< Numeri 33 >

1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
Tato jsou tažení synů Izraelských, kteříž vyšli z země Egyptské po houfích svých, pod spravou Mojžíše a Arona.
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
Sepsal pak Mojžíš vycházení jejich podlé toho, jakž táhli k rozkazu Hospodinovu. Tato jsou tedy vycházení jejich podlé toho, jakž táhli.
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
Nejprv z Ramesses jdouce prvního měsíce, v patnáctý den téhož prvního měsíce, nazejtří po slavnosti Fáze vyšli synové Izraelští v ruce silné před očima všech Egyptských,
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
Kdyžto Egyptští pochovávali všecky prvorozené, kteréž zbil Hospodin mezi nimi, a při bozích jejich vykonal Hospodin soudy své.
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
Hnuvše se tedy synové Izraelští z Ramesses, položili se v Sochot.
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
Potom hnuvše se z Sochot, položili se v Etam, jenž jest při kraji pouště.
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
A hnuvše se z Etam, navrátili se zase k Fiarot, jenž jest před Belsefon, a položili se před Magdalem.
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
A hnuvše se z Fiarot, šli prostředkem moře na poušť, a ušedše tří dnů cesty po poušti Etam, položili se v Marah.
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
Jdouce pak z Marah, přišli do Elim, kdežto bylo dvanácte studnic vod, a sedmdesáte palm. I položili se tu.
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
A hnuvše se z Elim, položili se u moře Rudého.
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
Potom hnuvše se od moře Rudého, položili se na poušti Sin.
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
A když se hnuli z pouště Sin, položili se v Dafka.
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
A hnuvše se z Dafka, položili se v Halus.
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
Hnuvše se pak z Halus, rozbili stany v Rafidim, kdežto lid neměl vody ku pití.
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
A hnuvše se z Rafidim, položili se na poušti Sinai.
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
Hnuvše se pak z pouště Sinai, položili se v Kibrot Hattáve.
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
A když se hnuli z Kibrot Hattáve, položili se v Hazerot.
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
Hnuvše se pak z Hazerot, položili se v Retma.
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
A z Retma hnuvše se, položili se v Remmon Fáres.
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
Potom hnuvše se z Remmon Fáres, položili se v Lebna.
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
A hnuvše se z Lebna, položili se v Ressa.
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
A hnuvše se z Ressa, položili se v Cehelot.
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
Z Cehelot pak hnuvše se, položili se na hoře Sefer.
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
A když se hnuli s hory Sefer, položili se v Arad.
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
A hnuvše se z Arad, položili se v Machelot.
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
Potom hnuvše se z Machelot, položili se v Tahat.
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
A hnuvše se z Tahat, položili se v Tár.
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
A když se hnuli z Tár, položili se v Metka.
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
A hnuvše se z Metka, položili se v Esmona.
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
Z Esmona pak hnuvše se, položili se v Moserot.
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
A když se hnuli z Moserot, položili se v Benejakan.
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
A hnuvše se z Benejakan, položili se v Chor Gidgad.
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
A hnuvše se z Chor Gidgad, položili se v Jotbata.
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
Když se pak hnuli z Jotbata, položili se v Habrona.
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
A z Habrona hnuvše se, položili se v Aziongaber.
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
A odtud hnuvše se, položili se na poušti Tsin, jenž jest Kádes.
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
A hnuvše se z Kádes, položili se na hoře řečené Hor, při končinách země Edomské.
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
Tu vstoupil Aron kněz na horu, jenž slove Hor, k rozkazu Hospodinovu, a umřel tam, léta čtyřidcátého po vyjití synů Izraelských z země Egyptské, v první den měsíce pátého.
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
A byl Aron ve stu ve dvadcíti a třech letech, když umřel na hoře Hor.
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
Uslyšel také Kananejský král v Arad, kterýž bydlil na poledne v zemi Kananejské, že by táhli synové Izraelští.
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
Tedy hnuvše se s hory Hor, položili se v Salmona.
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
A hnuvše se z Salmona, položili se v Funon.
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
Z Funon pak hnuvše se, položili se v Obot.
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
A když se hnuli z Obot, rozbili stany při pahrbcích hor Abarim, na pomezí Moábském.
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
Potom hnuvše se od těch pahrbků, položili se v Dibongad.
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
Z Dibongad hnuvše se, položili se v Helmondeblataim.
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
A když se hnuli z Helmondeblataim, položili se na horách Abarim proti Nébo.
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
Odšedše pak z hor Abarim, položili se na rovinách Moábských, při Jordánu proti Jerichu.
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
A rozbili stany při Jordánu, od Betsimot až do Abelsetim, na rovinách Moábských.
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
Mluvil pak Hospodin k Mojžíšovi na rovinách Moábských, při Jordánu naproti Jerichu, řka:
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
Mluv k synům Izraelským a rci jim: Když přejdete Jordán, a vejdete do země Kananejské,
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
Vyžeňte všecky obyvatele země té od tváři vaší, a zkazte všecky rytiny jejich; i všecky obrazy slité jejich zkazte, všecky také výsosti jejich zbořte.
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
A když vyženete obyvatele země, bydliti budete v ní; nebo vám jsem dal tu zemi, abyste jí dědičně vládli.
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
Kteroužto rozdělíte sobě k dědictví losem, vedlé čeledí svých. Kterých jest více, těm větší dědictví dáte, kterých pak jest méně, těm menší dědictví dáte. Na kterém místě komu los padne, to jemu bude; podlé pokolení otců svých dědictví dosáhnete.
55 “‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
Pakli nevyženete obyvatelů země od tváři své, tedy ti, kterýchž zanecháte, budou vám jako trní v očích vašich, a jako ostnové po bocích vašich, a budou vás ssužovati na zemi, na kteréž vy bydliti budete.
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”
A na to přijde, abych to, což jsem jim umínil učiniti, vám učinil.

< Numeri 33 >