< Numeri 33 >
1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
१जब से इस्राएली मूसा और हारून की अगुआई में दल बाँधकर मिस्र देश से निकले, तब से उनके ये पड़ाव हुए।
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
२मूसा ने यहोवा से आज्ञा पाकर उनके कूच उनके पड़ावों के अनुसार लिख दिए; और वे ये हैं।
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
३पहले महीने के पन्द्रहवें दिन को उन्होंने रामसेस से कूच किया; फसह के दूसरे दिन इस्राएली सब मिस्रियों के देखते बेखटके निकल गए,
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
४जबकि मिस्री अपने सब पहिलौठों को मिट्टी दे रहे थे जिन्हें यहोवा ने मारा था; और उसने उनके देवताओं को भी दण्ड दिया था।
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
५इस्राएलियों ने रामसेस से कूच करके सुक्कोत में डेरे डाले।
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
६और सुक्कोत से कूच करके एताम में, जो जंगल के छोर पर है, डेरे डाले।
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
७और एताम से कूच करके वे पीहहीरोत को मुड़ गए, जो बाल-सपोन के सामने है; और मिग्दोल के सामने डेरे खड़े किए।
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
८तब वे पीहहीरोत के सामने से कूच कर समुद्र के बीच होकर जंगल में गए, और एताम नामक जंगल में तीन दिन का मार्ग चलकर मारा में डेरे डाले।
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
९फिर मारा से कूच करके वे एलीम को गए, और एलीम में जल के बारह सोते और सत्तर खजूर के वृक्ष मिले, और उन्होंने वहाँ डेरे खड़े किए।
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
१०तब उन्होंने एलीम से कूच करके लाल समुद्र के तट पर डेरे खड़े किए।
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
११और लाल समुद्र से कूच करके सीन नामक जंगल में डेरे खड़े किए।
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
१२फिर सीन नामक जंगल से कूच करके उन्होंने दोपका में डेरा किया।
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
१३और दोपका से कूच करके आलूश में डेरा किया।
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
१४और आलूश से कूच करके रपीदीम में डेरा किया, और वहाँ उन लोगों को पीने का पानी न मिला।
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
१५फिर उन्होंने रपीदीम से कूच करके सीनै के जंगल में डेरे डाले।
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
१६और सीनै के जंगल से कूच करके किब्रोतहत्तावा में डेरा किया।
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
१७और किब्रोतहत्तावा से कूच करके हसेरोत में डेरे डाले।
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
१८और हसेरोत से कूच करके रित्मा में डेरे डाले।
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
१९फिर उन्होंने रित्मा से कूच करके रिम्मोनपेरेस में डेरे खड़े किए।
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
२०और रिम्मोनपेरेस से कूच करके लिब्ना में डेरे खड़े किए।
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
२१और लिब्ना से कूच करके रिस्सा में डेरे खड़े किए।
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
२२और रिस्सा से कूच करके कहेलाता में डेरा किया।
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
२३और कहेलाता से कूच करके शेपेर पर्वत के पास डेरा किया।
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
२४फिर उन्होंने शेपेर पर्वत से कूच करके हरादा में डेरा किया।
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
२५और हरादा से कूच करके मखेलोत में डेरा किया।
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
२६और मखेलोत से कूच करके तहत में डेरे खड़े किए।
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
२७और तहत से कूच करके तेरह में डेरे डाले।
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
२८और तेरह से कूच करके मित्का में डेरे डाले।
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
२९फिर मित्का से कूच करके उन्होंने हशमोना में डेरे डाले।
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
३०और हशमोना से कूच करके मोसेरोत में डेरे खड़े किए।
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
३१और मोसेरोत से कूच करके याकानियों के बीच डेरा किया।
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
३२और याकानियों के बीच से कूच करके होर्हग्गिदगाद में डेरा किया।
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
३३और होर्हग्गिदगाद से कूच करके योतबाता में डेरा किया।
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
३४और योतबाता से कूच करके अब्रोना में डेरे खड़े किए।
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
३५और अब्रोना से कूच करके एस्योनगेबेर में डेरे खड़े किए।
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
३६और एस्योनगेबेर से कूच करके उन्होंने सीन नामक जंगल के कादेश में डेरा किया।
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
३७फिर कादेश से कूच करके होर पर्वत के पास, जो एदोम देश की सीमा पर है, डेरे डाले।
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
३८वहाँ इस्राएलियों के मिस्र देश से निकलने के चालीसवें वर्ष के पाँचवें महीने के पहले दिन को हारून याजक यहोवा की आज्ञा पाकर होर पर्वत पर चढ़ा, और वहाँ मर गया।
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
३९और जब हारून होर पर्वत पर मर गया तब वह एक सौ तेईस वर्ष का था।
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
४०और अराद का कनानी राजा, जो कनान देश के दक्षिण भाग में रहता था, उसने इस्राएलियों के आने का समाचार पाया।
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
४१तब इस्राएलियों ने होर पर्वत से कूच करके सलमोना में डेरे डाले।
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
४२और सलमोना से कूच करके पूनोन में डेरे डाले।
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
४३और पूनोन से कूच करके ओबोत में डेरे डाले।
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
४४और ओबोत से कूच करके अबारीम नामक डीहों में जो मोआब की सीमा पर हैं, डेरे डाले।
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
४५तब उन डीहों से कूच करके उन्होंने दीबोन-गाद में डेरा किया।
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
४६और दीबोन-गाद से कूच करके अल्मोनदिबलातैम में डेरा किया।
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
४७और अल्मोनदिबलातैम से कूच करके उन्होंने अबारीम नामक पहाड़ों में नबो के सामने डेरा किया।
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
४८फिर अबारीम पहाड़ों से कूच करके मोआब के अराबा में, यरीहो के पास यरदन नदी के तट पर डेरा किया।
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
४९और उन्होंने मोआब के अराबा में बेत्यशीमोत से लेकर आबेलशित्तीम तक यरदन के किनारे-किनारे डेरे डाले।
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
५०फिर मोआब के अराबा में, यरीहो के पास की यरदन नदी के तट पर, यहोवा ने मूसा से कहा,
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
५१“इस्राएलियों को समझाकर कह: जब तुम यरदन पार होकर कनान देश में पहुँचो
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
५२तब उस देश के निवासियों को उनके देश से निकाल देना; और उनके सब नक्काशीदार पत्थरों को और ढली हुई मूर्तियों को नाश करना, और उनके सब पूजा के ऊँचे स्थानों को ढा देना।
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
५३और उस देश को अपने अधिकार में लेकर उसमें निवास करना, क्योंकि मैंने वह देश तुम्हीं को दिया है कि तुम उसके अधिकारी हो।
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
५४और तुम उस देश को चिट्ठी डालकर अपने कुलों के अनुसार बाँट लेना; अर्थात् जो कुल अधिकवाले हैं उन्हें अधिक, और जो थोड़ेवाले हैं उनको थोड़ा भाग देना; जिस कुल की चिट्ठी जिस स्थान के लिये निकले वही उसका भाग ठहरे; अपने पितरों के गोत्रों के अनुसार अपना-अपना भाग लेना।
55 “‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
५५परन्तु यदि तुम उस देश के निवासियों को अपने आगे से न निकालोगे, तो उनमें से जिनको तुम उसमें रहने दोगे, वे मानो तुम्हारी आँखों में काँटे और तुम्हारे पांजरों में कीलें ठहरेंगे, और वे उस देश में जहाँ तुम बसोगे, तुम्हें संकट में डालेंगे।
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”
५६और उनसे जैसा बर्ताव करने की मनसा मैंने की है वैसा ही तुम से करूँगा।”