< Numeri 32 >
1 Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
Forsothe the sones of Ruben and of Gad hadden many beestis, and catel with out noumbre was to hem, in werk beestis. And whanne thei hadden seyn Jazer and Galaad, couenable londis to beestis to be fed,
2 Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
thei camen to Moyses and Eleazar, preest, and to the princes of the multitude, and seiden,
3 “Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
Astaroth, and Dibon, and Jacer, and Nemra, Esebon, and Eleale, and Sabam,
4 dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
and Nebo, and Beon, the lond which the Lord smoot in the siyt of the sones of Israel, is of moost plenteuous cuntrey to the pasture of beestis; and we thi seruauntis han ful many beestis;
5 Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
and we preyen, if we han founde grace bifor thee, that thou yyue to vs thi seruauntis that cuntrey in to possessioun, and make not vs to passe Jordan.
6 Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
To whiche Moises answeride, Whether youre britheren schulen go to batel, and ye schulen sitte here?
7 Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
Whi peruerten ye the soulis of Israel, that thei doren not passe in to the place, which the Lord schal yyue to hem?
8 Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
Whether youre fadris diden not so, whanne Y sente fro Cades Barne to aspie the lond,
9 Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
and whanne thei camen to the valey of Clustre, whanne al the cuntrey was cumpassid, thei peruertiden the herte of the sones of Israel, that thei entriden not in to the coostis, whiche the Lord yaf to hem.
10 Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
And the Lord was wrooth, and swoor,
11 ‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
seiynge, Thes men that stieden fro Egipt, fro twenti yeer and aboue, schulen not se the lond which Y bihiyte vndur an ooth to Abraham, Isaac, and Jacob, and nolden sue me,
12 Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
outakun Caleph, Cenezei, the sone of Jephone, and Josue, the sone of Nun; these tweyne filliden my wille.
13 Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
And the Lord was wrooth ayens Israel, and ledde hym aboute the deseert bi fourti yeer, til al the generacioun was wastid, that hadde do yuel in the `siyt of the Lord.
14 “Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
And Moyses seide, Lo! ye encressyngis, and nurreis, `ether nurschid children, of synful men, han ryse for youre fadris, that ye schulden encreesse the strong veniaunce of the Lord ayens Israel.
15 Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
That if ye nylen sue the Lord, in `the wildirnesse he schal forsake the puple, and ye schulen be cause of the deeth of alle men.
16 Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
And thei neiyiden nyy, and seiden, We schulen make foldis of scheep, and the stablis of beestis, and we schulen make strengthid citees to oure litle children.
17 Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
Forsothe we vs silf schulen be armed `to defence, and schulen be gird `with armeris to asailyng, and schulen go to batel bifor the sones of Israel, til we bryngen hem in to her places; oure litle children and what euer thing we moun haue, schulen be in strengthid cytees, for the tresouns of the dwelleris.
18 Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
We schulen not turne ayen in to oure housis, til the sones of Israel welden her eritage;
19 Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
and we schulen not axe ony thing ouer Jordan, for we han now oure possessioun in the eest coost therof.
20 Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
To whiche Moises seide, If ye doen that, that ye biheten, be ye maad redi, and go ye to batel bifor the Lord;
21 ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
and ech man fiytere be armed, and passe Jordan, til the Lord distrye hise enemyes,
22 dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
and al the lond be maad suget to hym; thanne ye schulen be giltles anentis God, and anentis Israel, and ye schulen holde the cuntreys, whiche ye wolen, bifor the Lord.
23 “Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
But if ye doon not that, that ye seien, it is not doute to ony man, that ne ye synnen ayens God; and wite ye, that youre synne schal take you.
24 Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
Therfor bilde ye citees to youre litle children, and foldis and stablis to scheep, and to beestis; and fille ye that, that ye bihiyten.
25 Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
And the sones of Gad and of Ruben seiden to Moises, We ben thi seruauntis; we schulen do that, that oure lord comaundith.
26 Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
We schulen leeue oure litle children, and wymmen, and scheep, and beestis in the citees of Galaad;
27 koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
forsothe alle we thi seruauntis schulen go redi to batel, as thou, lord, spekist.
28 Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
Therfor Moyses comaundide to Eleazar, preest, and to Josue, the sone of Nun, and to the princes of meynees, bi the lynagis of Israel, and seide to hem,
29 Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
If the sones of Gad, and the sones of Ruben goen alle armed with you, to batel bifor the Lord, and the lond be maad suget to you, yyue ye to hem Galaad in to possessioun;
30 Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
but if thei nylen passe with you in to the lond of Chanaan, take thei places to dwelle among you.
31 Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
And the sones of Gad and the sones of Ruben answeriden, As the Lord spak to hise seruauntis, so we schulen do;
32 Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
we schulen go armed bifor the Lord, in to the lond of Chanaan, and we knowlechen, that we han take now possessioun ouer Jordan.
33 Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
And so Moises yaf to the sones of Gad and of Ruben, and to half the lynage of Manasses, sone of Joseph, the rewme of Seon, kyng of Ammorey, and the rewme of Og, kyng of Basan, and `the lond of hem, with her citees, bi cumpas.
34 Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
Therfor the sones of Gad bildiden Dibon, and Astaroth, and Aroer,
35 Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
and Roth-Sophan, and Jazer, and Jebaa,
36 Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
and Beeth-Nemra, and Betharan, strengid citees; and foldis to her beestis.
37 Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
Forsothe the sones of Ruben bildiden Esebon, and Eleale, and Cariathiarym, and Nabo,
38 Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
and Balmeon, whanne the names weren turned, and thei bildiden Sabama; and puttiden names to the citees, whiche thei hadden bildid.
39 Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
Forsothe the sones of Machir, sone of Manasses, yeden in to Galaad, and distrieden it, and killiden Ammorei, enhabitere therof.
40 Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
Therfor Moises yaf the lond of Galaad to Machir, sone of Manasses, which Machir dwellide ther ynne.
41 Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
Forsothe Jair, the sone of Manasses, yede, and occupiede the townes therof, whiche he clepide Anochiair, that is, the townes of Jair.
42 Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.
Also Nobe yede, and took Canath, with hise townes, and clepide it, bi his name, Nobe.