棕櫚七十本あり乃ち此に營を張り
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
かくてエリムより出たちて紅海の邊に營を張り
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
紅海より出たちてシンの曠野に營を張り
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
シンの曠野より出たちてドフカに營を張り
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
ドフカより出たちてアルシに營を張り
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
アルシより出たちてレピデムに營を張り此には民の飮む水あらざりき
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
かくてレピデムより出たちてシナイの曠野に營を張り
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
シナイの曠野より出たちてキブロテハッタワに營を張り
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
キブロテハッタワより出たちてハゼロテに營を張り
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
ハゼロテより出たちてリテマに營を張り
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
リテマより出たちてリンモンバレツに營を張り
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
リンモンパレツより出たちてリブナに營を張り
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
リブナより出たちてリッサに營を張り
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
リッサより出たちてケヘラタに營を張り
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
ケヘラタより出たちてシヤペル山に營を張り
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
シヤペル山より出たちてハラダに營を張り
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
ハラダより出たちてマケロテに營を張り
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
マケロテより出たちてタハテに營を張り
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
タハテより出たちてテラに營を張り
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
テラより出たちてミテカに營を張り
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
ミテカより出たちてハシモナに營を張り
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
ハシモナより出たちてモセラに營を張り
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
モセラより出たちてベネヤカンに營を張り
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
ベネヤカンより出たちてホルハギデガデに營を張り
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
ホルハギデガデより出たちてヨテバタに營を張り
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
ヨテバタより出たちてアブロナに營を張り
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
アブロナより出たちてエジオングベルに營を張り
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
エジオングベルより出たちてカデシのチンの曠野に營を張り
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
カデシより出たちてエドムの國の界なるホル山に營を張り
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
イスラエルの子孫がエジプトの國を出てより四十年の五月の朔日に祭司アロンはヱホバの命によりてホル山に登て其處に死り
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
アロンはホル山に死たる時は百二十三歳なりき
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
カナンの地の南に住るカナン人アラデ王といふ者イスラエルの子孫の來るを聞り
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
かくてホル山より出たちてザルモナに營を張り
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
ザルモナより出立てプノンに營を張り
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
プノンより出たちてオボテに營を張り
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
オボテより出たちてモアブの界なるイヱアバリムに營を張り
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
イヰムより出たちてデボンガドに營を張り
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
デボンガドより出たちてアルモンデブラタイムに營を張り
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
アルモンデブラタイムより出たちてネボの前なるアバリムの山々に營を張り
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
アバリムの山々より出たちてヱリコに對するヨルダンの邊なるモアブの平野に營を張り
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
すなはちモアブの平野においてヨルダンの邊に營を張りベテヱシモテよりアベルシッテムにいたる
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
ヱリコに對するヨルダンの邊なるモアブの平野においてヱホバ、モーセに告て言たまはく
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
イスラエルの子孫に告てこれに言へ汝らヨルダンを濟りてカナンの地に入る時は
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
その地に住る民をことごとく汝らの前より逐はらひその石の像をことごとく毀ちその鋳たる像を毀ちその崇邱をことごとく毀ちつくすべし
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
汝らその地の民を逐はらひて其處に住べし其は我その地を汝らの產業として汝らに與へたればなり
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
汝らの族にしたがひ鬮をもてその地を分ちて產業となし人多きには多くの產業を與へ人少きには少しの產業を與ふべし各人の分はその鬮にあたれる處にあるべきなり汝らその先祖の支派にしたがひて之を獲べし
55 “‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
然ど汝らもしその地に住る民を汝らの前より逐はらはずば汝らが存しおくところの者汝らの目に莿となり汝の脇に棘となり汝らの住む國において汝らを惱さん
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”
且また我は彼らに爲んと思ひし事を汝らに爲ん