< Numeri 32 >

1 Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
و بنی روبین و بنی جاد را مواشی بی نهایت بسیار و کثیر بود، پس چون زمین یعزیر و زمین جلعاد را دیدند که اینک این مکان، مکان مواشی است.۱
2 Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
بنی جاد و بنی روبین نزد موسی و العازار کاهن و سروران جماعت آمده، گفتند:۲
3 “Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
«عطاروت و دیبون و یعزیر و نمره و حشبون و العاله و شبام و نبو و بعون،۳
4 dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
زمینی که خداوند پیش روی جماعت اسرائیل مفتوح ساخته است، زمین مواشی است، و بندگانت صاحب مواشی می‌باشیم.۴
5 Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
پس گفتند: اگر درنظر تو التفات یافته‌ایم، این زمین به بندگانت به ملکیت داده شود، و ما را از اردن عبور مده.»۵
6 Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
موسی به بنی جاد و بنی روبین گفت: «آیابرادران شما به جنگ روند و شما اینجا بنشینید؟۶
7 Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
چرا دل بنی‌اسرائیل را افسرده می‌کنید تا به زمینی که خداوند به ایشان داده است، عبورنکنند؟۷
8 Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
به همین طور پدران شما عمل نمودند، وقتی که ایشان را از قادش برنیع برای دیدن زمین فرستادم.۸
9 Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
به وادی اشکول رفته، زمین را دیدند ودل بنی‌اسرائیل را افسرده ساختند تا به زمینی که خداوند به ایشان داده بود، داخل نشوند.۹
10 Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
پس غضب خداوند در آن روز افروخته شد به حدی که قسم خورده، گفت:۱۰
11 ‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
البته هیچکدام ازمردانی که از مصر بیرون آمدند از بیست ساله وبالاتر آن زمین را که برای ابراهیم و اسحاق ویعقوب قسم خوردم، نخواهند دید، چونکه ایشان مرا پیروی کامل ننمودند.۱۱
12 Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
سوای کالیب بن یفنه قنزی و یوشع بن نون، چونکه ایشان خداوند را پیروی کامل نمودند.۱۲
13 Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
پس غضب خداوند بر اسرائیل افروخته شده، ایشان را چهل سال در بیابان آواره گردانید، تا تمامی آن گروهی که این شرارت را در نظر خداوند ورزیده بودند، هلاک شدند.۱۳
14 “Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
و اینک شما به‌جای پدران خودانبوهی از مردان خطاکار برپا شده‌اید تا شدت غضب خداوند را بر اسرائیل باز زیاده کنید؟۱۴
15 Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
زیرا اگر از پیروی او روبگردانید بار دیگرایشان را در بیابان ترک خواهد کرد و شما تمامی این قوم را هلاک خواهید ساخت.»۱۵
16 Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
پس ایشان نزد وی آمده، گفتند: «آغلها رااینجا برای مواشی خود و شهرها بجهت اطفال خویش خواهیم ساخت.۱۶
17 Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
و خود مسلح شده، حاضر می‌شویم و پیش روی بنی‌اسرائیل خواهیم رفت تا آنها را به مکان ایشان برسانیم. واطفال ما از ترس ساکنان زمین در شهرهای حصاردار خواهند ماند.۱۷
18 Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
و تا هر یکی ازبنی‌اسرائیل ملک خود را نگرفته باشد، به خانه های خود مراجعت نخواهیم کرد.۱۸
19 Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
زیرا که ما با ایشان در آن طرف اردن و ماورای آن ملک نخواهیم گرفت، چونکه نصیب ما به این طرف اردن به طرف مشرق به ما رسیده است.»۱۹
20 Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
و موسی به ایشان گفت: «اگر این کار رابکنید و خویشتن را به حضور خداوند برای جنگ مهیا سازید،۲۰
21 ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
و هر مرد جنگی از شما به حضورخداوند از اردن عبور کند تا او دشمنان خود را ازپیش روی خود اخراج نماید،۲۱
22 dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
و زمین به حضور خداوند مغلوب شود، پس بعد از آن برگردیده، به حضور خداوند و به حضور اسرائیل بی‌گناه خواهید شد، و این زمین از جانب خداوندملک شما خواهد بود.۲۲
23 “Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
و اگر چنین نکنید اینک به خداوند گناه ورزیده‌اید، و بدانید که گناه شما، شما را درخواهد گرفت.۲۳
24 Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
پس شهرها برای اطفال و آغلها برای گله های خود بنا کنید، و به آنچه از دهان شما درآمد، عمل نمایید.»۲۴
25 Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
پس بنی جاد و بنی روبین موسی را خطاب کرده، گفتند: «بندگانت به طوری که آقای مافرموده است، خواهیم کرد.۲۵
26 Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
اطفال و زنان ومواشی و همه بهایم ما اینجا در شهرهای جلعادخواهند ماند.۲۶
27 koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
و جمیع بندگانت مهیای جنگ شده، چنانکه آقای ما گفته است به حضورخداوند برای مقاتله عبور خواهیم نمود.»۲۷
28 Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
پس موسی العازار کاهن، و یوشع بن نون، وروسای خاندان آبای اسباط بنی‌اسرائیل را درباره ایشان وصیت نمود.۲۸
29 Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
و موسی به ایشان گفت: «اگر جمیع بنی جاد و بنی روبین مهیای جنگ شده، همراه شما به حضور خداوند از اردن عبورکنند، و زمین پیش روی شما مغلوب شود، آنگاه زمین جلعاد را برای ملکیت به ایشان بدهید.۲۹
30 Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
واگر ایشان مهیا نشوند و همراه شما عبور ننمایند، پس در میان شما در زمین کنعان ملک بگیرند.»۳۰
31 Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
بنی جاد و بنی روبین در جواب وی گفتند: «چنانکه خداوند به بندگانت گفته است، همچنین خواهیم کرد.۳۱
32 Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
ما مهیای جنگ شده، پیش روی خداوند به زمین کنعان عبور خواهیم کرد، و ملک نصیب ما به این طرف اردن داده شود.»۳۲
33 Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
پس موسی به ایشان یعنی به بنی جاد وبنی روبین و نصف سبط منسی ابن یوسف، مملکت سیحون، ملک اموریان و مملکت عوج ملک باشان را داد، یعنی زمین را با شهرهایش وحدود شهرهایش، زمین را از هر طرف.۳۳
34 Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
وبنی جاد، دیبون و عطاروت و عروعیر.۳۴
35 Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
وعطروت، شوفان و یعزیز و یجبهه.۳۵
36 Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
و بیت نمره و بیت هاران را بنا کردند یعنی شهرهای حصارداررا با آغلهای گله‌ها.۳۶
37 Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
و بنی روبین حشبون والیعاله و قریتایم.۳۷
38 Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
و نبو و بعل معون که نام این دورا تغییر دادند و سبمه را بنا کردند و شهرهایی راکه بنا کردند به نامها مسمی ساختند.۳۸
39 Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
وبنی ماکیر بن منسی به جلعاد رفته، آن را گرفتند واموریان را که در آن بودند، اخراج نمودند.۳۹
40 Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
وموسی جلعاد را به ماکیر بن منسی داد و او در آن ساکن شد.۴۰
41 Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
و یائیر بن منسی رفته، قصبه هایش راگرفت، و آنها را حووت یائیر نامید.۴۱
42 Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.
و نوبح رفته، قنات و دهاتش را گرفته، آنها را به اسم خودنوبح نامید.۴۲

< Numeri 32 >