< Numeri 33 >

1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
以下是以色列子民在梅瑟和亞郎指揮下,分隊出離埃及國後所行的路程。
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
梅瑟記錄了他們遵上主的命啟營的出發點。以下是他們依次出發的行程:
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
他們於正月十五日由辣默色斯起程,即在逾越節第二日,以色列子民大膽地、當著眾埃及人的面出走了,
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
其時埃及人正在埋葬上主在他們中所擊殺的一切長子;上主也懲罰了他們的神祇。
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
以色列子民由辣默色斯起程,在酥苛特紮營。
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
由穌苛特起程,在位於曠野邊界的厄堂紮營。
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
由厄堂起程,轉向巴耳責豐的丕哈希洛特,在米革多耳對面紮營。
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
由丕哈希洛特起程,由海中經過進入曠野,在厄堂曠野中行了三天的路,然後在瑪辣紮營。
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
由瑪辣起程,來到厄林。在厄林有十二水泉和七十株棕櫚樹,就在那裡紮營。
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
由厄林起程,在紅海旁紮營。
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
由紅海起程,在欣曠野紮營。
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
由欣曠野啟程,在多弗卡紮營。
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
由多弗卡起程,在阿路士紮營。
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
由阿路士起程,在勒非丁紮營;民眾在這裡沒有水喝。
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
由勒非丁起程,在西乃曠野裡紮營。
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
由西乃曠野起程,在克貝洛特哈塔瓦紮營。
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
由克貝洛特哈塔瓦起程,在哈責洛特紮營。
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
由哈責洛特起程,在黎特瑪紮營。
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
由黎特瑪起程,在黎孟培勒茲紮營。
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
由黎孟培勒茲起程,在里貝納紮營。
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
由里貝納起程,在黎撒紮營。
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
由黎撒起程,在刻黑拉達紮營。
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
由刻黑拉達起程,在舍斐爾山紮營。
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
由舍斐爾山起程,在哈辣達紮營。
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
由哈辣達起程,在瑪刻黑羅特紮營。
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
由瑪刻黑羅特起程,在塔哈特紮營。
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
由塔哈特起程,在特辣黑紮營。
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
由特辣黑起程,在米特卡紮營。
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
由米特卡起程,在哈市摩納紮營。
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
由哈市摩納起程,在摩色爾紮營。
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
由摩色爾起程,在貝乃雅干紮營。
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
由貝乃雅干起程,在曷爾哈基加得紮營。
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
由曷爾哈基加得起程,在約特巴達紮營。
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
由約特巴達起程,在阿貝洛納紮營。
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
由阿貝洛納起程,在厄茲雍革貝爾紮營。
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
由厄茲雍革貝爾起程,在親曠野,即卡德士紮營。
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
由卡德士起程,在位於厄東地邊界上的曷爾山下紮營。
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
亞郎大司祭依上主的命,上了曷爾山,死在那裡,時在以色列子民出埃及國後四十年五月初一日。
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
亞郎死在曷爾山上時,已一百二十三歲。
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
其時住在客納罕南部的客納罕人王阿辣得聽說以色列子民來了。
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
它們再由曷爾山下起程,在匝耳摩納紮營。
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
由匝耳摩納起程,在普農紮營。
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
由普農起程,在敖波特紮營。
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
由敖波特起程,在位於摩阿布邊境的依因阿巴陵紮營。
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
由依因起程,在狄朋加得紮營。
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
由狄朋加得起程,在阿耳孟狄貝拉塔因紮營。
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
由阿耳孟狄貝拉塔因起程,在乃波前面的阿巴陵山地內紮營。
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
由阿巴陵山地起程,在耶里哥對面,約但河邊,摩阿布曠野紮營;
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
他們在摩阿布曠野裡,沿著約但河邊紮營,由貝特耶史摩特直到阿貝耳史廷。
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
在耶里哥對面,約但河邊,摩阿布曠野內,上主訓示梅瑟說:「
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
你告訴以色列子民說:你們幾時過了約但,進入客納罕地,
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
應由你們面前驅逐當地所有的居民,應毀壞他們的一切偶像,應打碎他們的一切鑄像,應鏟除他們的一切丘壇。
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
你們要佔領那地方,住在那裡,因為我已將那裡給了你們叫你們佔有。
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
你們要按支派抽籤分配那地方:人數多的多給,人數少的少給。誰的籤落在那裡,那裡就屬於他。你們依照宗祖支派分配你們的產業。
55 “‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
但如果你們不把當地的居民由你們面前驅逐,那留下的居民,必要成為你們的眼中刺,腰間針,在你們住的地方內迫害你們;
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”
並且我打算了怎樣對待他們,也要怎樣對待你們。」

< Numeri 33 >