< Numeri 33 >

1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
These are the mansions of the children of Israel, who went out of Egypt by their troops under the conduct of Moses and Aaron,
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
Which Moses wrote down according to the places of their encamping, which they changed by the commandment of the Lord.
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
Now the children of Israel departed from Ramesses the first month, on the fifteenth day of the first month, the day after the phase, with a mighty hand, in the eight of all the Egyptians,
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
Who were burying their firstborn, whom the Lord had slain (upon their gods also he had executed vengeance, )
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
And they camped in Soccoth.
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
And from Soccoth they came into Etham, which is in the uttermost borders of the wilderness.
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
Departing from thence they came over against Phihahiroth, which looketh towards Beelsephon, and they camped before Magdalum.
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
And departing from Phihahiroth, they passed through the midst of the sea into the wilderness: and having marched three days through the desert of Etham, they camped in Mara.
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
And departing from Mara, they came into Elim, where there were twelve fountains of waters, and seventy palm trees: and there they camped.
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
But departing from thence also, they pitched their tents by the Red Sea. And departing from the Red Sea,
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
They camped in the desert of Sin.
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
And they removed from thence, and came to Daphca.
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
And departing from Daphca, they camped in Alus.
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
And departing from Alus, they pitched their tents in Raphidim, where the people wanted water to drink.
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
And departing from Raphidim, they camped in the desert of Sinai.
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
But departing also from the desert of Sinai, they came to the graves of lust.
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
And departing from the graves of lust, they camped in Haseroth.
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
And from Haseroth they came to Rethma.
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
And departing from Rethma, they camped in Remmomphares.
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
And they departed from thence and came to Lebna.
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
Removing from Lebna they camped in Ressa.
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
And departing from Ressa, they came to Ceelatha.
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
And they removed from thence and camped in the mountain Sepher.
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
Departing from the mountain Sepher, they came to Arada.
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
From thence they went and camped in Maceloth.
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
And departing from Maceloth, they came to Thahath.
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
Removing from Thahath they camped in Thare.
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
And they departed from thence, and pitched their tents in Methca.
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
And removing from Methca, they camped in Hesmona.
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
And departing from Hesmona, they came to Moseroth.
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
And removing from Moseroth, they camped in Benejaacan.
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
And departing from Benejaacan, they came to mount Gadgad.
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
From thence they went and camped in Jetebatha.
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
And from Jetebatha they came to Hebrona.
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
And departing from Hebrona, they camped in Asiongaber.
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
They removed from thence and came into the desert of Sin, which is Cades.
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
And departing from Cades, they camped in mount Her, in the uttermost borders of the land of Edom.
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
And Aaron the priest went up into mount Hor at the commandment of the Lord: and there he died in the fortieth year of the coming forth of the children of Israel out of Egypt, the fifth month, the first day of the month,
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
When he was a hundred and twenty-three years old.
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
And king Arad the Chanaanite, who dwelt towards the south, heard that the children of Israel were come to the land of Chanaan.
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
And they departed from mount Her, and camped in Salmona.
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
From whence they removed and came to Phunon.
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
And departing from Phunon, they camped in Oboth.
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
And from Oboth they came to Ijeabarim, which is in the borders of the Moabites.
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
And departing from Ijeabarim they pitched their tents in Dibongab.
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
From thence they went and camped in Helmondeblathaim.
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
And departing from Helmondeblathaim, they came to the mountains of Abarim over against Nabo.
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
And departing from the mountains of Abarim, they passed to the plains of Moab, by the Jordan, over against Jericho.
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
And there they camped from Bethsi moth even to Ablesatim in the plains of the Moabites,
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
Where the Lord said to Moses:
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
Command the children of Israel, and say to them: When you shall have passed over the Jordan, entering into the land of Chanaan,
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
Destroy all the inhabitants of that land: beat down their pillars, and break in pieces their statues, and waste all their high places,
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
Cleansing the land, and dwelling in it. For I have given it you for a possession.
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
And you shall divide it among you by lot. To the more you shall give a larger part, and to the fewer a lesser. To every one as the lot shall fall, so shall the inheritance be given. The possession shall be divided by the tribes and the families.
55 “‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
But if you will not kill the inhabitants of the land: they that remain, shall be unto you as nails in your eyes, and spears in your sides, and they shall be your adversaries in the land of your habitation.
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”
And whatsoever I had thought to do to them, I will do to you.

< Numeri 33 >